Yobu 14 – CCL & LCB

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yobu 14:1-22

1“Munthu wobadwa mwa amayi

amakhala masiku owerengeka ndipo ndi odzaza ndi mavuto okhaokha.

2Amaphuka ngati duwa ndipo kenaka amafota;

amathawa ngati mthunzi ndipo sakhalitsa.

3Kodi munthu wotereyo nʼkumuyangʼanitsitsa?

Kodi mungamubweretse pamaso panu kuti mumuzenge mlandu?

4Ndani angatulutse chabwino mʼchoyipa?

Palibe ndi mmodzi yemwe!

5Masiku a munthu ndi odziwikiratu;

munakhazikitsa chiwerengero cha miyezi yake

ndipo munamulembera malire amene sangathe kuwalumpha.

6Choncho Inu mumufulatire ndipo mumuleke apumule

kufikira atakondwera nawo moyo ngati munthu waganyu.

7“Mtengo uli nacho chiyembekezo:

ngati wadulidwa, udzaphukiranso

ndipo nthambi zake sizidzaleka kuphukira.

8Mizu yake ingathe kukalamba mʼnthaka

ndipo chitsa chake nʼkuwola pa dothi,

9koma pamene chinyontho chafika udzaphukira

ndipo udzaphuka nthambi ngati mtengo wanthete.

10Koma munthu amafa nayikidwa mʼmanda,

amapuma mpweya wotsiriza ndipo kutha kwake nʼkomweko.

11Monga madzi amaphwera mʼnyanja

kapena monga mtsinje umaphwera nuwuma,

12momwemonso munthu amagona ndipo sadzukanso;

mpaka zamlengalenga zidzathe, anthu sadzauka

kapena kudzutsidwa ku tulo tawo.

13“Aa, Inu mukanangondibisa mʼmanda

ndi kundiphimba kuti ndisaoneke mpaka mkwiyo wanu utapita!

Achikhala munandiyikira nthawi,

kuti pambuyo pake mundikumbukirenso.

14Munthu akafa, kodi adzakhalanso ndi moyo?

Masiku anga onse a moyo wovutikawu

ndidzadikira mpaka itafika nthawi yomasulidwa.

15Inu mudzandiyitane ndipo ndidzakuyankhani;

inu mudzafunitsitsa kuona cholengedwa chimene munachipanga ndi manja anu.

16Ndithudi pamenepo mudzayangʼana mayendedwe anga

koma simudzalondola tchimo langa.

17Zolakwa zanga zidzakulungidwa mʼthumba;

inu mudzaphimba tchimo langa.

18“Koma monga phiri limakokolokera ndi kuswekasweka

ndipo monga thanthwe limasunthira kuchoka pa malo ake,

19monganso madzi oyenda amaperesera miyala

ndipo madzi othamanga amakokololera nthaka,

momwemonso Inu mumawononga chiyembekezo cha munthu.

20Inu mumamugonjetsa kamodzinʼkamodzi ndipo munthuyo nʼkutheratu;

Inu mumasintha maonekedwe a nkhope yake ndipo mumamutaya kutali.

21Ana ake akamalemekezedwa, iyeyo sazidziwa zimenezo;

akamachititsidwa manyazi iye saziona zimenezo.

22Iye amangomva zowawa za mʼthupi lake

ndipo amangodzilirira yekha mwini wakeyo.”

Luganda Contemporary Bible

Yobu 14:1-22

114:1 Yob 5:7; Mub 2:23“Omuntu azaalibwa omukazi,

abeera ku nsi akaseera katono era abeera mu kutegana.

214:2 a Yak 1:10 b Zab 90:5-6 c Yob 8:9Amulisa ng’ekimuli n’awotoka;

abulawo mangu ng’ekisiikirize, tabeerera.

314:3 a Zab 8:4; 144:3 b Zab 143:2Otunuulira omuntu afaanana bw’atyo?

Olimuleeta gy’oli asalirwe omusango?

414:4 a Zab 51:10 b Bef 2:1-3 c Yk 3:6; Bar 5:12Ani ayinza okuggya ekirongoofu mu kitali kirongoofu?

Tewali n’omu!

514:5 Yob 21:21Ennaku z’omuntu zaagererwa,

wagera obungi bw’emyezi gye

era n’oteekawo ekkomo ly’atasobola kusukka.

614:6 a Yob 7:19 b Yob 7:1, 2; Zab 39:13Kale tomufaako muleke yekka,

okutuusa lw’alimala okutuukiriza emirimu gye ng’omupakasi.

7“Wakiri waliwo essuubi ng’omuti guloka:

Bwe gutemebwa, guloka nate,

era ekikolo kyagwo ekiggya tekifa.

8Emirandira gyagwo gyandikaddiyidde mu ttaka

era n’ekikonge ne kifiira mu ttaka,

9naye olw’emirandira okutambula ne ginoonya amazzi kimulisa

ne kireeta amatabi ng’ekisimbe.

1014:10 Yob 13:19Naye omuntu afa era n’agalamizibwa,

assa ogw’enkomerero n’akoma.

1114:11 Is 19:5Ng’amazzi bwe gaggwa mu nnyanja

oba omugga bwe gukalira ne guggwaawo,

1214:12 a Kub 20:11; 21:1 b Bik 3:21bw’atyo omuntu bw’agalamira,

era n’atasituka okutuusa eggulu bwe linaggwaawo,

abantu tebajja kuzuukuka oba kuggyibwa mu tulo twabwe.

1314:13 Is 26:20“Singa kale onkweka emagombe

era n’onziika okutuusa obusungu bwo lwe buliggwaawo!

Singa ongerera ekiseera

n’onzijukira!

14Omuntu bw’afa, addamu n’abeera omulamu?

Ennaku zange zonna ez’okuweereza

nnaalindanga okuwona kwange kujje.

1514:15 Yob 13:22Olimpita nange ndikuyitaba;

olyegomba ekitonde emikono gyo kye gyatonda.

1614:16 a Zab 139:1-3; Nge 5:21; Yer 32:19 b Yob 10:6Ddala ku olwo bw’olibala ebigere byange,

naye tolyekaliriza bibi byange.

1714:17 a Ma 32:34 b Kos 13:12Ebisobyo byange biriba bisibiddwa mu kisawo;

olibikka ku kibi kyange.

18“Naye ng’olusozi bwe luseebengerera ne luggwaawo,

era ng’ejjinja bwe liva mu kifo kyalyo,

1914:19 Yob 7:6ng’amazzi bwe gaggwereeza amayinja

era ng’okwanjaala kwago bwe kutwala ettaka ly’oku nsi;

bw’atyo bw’azikiriza essuubi ly’omuntu.

20Omumalamu amaanyi omuwangula lumu n’aggweerawo ddala;

okyusa enfaanana ye n’omugoba.

2114:21 Mub 9:5; Is 63:16Abaana be bwe bafuna ekitiibwa, takimanya,

bwe bagwa, takiraba.

22Obulamu bw’omubiri gwe bwokka bw’awulira

ne yeekungubagira yekka.”