Yobu 22 – CCL & LCB

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yobu 22:1-30

Mawu a Elifazi

1Pamenepo Elifazi wa ku Temani anayankha kuti,

2“Kodi munthu nʼkukhala waphindu kwa Mulungu?

Kodi munthu wanzeru angamupindulire Iye?

3Kodi Wamphamvuzonse akanapeza chabwino chotani iweyo ukanakhala wolungama?

Kodi iyeyo akanapeza phindu lanji makhalidwe ako akanakhala angwiro?

4“Kodi nʼchifukwa choti umamuopa, kuti azikudzudzula,

kuti azifuna kukukokera ku mlandu?

5Kodi osati nʼchifukwa chakuti kuyipa kwako nʼkwakukulu?

Kodi machimo ako si opanda malire?

6Iwe unkawumiriza abale ako kuti akupatse chikole popanda chifukwa;

umalanda anthu zovala zawo ndi kuwasiya amaliseche.

7Sunawapatse madzi anthu otopa,

ndipo unawamana chakudya anthu anjala,

8ngakhale unali munthu wamphamvu, wokhala ndi malo akeake,

munthu waulemu wake, wokhala mʼdzikomo.

9Ndipo akazi amasiye unawachotsa wopanda kanthu,

ndipo unapondereza ana amasiye.

10Nʼchifukwa chake misampha yakuzungulira,

nʼchifukwa chake tsoka ladzidzidzi lakuchititsa mantha,

11nʼchifukwa chake kuli mdima kuti sungathe kuona kanthu,

nʼchifukwa chakenso madzi achigumula akumiza.

12“Kodi Mulungu sali kutalitali kumwamba?

Ndipo ona nyenyezi zili mmwamba kwambirizo, ona kutalika kwake pamene zililipo!

13Komabe iweyo ukunena kuti, ‘Kodi Mulungu amadziwa chiyani?

Kodi Iye amaweruza mu mdima woterewu?

14Mitambo yakuda yamuphimba, kotero kuti Iye sakutiona

pamene akuyendayenda pamwamba pa thambopo.’

15Kodi iwe udzayendabe mʼnjira yakale

imene anthu oyipa ankayendamo?

16Iwo anachotsedwa nthawi yawo isanakwane,

maziko awo anakokoloka ndi madzi achigumula.

17Anthuwo anati kwa Mulungu, ‘Tichokereni!

Kodi Wamphamvuzonse angatichitire chiyani?’

18Chonsecho ndi Iye amene anadzaza nyumba zawo ndi zinthu zabwino,

choncho ine sindigwirizana ndi uphungu wa anthu oyipa.

19“Anthu olungama amaona kuwonongeka kwawo ndipo amakondwera;

anthu osalakwa amangoseka, akamuona woyipa akulangidwa.

20Amanena kuti, ‘Ndithudi adani athu awonongeka

ndipo moto wawononga chuma chawo!’

21“Gonjera Mulungu kuti ukhale naye pamtendere;

ukatero udzaona zabwino.

22Landira malangizo a pakamwa pake

ndipo usunge mawu ake mu mtima mwako.

23Ukabwerera kwa Wamphamvuzonse udzabwezeretsedwa;

ukachotsa zoyipa zonse zimene zimachitika mʼnyumba mwako,

24ndipo chuma chamtengowapatali nuchiona ngati fumbi,

golide wa ku Ofiri numutaya ku miyala ya ku zigwa.

25Pamenepo Wamphamvuzonseyo adzakhala golide wako,

siliva wako wamtengowapatali.

26Pamenepo udzakondwera naye Wamphamvuzonse

ndipo udzakweza nkhope yako kwa Mulungu.

27Udzamupempha ndipo adzakumvera,

ndipo udzapereka zimene unalonjeza.

28Chimene watsimikiza kuti uchite, chidzachitikadi,

kuwala kudzakuwunikira pa njira yako.

29Pamene anthu agwetsedwa pansi, iwe nʼkunena kuti, ‘Akwezeni!’

Pamenepo Iye adzapulumutsa anthu oponderezedwa.

30Iye adzapulumutsa ngakhale munthu amene ndi wolakwa,

ameneyo adzapulumutsidwa kudzera mʼkulungama kwako.”

Luganda Contemporary Bible

Yobu 22:1-30

Erifaazi Addamu

1Awo Erifaazi Omutemani n’addamu n’ayogera nti,

222:2 Luk 17:10“Omuntu ayinza okugasa Katonda?

Wadde oyo ow’amagezi ayinza okumuyamba?

