Yesaya 66 – CCL & NRT

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yesaya 66:1-24

Chiweruzo ndi Chiyembekezo

1Yehova akuti,

“Kumwamba ndi mpando wanga waufumu

ndipo dziko lapansi ndilo chopondapo mapazi anga.

Tsono nyumba ili kuti yomwe mundimangire,

ndipo malo ali kuti amene inu mungandikonzere kuti ndizipumuliramo?

2Kodi si manja anga amene anapanga zinthu zonsezi,

motero zonsezi ndi zanga?”

Akutero Yehova.

“Koma munthu amene ndimakondwera naye ndi uyu:

amene ali wodzichepetsa ndi wosweka mtima,

ndipo amamvera mawu anga.

3Koma aliyense amene amapereka nsembe ngʼombe yayimuna

amaphanso munthu,

ndipo aliyense amene amapereka mwana wankhosa,

amaphanso galu.

Aliyense amene amapereka nsembe chopereka cha chakudya

amaperekanso magazi a nkhumba.

Ndipo amene amafukiza lubani pa guwa lansembe la chikumbutso

amapembedzanso fano.

Popeza iwo asankha njira zawozawo,

ndiponso kusangalatsidwa ndi zonyansa zawo.

4Inenso ndawasankhira chilango chowawa

ndipo ndidzabweretsa pa iwo zimene amaziopa zija.

Pakuti pamene ndinawayitana palibe amene anayankha,

pamene ndinayankhula palibe amene anatchera khutu.

Anachita zoyipa pamaso panga

ndi kusankha kuchita zimene zimandinyansa zija.”

5Imvani mawu a Yehova,

inu amene mumanjenjemera ndi mawu ake:

“Abale anu amene amakudani,

ndi kukuchotsani pakati pawo chifukwa cha dzina langa, amanena kuti,

‘Yehova alemekezeke

kuti ife tione chimwemwe chanu!’

Koma ndi iwowo amene adzachite manyazi.

6Imvani mfuwu mu mzinda,

imvani phokoso mʼNyumba ya Mulungu!

Limenelo ndi liwu la Yehova,

kulanga adani ake onse.

7“Mzinda uli ngati amayi apakati amene asanayambe kumva zowawa

wachira kale;

asanayambe kumva ululu,

wabala kale mwana wamwamuna.

8Ndani anamvapo zinthu zoterezi?

Ndani anazionapo zinthu zoterezi?

Kodi dziko nʼkupangika tsiku limodzi,

kapena mtundu wa anthu nʼkubadwa tsiku limodzi?

Komatu Ziyoni atangoyamba kumva zowawa

nthawi yomweyo anabereka ana ake.

9Kodi Ine ndingangofikitsa amayi apakati mpaka nthawi yake yochira,

koma osalola kuti abaledi mwana?” akutero Yehova.

“Kodi ndingatseke mimba

pa nthawi yoti abeleke?” akutero Mulungu wako.

10“Kondwera nayeni Yerusalemu ndipo musangalale chifukwa cha Iye,

inu nonse amene mumakonda Yerusalemu,

kondwera nayeni kwambiri,

nonse amene mumamulira.

11Pakuti mudzagawana naye ulemerero wake

ngati kuyamwa ndi kukhuta mkaka wambiri

wa mʼmawere

a chitonthozo chake.”

12Yehova akuti,

“Ndidzamupatsa mtendere ngati mtsinje wa madzi,

ndiponso chuma cha anthu a mitundu ina ngati mtsinje wosefukira.

Mudzakhala ngati mwana woyamwa amene amayi ake amunyamulira pambalipa,

kapena kumufungata pa miyendo yake.

13Monga momwe amayi amasangalatsira mwana wawo,

moteronso Ine ndidzakusangalatsani;

ndipo mudzasangalala chifukwa cha Yerusalemu.”

14Mukadzaona zimenezi mitima yanu idzakondwera. Mudzabiriwira ngati udzu.

