Yobu 28 – CCL & HOF

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yobu 28:1-28

1Pali mgodi wa siliva

ndiponso malo oyengerapo golide.

2Chitsulo amachikumba pansi,

ndipo mkuwa amawusungunula ku miyala yamkuwa.

3Munthu amalowa mu mdima atatenga nyale,

amafunafuna miyala mpaka ku malire a mgodiwo,

kufuna mkuwa mu mdima wandiweyani.

4Amakumba njira zapansi mu mgodimo, kutali ndi kumene kumakhala anthu,

kumalo kumene phazi la munthu silinapondeko;

iye amakhala ali lende pansipo namazungulira uku ndi uku.

5Nthaka, imene imatulutsa zakudya,

kunsi kwake kumachita ngati kwasandulizika ndi moto;

6miyala ya safiro imachokera mʼmatanthwe ake,

ndipo mʼfumbi lake mumakhala miyala yagolide.

7Palibe mbalame yodya zinzake imene imadziwa njira yobisikayi,

palibe kamtema amene anayiona.

8Zirombo zolusa sizipondamo mʼnjiramo,

ndipo mkango sudzeranso mʼmenemo.

9Munthu amaphwanya matanthwe olimba,

ndipo amagubuduza mapiri kuyambira mʼtsinde.

10Amabowola njira mʼmatanthwewo;

ndipo amaona chuma chonse cha mʼphirimo.

11Amaletsa mitsinje ya pansipo kuti isayendenso,

motero amatulutsira poyera zinthu zobisika.

12“Koma nzeru zingapezeke kuti?

Kodi kumvetsa zinthu kumakhala kuti?

13Munthu sadziwa kufunika kwake kwa nzeruzo;

nzeruyo sipezeka pa dziko lino la anthu amoyo.

14Phompho likuti, ‘Sizipezeka mwa ine muno.’

Nyanja ikuti, ‘Mwa ine munonso ayi.’

15Nzeru sungazigule ndi golide wabwino kwambiri,

mtengo wake sungawuyerekeze ndi siliva wambiri.

16Nzeru singagulidwe ndi golide wa ku Ofiri,

kapena ndi miyala ya onikisi kapena ya safiro.

17Nzeru sungayiyerekeze ndi golide kapena mwala wa galasi,

sungayigule ndi zokometsera zagolide.

18Miyala ya korali ndi krisitali siyoyeneranso ndi kuyitchula nʼkomwe;

mtengo wa nzeru ndi woposa miyala ya rubi.

19Nzeru sungayiyerekeze ndi miyala ya topazi ya ku Kusi;

nzeru singagulidwe ndi golide wabwino kwambiri.

20“Kodi tsono nzeru zimachokera kuti?

Kodi kumvetsa zinthu kumakhala kuti?

21Malo ake ndi obisika kwa zamoyo zonse,

ndi obisika ngakhale kwa mbalame zamlengalenga.

22Chiwonongeko ndi imfa zikuti,

‘Tangomva mphekesera chabe ya zimenezo!’

23Mulungu yekha ndiye amadziwa njira yake yopita kumeneko,

ndipo Iye yekha amadziwa kumene nzeru imakhala,

24pakuti Iye amayangʼana mpaka ku malekezero a dziko lapansi

ndipo amaona zonse za kunsi kwa thambo.

25Iye atapatsa mphepo mphamvu zake,

nayeza kuzama kwa nyanja,

26atakhazikitsa lamulo loti mvula izigwa

ndi kukonza njira ya chingʼaningʼani cha bingu,

27pamenepo ndi pamene anayangʼana nzeruzo naziyeza mtengo wake;

nazikhazikitsa ndi kuzisanthula bwino lomwe.

28Ndipo Iye anati kwa munthu,

‘Taonani, kuopa Ambuye, ndiye nzeru zimenezo

ndipo kuthawa zoyipa ndiye kumvetsa zinthu kumeneko.’ ”

Hoffnung für Alle

Hiob 28:1-28

Sag mir, wo die Weisheit ist!

1»Es gibt Minen, wo man nach Silber gräbt,

wir kennen die Stellen, wo das Gold gewaschen wird.

2Eisenerz holt man aus der Erde,

und Kupfer wird aus Gestein geschmolzen.

3Der Mensch erforscht auch die tiefste Dunkelheit;

er untersucht das Gestein und dringt dabei immer weiter vor

bis ins Innerste der Erde.

4Fern von jeder menschlichen Siedlung gräbt er einen Schacht,

an Orten, wo kein Mensch den Fuß hinsetzt;

die Bergleute lassen sich an Stricken hinunter

und schweben ohne jeden Halt.

5Oben auf der Erde wächst das Getreide,

doch tief unten wird sie umgewühlt,

als wütete ein Feuer.

6Ihr Gestein birgt den Saphir,

auch Goldstaub ist darin.

7Den Weg zu den Fundorten hat kein Geier erspäht,

nicht einmal das scharfe Auge eines Falken.

8Kein wildes Tier hat diesen Pfad betreten,

kein Löwe ist auf ihm geschritten.

9Doch der Mensch –

er arbeitet sich durch das härteste Gestein,

ganze Berge wühlt er um.

10Tief in den Felsen treibt er Stollen,

bis er dort findet, was sein Herz begehrt.

11Die Wasseradern im Gestein dichtet er ab;

tief Verborgenes bringt er ans Licht.

12Aber die Weisheit – wo ist sie zu finden?

Und wo entdeckt man die Einsicht?

13Kein Mensch kennt den Weg zu ihr,28,13 So nach der griechischen Übersetzung. Der hebräische Text lautet: Kein Mensch kennt ihren Wert.

unter den Lebenden findet man sie nicht.

14Das Meer und seine Tiefen sprechen:

›Die Weisheit ist nicht bei uns!‹

15Sie ist unbezahlbar, mit Gold und Silber nicht aufzuwiegen.

16Man kann sie weder mit Feingold kaufen

noch mit kostbarem Onyx oder Saphir.

17Gold und reines Glas reichen nicht an sie heran,

und auch gegen Goldschmuck kann man sie nicht tauschen,

18ganz zu schweigen von Korallen und Kristall!

Ja, der Wert der Weisheit übertrifft alle Rubine.

19Der Topas aus Äthiopien ist nichts

im Vergleich zu ihr,

mit reinem Gold ist sie nicht aufzuwiegen.

20Woher also kommt die Weisheit?

Und wo entdeckt man die Einsicht?

21Ja, sie ist dem menschlichen Auge verborgen,

und auch die Raubvögel erspähen sie nicht.

22Das tiefe Totenreich und selbst der Tod,

sie sprechen: ›Wir haben von ihr nur ein Gerücht gehört!‹

23Gott allein kennt den Weg zur Weisheit;

er nur weiß, wo sie zu finden ist.

24Denn er blickt über die ganze Welt,

er durchschaut Himmel und Erde.

25Schon damals, als er dem Wind seine Wucht gab

und den Wassermassen eine Grenze setzte;

26als er bestimmte, wo der Regen niedergehen sollte,

als er den Gewitterwolken einen Weg vorschrieb –

27schon da sah er die Weisheit an

und rühmte ihren Wert,

er erforschte sie und gab ihr Bestand.

28Und zum Menschen sprach er:

›Weise ist, wer Ehrfurcht vor mir hat,

und Einsicht besitzt, wer sich vom Bösen abkehrt.‹«