Yobu 15 – CCL & LCB

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yobu 15:1-35

Mawu a Elifazi

1Pamenepo Elifazi wa ku Temani anayankha kuti,

2“Kodi munthu wanzeru angayankhe ndi mawu achabechabe otere,

kapena angakhutitse mimba yake ndi mphepo yotentha yochokera kummawa?

3Kodi angathe kutsutsa ndi mawu opanda pake,

kapena kuyankhula mawu opanda phindu?

4Koma iwe ukuchepetsa zoopa Mulungu

ndipo ukutchinga zodzikhuthulira kwa Mulungu.

5Tchimo lako ndiye likuyankhulitsa pakamwa pakopo;

ndipo watengera mayankhulidwe a atambwali.

6Pakamwa pakopo ndiye pakukutsutsa osati pakamwa panga;

milomo yakoyo ikukutsutsa.

7“Kodi ndiwe munthu woyamba kubadwa?

Kodi unalengedwa mapiri asanalengedwe?

8Kodi unali mʼgulu la alangizi a Mulungu?

Kodi ukudziyesa wanzeru ndiwe wekha?

9Kodi iwe umadziwa chiyani chimene ife sitichidziwa?

Kodi iwe uli ndi chidziwitso chanji chimene ife tilibe?

10Anthu a imvi ndi okalamba ali mbali yathu,

anthu amvulazakale kupambana abambo ako.

11Kodi mawu otonthoza mtima ochokera kwa Mulungu sakukukwanira,

mawu oyankhula mofatsawa kwa iwe?

12Chifukwa chiyani ukupsa mtima,

ndipo chifukwa chiyani ukutuzula maso ako,

13moti ukupsera mtima Mulungu

ndi kuyankhula mawu otero pakamwa pako?

14“Kodi munthu nʼchiyani kuti nʼkukhala woyera mtima

kapena wobadwa mwa amayi nʼchiyani kuti nʼkukhala wolungama mtima?

15Ngati Mulungu sakhulupirira ngakhale angelo ake,

ngakhale zakumwamba sizoyera pamaso pake,

16nanga kuli bwanji munthu amene ndi wonyansa ndi wa njira zokhotakhota,

amene kuchita zoyipa kuli ngati kumwa madzi.

17“Mvetsera kwa ine ndipo ndidzakufotokozera;

ndilole ndikuwuze zimene ndaziona,

18zimene anandiphunzitsa anthu anzeru,

sanandibisire kalikonse kamene anamva kuchokera kwa makolo awo.

19(Ndi kwa iwowa kumene dziko lino linaperekedwa

pamene panalibe mlendo wokhala pakati pawo).

20Munthu woyipa amavutika ndi masautso masiku onse a moyo wake,

munthu wankhanza adzavutika zaka zake zonse.

21Amamva mawu owopsa mʼmakutu mwake,

pamene zonse zikuoneka ngati zili bwino, anthu achifwamba amamuthira nkhondo.

22Iye sakhulupirira kuti angathe kupulumuka ku mdima wa imfa;

iyeyo ndi woyenera kuphedwa.

23Amangoyendayenda pali ponse kunka nafuna chakudya;

amadziwa kuti tsiku la mdima lili pafupi.

24Masautso ndi nthumanzi zimamuchititsa mantha kwambiri;

zimamugonjetsa iye monga imachitira mfumu yokonzekera kukathira nkhondo,

25chifukwa iye amatambasula dzanja lake kuyambana ndi Mulungu

ndipo amadzitama yekha polimbana ndi Wamphamvuzonse.

26Amapita mwa mwano kukalimbana naye

atanyamula chishango chochindikala ndi cholimba.

27“Ngakhale nkhope yake ndi yonenepa

ndipo mʼchiwuno mwake muli mnofu wambiri,

28munthuyo adzakhala mʼmizinda yowonongeka

ndi mʼnyumba zosayenera kukhalamo anthu,

nyumba zimene zikugwa ndi kuwonongeka.

29Iye sadzalemeranso ndipo chuma chake sichidzakhalitsa,

ngakhale minda yake sidzabala zipatso pa dziko lapansi.

30Iyeyo sadzapulumuka mu mdimamo;

lawi lamoto lidzawumitsa nthambi zake,

ndipo mpweya wochokera mʼkamwa mwa Mulungu udzamusesa.

31Asadzinyenge yekha podalira zinthu zachabechabe,

pakuti pa mapeto pake sadzaphulapo kanthu.

32Iye adzalandira malipiro ake nthawi yake isanakwane,

ndipo nthambi zake sizidzaphukanso.

33Iye adzakhala ngati mtengo wamphesa wopululidwa zipatso zake zisanapse,

adzakhala ngati mtengo wa olivi umene wayoyola maluwa ake.

34Pakuti anthu osapembedza Mulungu adzakhala osabala

ndipo moto udzapsereza nyumba za onse okonda ziphuphu.

35Iwo amalingalira zaupandu ndipo amachita zoyipa;

mtima wawo umakonzekera zachinyengo.”

Luganda Contemporary Bible

Yobu 15:1-35

Erifaazi Ayogera

1Awo Erifaazi Omutemani n’addamu n’ayogera nti,

215:2 Yob 6:26“Omuntu ow’amagezi yandizzeemu n’amagezi agataliimu,

oba n’ajjuza olubuto lwe embuyaga ez’ebuvanjuba?