Zimenezi zidzakulimbikitsani ndi kukupatsani moyo wamphamvu.

Mudzadziwa kuti ndimathandiza amene amanditumikira

ndi kuti ndimakwiyira adani anga.

15Taonani, Yehova akubwera ngati moto,

ndipo magaleta ake ali ngati kamvuluvulu;

Iye adzaonetsa mkwiyo wake nadzalanga adani ake

ndi malawi amoto.

16Pakuti Yehova adzalanga anthu onse

ndi moto ndi lupanga,

Yehova adzapha anthu ambiri.

17Yehova akuti, “Amene amadzipatula ndi kudziyeretsa okha kuti apite ku minda, ali ndi mtsogoleri awo, nʼkumadya nyama ya nkhumba, mbewa ndi zinthu zina zonyansa, onsewa adzafera limodzi.”

18“Ndipo Ine, chifukwa cha zochita zawo ndi maganizo awo, ndili pafupi kubwera kudzasonkhanitsa mitundu yonse ya anthu ndi ziyankhulo zonse. Iwo adzabwera ndi kuona ulemerero wanga.

19“Ndidzayika chizindikiro pakati pawo, ndipo ndidzatumiza ena mwa iwowa amene anapulumuka kuti apite kwa anthu a mitundu ina inu ku Tarisisi, ku Libiya ndi ku Ludi (akatswiri a mauta) ku Tubala ndi Grisi, ndi ku mayiko akutali a mbali mwa nyanja amene sanamvepo za mbiri yanga kapena kuona ulemerero wanga. Iwo adzalalika za ulemerero wanga pakati pa anthu a mitundu ina. 20Ndipo adzabwera nawo abale anu onse ngati mphatso yopereka kwa Yehova kuchokera kwa anthu a mitundu yonse. Iwo adzakwera nawo kupita ku Yerusalemu, phiri langa loyera ku Yerusalemu monga nsembe kwa Yehova, atakwera akavalo, magaleta ndi ngolo, ndi pa abulu ndi ngamira,” akutero Yehova. “Adzabwera nawo ngati momwe Aisraeli amabwerera ndi zopereka zachakudya ku Nyumba ya Yehova mu ziwiya zoyeretsedwa monga mwa mwambo. 21Ndipo ndidzasankha ena mwa iwonso kukhala ansembe ndi Alevi,” akutero Yehova.

22“Monga momwe mlengalenga mwatsopano ndi dziko lapansi latsopano zimene ndidzapanga zidzakhala mpaka muyaya pamaso panga, ndi chonchonso dzina lanu ndi zidzukulu zanu zidzakhalire.” Akutero Yehova. 23“Anthu a mitundu yonse adzabwera kudzandipembedza ku Yerusalemu, pa chikondwerero chilichonse cha pokhala pa mwezi watsopano ndi tsiku la Sabata lililonse,” akutero Yehova. 24“Akamachoka adzaona mitembo ya anthu amene anandiwukira Ine. Mphutsi zawo sizidzafa, kapena moto wawo sudzazimitsidwa. Anthu a mitundu ina yonse powaona adzanyansidwa nawo.”

New Russian Translation

Исаия 66:1-24

Суд, утешение и надежда

1Так говорит Господь:

– Небеса – престол Мой,

и земля – подножие ног Моих!

Какой вы можете построить Мне дом?

Где может быть место отдыха для Меня?

2Все это сотворено Моей рукой,

и так все это появилось66:2 Или: «и все это – Мое»., –

возвещает Господь. –

Вот кем Я дорожу:

тем, кто кроток и сокрушен духом

и трепещет перед словом Моим.

