Yobu 23 – CCL & LCB

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yobu 23:1-17

Yobu

1Pamenepo Yobu anayankha kuti,

2“Leronso kudandaula kwanga nʼkwakukulu kwambiri;

Iye akundilanga kwambiri ngakhale ndi kubuwula.

3Ndikanangodziwa kumene ndikanamupeza Mulungu;

ndikanangopita kumene amakhalako!

4Ndikanafotokoza mlandu wanga pamaso pake

ndipo ndikanayankhula mawu odziteteza.

5Ndikanadziwa mawu amene Iye akanandiyankha,

ndi kulingalira bwino zimene akananena!

6Kodi Iye akanalimbana nane mwa mphamvu zake zazikulu?

Ayi, Iye sakanayankhula zinthu zotsutsana nane.

7Kumeneko munthu wolungama akanafotokoza mlandu wake pamaso pake,

ndipo woweruzayo akanandipeza wosalakwa nthawi zonse.

8“Taonani, ndikapita kummawa, Iye kulibe kumeneko,

ndikapita kumadzulo sinditha kumupeza kumeneko.

9Akamagwira ntchito kumpoto, sindimuona kumeneko

akapita kummwera, sindimuona.

10Koma Iye amadziwa mmene ndimayendera;

Iyeyo akandiyesa adzandipeza kuti ndili ngati golide.

11Mapazi anga akhala akuponda mʼmapazi ake;

ndasunga njira yake ndipo sindinayitaye.

12Sindinapatuke kusiya malamulo ochokera pakamwa pake;

ndasunga mawu a pakamwa pake kupambana chakudya changa cha tsiku ndi tsiku.

13“Koma Iyeyo ndi wosasinthika, ndipo ndani angatsutsane naye?

Iye amachita chilichonse chimene wafuna.

14Iye amachita chimene watsimikiza kuti chindichitikire,

ndipo malingaliro oterowa ali nawobe.

15Nʼchifukwa chake ndikuchita mantha kwambiri pamaso pake;

ndikamaganiza zonsezi ndimamuopa.

16Mulungu walefula mtima wanga;

Wamphamvuzonse wandiopseza kwambiri.

17Komatu sindinachititsidwe mantha ndi mdima,

ndi mdima wandiweyani umene waphimba nkhope yanga.

Luganda Contemporary Bible

Yobu 23:1-17

Yobu Ayanukula

1Awo Yobu n’addamu nti,

223:2 a Yob 7:11 b Yob 6:3“N’okutuusa leero okwemulugunya kwange kubalagala,

omukono gwe gunzitoowerera wadde mbadde mu kusinda.

3Singa nnali mmanyi aw’okumusanga

nandisobodde okulaga gy’abeera!

423:4 Yob 13:18Nanditutte empoza yange gy’ali,

akamwa kange nga nkajjuzizza ensonga zange.

5Nanditegedde kye yandinzizeemu,

ne neetegereza kye yandiŋŋambye.

623:6 Yob 9:4Yandimpakanyizza n’amaanyi mangi?

Nedda, teyandinteeseko musango.

723:7 Yob 13:3Eyo omuntu omutuukirivu asobola okutwalayo ensonga ye,

era nandisumuluddwa omulamuzi wange emirembe n’emirembe.

8“Bwe ŋŋenda ebuvanjuba, nga taliiyo;

ne bwe ŋŋenda ebugwanjuba, simusangayo.

923:9 Yob 9:11Bw’aba akola mu bukiikakkono simulaba,

bw’adda mu bukiikaddyo, simulabako.

1023:10 a Zab 66:10; 139:1-3 b 1Pe 1:7Naye amanyi amakubo mwe mpita,

bw’anaamala okungezesa, nzija kuvaamu nga zaabu.

1123:11 a Zab 17:5 b Zab 44:18Ebigere byange bimugoberedde;

ntambulidde mu makubo ge nga sikyamakyama.

1223:12 a Yob 6:10 b Yk 4:32, 34Saava ku biragiro by’akamwa ke.

Nayagala ebigambo by’akamwa ke okusinga emmere yange gyendya bulijjo.

1323:13 Zab 115:3“Naye yeemalirira, ani ayinza okumuwakanya?

Akola kyonna ekimusanyusa.

1423:14 1Bs 3:3Weewaawo ajja kutuukiriza by’asazzeewo okunjolekeza,

era bingi byategese by’akyaleeta.

15Kyenva mba n’entiisa nga ndi mu maaso ge;

bwe ndowooza ku bino byonna, ne mmutya.

1623:16 a Ma 20:3; Zab 22:14; Yer 51:46 b Yob 27:2Katonda anafuyizza nnyo omutima gwange,

Ayinzabyonna antiisizza nnyo.

1723:17 Yob 19:8Naye ekizikiza tekinsirisizza,

ekizikiza ekikutte ennyo ekibisse amaaso gange.”