3Yandiwakanye n’ebigambo ebitaliiko kye bigasa,

oba okwogera ebigambo ebitalina kye bikola?

4Naye onyooma Katonda

n’oziyiza okwewaayo eri Katonda.

515:5 Yob 5:13Kubanga obutali butuukirivu bwo bwe buyigiriza akamwa ko,

era olonzeewo okukozesa olulimi lw’abalimba.

615:6 Luk 19:22Akamwa ko kennyini ke kakusalira omusango si nze,

emimwa gyo gyennyini gye gikulumiriza.

715:7 a Yob 38:21 b Zab 90:2; Nge 8:25“Gwe wasooka abantu bonna okuzaalibwa?

Oba ggwe wazaalibwa ensozi nga tezinnabaawo?

815:8 Bar 11:34; 1Ko 2:11Ofaayo okuwuliriza okuteesa kwa Katonda?

Olowooza gwe mugezi wekka?

915:9 Yob 13:2Kiki ky’omanyi kye tutamanyi?

Kubikkulirwa ki kw’olina ffe kwe tutalina?

1015:10 Yob 32:6-7Ab’envi abakaddiye bali ku ludda lwaffe,

abasajja abakulu n’okusinga kitaawo.

1115:11 a 2Ko 1:3-4 b Zek 1:13 c Yob 36:16Katonda by’akugambye ebikuzzaamu amaanyi bitono nnyo tebikumala,

ebigambo ebikubuuliddwa mu bukkakkamu?

1215:12 Yob 11:13Lwaki omutima gwo gukubuzizza,

amaaso go ne gatemereza

13n’olyoka ofuka obusungu bwo eri Katonda,

n’ofukumula ebigambo bwe bityo okuva mu kamwa ko?

1415:14 a Yob 14:4; 25:4 b Nge 20:9; Mub 7:20“Omuntu ye ani, alyoke abeere omutukuvu,

oba oyo azaalibwa omukazi nti ayinza okuba omutuukirivu?

1515:15 Yob 4:18; 25:5Katonda bw’aba tassa bwesige mu batukuvu be,

n’eggulu ne liba nga si ttukuvu mu maaso ge,

1615:16 a Zab 14:1 b Yob 34:7; Nge 19:28oba oleeta otya omuntu obuntu, omugwagwa era omuvundu,

anywa obutali butuukirivu nga amazzi!

17“Mpuliriza nnaakunnyonnyola,

leka nkubuulire kye ndabye:

1815:18 Yob 8:8abasajja ab’amagezi kye bagambye

nga tebalina kye bakwese ku kye baafuna okuva eri bakadde baabwe

19abo bokka abaweebwa ensi

nga tewali mugwira agiyitamu.

2015:20 Yob 24:1; 27:13-23Omuntu omukozi w’ebibi, aba mu kubonaabona ennaku ze zonna,

n’anyigirizibwa emyaka gyonna egyamutegekerwa.

2115:21 a Yob 18:11; 20:25 b Yob 27:20; 1Bs 5:3Amaloboozi agatiisa gajjuza amatu ge;

byonna bwe biba ng’ebiteredde, abanyazi ne bamulumba.

2215:22 Yob 19:29; 27:14Atya okuva mu kizikiza adde,

ekitala kiba kimulinze okumusala.

2315:23 a Zab 59:15; 109:10 b Yob 18:12Adda eno n’eri ng’anoonya ky’anaalya,

amanyi ng’olunaku olw’ekizikiza lumutuukiridde.

24Okweraliikirira n’obubalagaze bimubuutikira,

bimujjula nga kabaka eyetegekedde olutalo.

2515:25 Yob 36:9Kubanga anyeenyerezza Katonda ekikonde,

ne yeegereegeranya ku oyo Ayinzabyonna,

26n’agenda n’ekyejo amulumbe,

n’engabo ennene enzito.

2715:27 Zab 17:10“Wadde nga yenna yagejja amaaso

ng’ajjudde amasavu mu mbiriizi,

2815:28 a Is 5:9 b Yob 3:14wakubeera mu bibuga eby’amatongo,

ne mu bifulukwa,

ennyumba ezigwa okufuuka ebifunfugu.

2915:29 Yob 27:16-17Taddeyo kugaggawala,

n’obugagga bwe tebulirwawo,

n’ebintu by’alina tebirifuna mirandira mu ttaka.

3015:30 a Yob 5:14 b Yob 22:20 c Yob 4:9Taliwona kizikiza,

olulimi lw’omuliro lunaakazanga amatabi ge,

era omukka gw’omu kamwa gulimugobera wala.

3115:31 Is 59:4Alemenga okwerimba nga yeesiga ebitaliimu,

kubanga talina ky’ajja kuganyulwa.

3215:32 a Mub 7:17 b Yob 22:16; Zab 55:23 c Yob 18:16Wa kusasulwa byonna ng’obudde tebunnatuuka,

n’amatabi ge tegalikula.

3315:33 Kbk 3:17Aliba ng’omuzabbibu ogugiddwako emizabbibu egitannaba kwengera,

ng’omuzeyituuni ogukunkumula ebikoola byagwo.

3415:34 Yob 8:22Kubanga ekibiina ky’abatatya Katonda kinaabeeranga kigumba,

era omuliro gunaayokyanga weema ezinaabangamu enguzi.

3515:35 Zab 7:14; Is 59:4; Kos 10:13Baba embuto ez’ekibi ne bazaala obutali butuukirivu,

embuto zaabwe zizaala obulimba.”