3Ayinzabyonna yandifunye kwesiima ki singa wali mutuukirivu?

Yandiganyuddwa ki singa amakubo go gaali magolokofu?

422:4 Yob 14:3; 19:29; Zab 143:2“Akukangavvula lwa kumutya

era kyava akuvunaana?

522:5 Yob 11:6; 15:5Okwonoona kwo si kunene nnyo?

Ebibi byo si bingi nnyo?

622:6 Kuv 22:26; Ma 24:6, 17; Ez 18:12, 16Kubanga waggya ku muganda wo emisingo awatali nsonga;

waggya engoye ku bantu, n’obaleka bwereere.

722:7 Yob 31:17, 21, 31Tewawa bakoowu mazzi,

abaagala wabamma emmere,

822:8 Is 3:3; 9:15wadde nga wali musajja wa maanyi, eyalina ettaka,

omusajja ow’ekitiibwa, era nga byonna ggwe nnyini byo.

922:9 Yob 24:3, 21Weegobako bannamwandu bagende nga toliiko ky’obawadde;

abatalina bakitaabwe n’obamalamu amaanyi.

10Emitego kyegivudde gikwetooloola.

Lwaki entiisa ey’amangu ekujjira?

1122:11 a Yob 5:14 b Zab 69:1-2; 124:4-5; Kgb 3:54Lwaki enzikiza ekutte nnyo tosobola kulaba,

era lwaki amataba gakubikkako?

1222:12 Yob 11:8“Katonda tali waggulu mu ggulu?

Era laba, emmunyeenye ezisingayo okuba waggulu, nga bwe ziri ewala!

1322:13 a Zab 10:11; Is 29:15 b Ez 8:12Ate n’ogamba nti, ‘Katonda amanyi ki?

Ayinza okulamulira mu kizikiza?

1422:14 Yob 26:9Ebire ebikutte bimubikkako, n’aba ng’atatulaba

bw’aba atambula mu bifo by’omu ggulu.’

15Onoosigala mu kkubo ery’edda

abasajja abakozi b’ebibi lye baakwata?

1622:16 a Yob 15:32 b Yob 14:19; Mat 7:26-27Baatwalibwa ng’ekiseera kyabwe tekinnatuuka,

emisingi gyabwe gyatwalibwa amataba.

1722:17 Yob 21:15Be bagamba Katonda nti, ‘Tulekere emirembe!

Ayinzabyonna ayinza kutukola ki?’

1822:18 a Yob 12:6 b Yob 21:16Ate nga ye, ye yajjuza ennyumba zaabwe ebintu ebirungi,

noolwekyo neewuunya nnyo amagezi g’abakozi b’ebibi.

1922:19 a Zab 58:10; 107:42 b Zab 52:6Abatuukirivu balaba okuzikirira kwabwe ne bajaguza;

abataliiko musango babasekerera nga bagamba nti,

2022:20 Yob 15:30‘Ddala abalabe baffe bazikiridde,

era omuliro gulidde obugagga bwabwe.’ 

2122:21 Zab 34:8-10“Gonderanga Katonda ofunenga emirembe;

mu ngeri eno ebirungi lwe binajjanga gy’oli.

22Kkiriza ebiragiro ebiva mu kamwa ke

era oteeke ebigambo bye mu mutima gwo.

2322:23 a Yob 8:5; Is 31:6; Zek 1:3 b Is 19:22; Bik 20:32 c Yob 11:14Bw’onodda eri oyo Ayinzabyonna, onodda buggya,

bwonooteeka ebibi ewala ne weema yo,

2422:24 Yob 31:25n’oteeka n’amayinja go ag’omuwendo mu ttaka,

zaabu yo eya Ofiri ku njazi z’omu mugga,

2522:25 Is 33:6awo Ayinzabyonna anaabeeranga zaabu yo,

era ffeeza esingayo obulungi.

2622:26 Yob 27:10; Is 58:14Ddala ddala olisanyukira mu oyo Ayinzabyonna

era oyimuse amaaso go eri Katonda.

2722:27 Yob 33:26; 34:28; Is 58:9Olimusaba, alikuwulira,

era olituukiriza obweyamo bwo.

28Ky’olisalawo kirikolebwa,

era ekitangaala kirimulisa amakubo go.

2922:29 Mat 23:12; 1Pe 5:5Abantu abalala bwe balisuulibwa n’ogamba nti, ‘Bayimuse!’

Olwo alirokola abagudde.

3022:30 Yob 42:7-8Alinunula n’oyo aliko omusango,

alinunulwa olw’obulongoofu bw’emikono gyo.”