Yobu 27 – CCL & HOF

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yobu 27:1-23

1Ndipo Yobu anapitiriza kuyankhula kwake:

2“Ndithu pali Mulungu wamoyo, amene wakana kundiweruza molungama,

Wamphamvuzonse, amene wawawitsa mtima wanga,

3nthawi zonse pamene ndili ndi moyo,

mpweya wa Mulungu uli mʼmphuno mwanga,

4pakamwa panga sipadzatuluka mawu oyipa,

lilime langa silidzayankhula zachinyengo.

5Sindidzavomereza kuti inu mukunena zoona;

mpaka imfa yanga, sindidzataya ungwiro wanga.

6Ndidzasunga chilungamo changa ndipo sindidzalola kuti chindichokere;

chikumbumtima changa sichidzanditsutsa nthawi yonse ya moyo wanga.

7“Mdani wanga akhale ngati woyipa,

wondiwukira akhale ngati munthu wosalungama!

8Nanga chiyembekezo cha munthu wosapembedza nʼchiyani pamene aphedwa,

pamene Mulungu achotsa moyo wake?

9Kodi Mulungu amamva kulira kwake

pamene zovuta zamugwera?

10Kodi adzapeza chikondwerero mwa Wamphamvuzonse?

Kodi adzapemphera kwa Mulungu nthawi zonse?

11“Ndidzakuphunzitsani za mphamvu ya Mulungu ndipo

sindidzabisa njira za Wamphamvuzonse.

12Inu mwadzionera nokha zonsezi.

Nanga bwanji mukuyankhula zopanda pake?

13“Pano pali chilango chimene Mulungu amasungira woyipa,

cholowa chimene munthu wankhanza amalandira kuchokera kwa Wamphamvuzonse.

14Angakhale ana ake achuluke chotani adzaphedwa ndi lupanga ndipo

zidzukulu zake zidzasowa zakudya.

15Amene adzatsalireko adzafa ndi mliri,

ndipo akazi awo amasiye sadzawalira.

16Ngakhale aunjike siliva ngati fumbi,

ndi kukundika zovala ngati mchenga,

17zimene wasungazo wolungama ndiye adzavale,

ndipo anthu osalakwa ndiwo adzagawane siliva wakeyo.

18Nyumba imene akuyimanga ili ngati mokhala kadziwotche,

ili ngati msasa umene mlonda amamanga.

19Amapita kokagona ali wolemera koma kutha kwake nʼkomweko;

akatsekula maso ake, chuma chake chonse chapita.

20Zoopsa zimamukokolola ngati madzi achigumula;

mphepo yamkuntho imamunyamula usiku.

21Mphepo ya kummawa imamuwulutsa ndipo iye saonekanso ndipo

imamuchotsa pamalo pake.

22Imakuntha pa iye osamuchitira chisoni,

pamene akuyesa kuthawa mphamvu zake mwaliwiro.

23Mphepoyo imamuwomba ndithu

ndipo kuchokera pamalo pake imamuopseza.”

Hoffnung für Alle

Hiob 27:1-23

Ich bin unschuldig!

1Hiob fuhr fort:

2»Das schwöre ich,

so wahr Gott, der Allmächtige, lebt,

der mir mein Recht verweigert

und mich bittere Stunden durchleiden lässt:

3Solange er mir den Atem gibt,

solange ich noch Leben in mir spüre,

4werde ich nie die Unwahrheit sagen,

kein betrügerisches Wort soll über meine Lippen kommen!

5Verflucht will ich sein,

wenn ich euch jemals recht gebe!

Bis zum letzten Atemzug bleibe ich dabei:

Ich bin unschuldig!

6Ich bin im Recht – und davon lasse ich nicht ab!

Ich habe ein reines Gewissen.

7Wer mich verklagt,

sich zu Unrecht gegen mich stellt,

der soll schuldig gesprochen werden.

Gott soll ihn mit vollem Recht verurteilen!

8Wer Gott verachtet, hat nichts mehr zu hoffen,

wenn seine Stunde schlägt,

wenn Gott von ihm sein Leben fordert.

9Wenn Angst und Schrecken ihn überfallen,

wird Gott sein Schreien nicht erhören.

10Denn an Gott hat er sich nie gefreut,

zu ihm zu beten, lag ihm fern.

11Ich will euch Gottes große Macht vor Augen führen

und euch nicht verschweigen, was der Allmächtige tun will.

12Ihr habt es doch alle selbst gesehen,

warum redet ihr dann solchen Unsinn?«

Der Gottlose bleibt nicht am Leben!

13»Was steht einem Menschen zu, der Gott verachtet?

Welchen Lohn zahlt der Allmächtige ihm für seine skrupellosen Taten?

14Er hat viele Söhne, doch sie fallen im Krieg;

seine Nachkommen müssen bitteren Hunger leiden.

15Wer dann noch lebt, stirbt an der Pest;

ihm selbst weinen seine Witwen keine Träne nach.

16Er hat Silber aufgehäuft, als wäre es bloßer Staub,

und kostbare Kleider gestapelt;

17doch aufrichtige Menschen werden sie tragen,

und wer schuldlos ist, wird seinen Silberschatz verteilen.

18Sein Haus hält nicht länger als ein Spinngewebe;27,18 So nach der griechischen Übersetzung. Der hebräische Text lautet: Er hat sein Haus gebaut wie die Motte.

es verfällt wie ein Unterschlupf,

den sich ein Wächter draußen für die Nacht aufstellt.

19Legt sich der Gottlose abends nieder,

fehlt nichts von seinem Reichtum;

am nächsten Morgen jedoch ist alles dahin!

20Wie eine Flut holt ihn das Unheil ein;

in der Nacht wirbelt ihn der Sturm davon.

21Der heiße Wüstenwind packt ihn und weht ihn fort!

22Hals über Kopf will er fliehen,

doch erbarmungslos überfällt ihn der Sturm;

23er heult und pfeift um ihn her,

als wollte er ihn verhöhnen.«