3Режущий в жертву быка –

как убивающий человека;

приносящий в жертву ягненка –

как ломающий шею псу;

представляющий хлебное приношение –

как приносящий свиную кровь66:3 Смысл этого места в еврейском тексте неясен.,

и приносящий в памятную жертву ладан –

как тот, кто молится идолу66:3 Или: «Приносящий в жертву быка также убивает человека; приносящий в жертву ягненка также ломает шею псу; представляющий хлебное приношение также приносит свиную кровь, и приносящий в памятную жертву благовония также молится идолу»..

Они сами избрали свои пути,

и мерзости их им приятны.

4Что ж, и Я изберу суровое наказание для них

и наведу на них то, чего они боятся.

Когда Я звал, никто не ответил,

когда Я говорил, никто не слушал.

Они делали злое в Моих глазах

и избрали неугодное Мне.

5Слушайте слово Господне,

трепещущие перед Его словом:

– Ваши братья, которые вас ненавидят

и изгоняют за имя Мое, сказали:

«Пусть Господь явит Себя в славе,

а мы посмотрим на вашу радость!»

Но они будут опозорены.

6Вот, шум из города,

шум из храма – шум от того,

что Господь воздает врагам Своим по заслугам!

7Еще не мучилась родами,

а уже родила;

еще не страдала от болей,

но уже разрешилась сыном.

8Кто слышал о таком?

Кто видел подобное?

Рождается ли страна в один день

или народ – за одно мгновение?

Но дочь Сиона, едва начала мучиться родами,

как родила своих сыновей.

9– Доведу ли Я до родов

и не дам родить? – говорит Господь. –

Разве закрою Я утробу,

дав силу родить? – говорит Бог твой. –

10Ликуйте с дочерью Иерусалима и веселитесь о ней,

все, кто любит ее;

радуйтесь, радуйтесь с ней,

все, кто над ней плачет!

11Потому что вы будете питаться и насыщаться

из ее груди, дающей утешение,

будете упиваться и наслаждаться

полнотой ее славы.

12Ведь так говорит Господь:

– Я направляю к нему мир, как реку,

и богатства народов, как полноводный поток.

Вас будут кормить,

будут носить на руках

и качать на коленях.

13Как мать утешает свое дитя,

так утешу вас Я;

вы будете утешены в Иерусалиме.

14Когда вы увидите это, сердце ваше возрадуется,

и ваши тела66:14 Букв.: «ваши кости». будут цвести, как трава;

Господня рука откроется Его слугам,

но ярость Его будет против Его врагов.

15Вот, Господь придет в огне,

колесницы Его подобны урагану;

в ярости Он обрушит Свой гнев,

и в пылающем пламени – Свой укор.

16Огнем и Своим мечом Господь исполнит

приговор над всеми людьми,

и много будет сраженных Господом.

17– Те, кто освящается и очищается, чтобы идти, следуя за ведущим, в сады для поклонения идолам, кто ест свинину, мышей и другие мерзости66:17 См. Лев. 11., погибнут вместе, – возвещает Господь.

18Я знаю их дела и мысли, и иду66:18 Так в ряде древних переводов; букв.: «идущая». собрать все народы и людей всех языков; они придут, увидят Мою славу, 19и Я сотворю среди них знамение. Я пошлю некоторых из уцелевших к народам – в Таршиш, Пул66:19 Так в нормативном еврейском тексте. В одном из древних переводов: «Пут». и Луд (знаменитый стрелками из лука), в Тувал и Грецию66:19 Евр.: «Иаван»., к дальним островам, которые не слышали обо Мне и не видели Моей славы. Они возвестят Мою славу среди народов. 20Они доставят всех ваших братьев из всех народов к Моей святой горе, в Иерусалим, как приношение Господу – на конях, в колесницах и повозках, на мулах и на верблюдах, – говорит Господь. – Они доставят их, как израильтяне доставляют свои хлебные приношения в храм Господа, в сосудах посвященных. 21И еще Я отберу некоторых из них, чтобы они были священниками и левитами, – говорит Господь.

22Потому что, как новое небо и новая земля, которые Я создам, устоят и останутся предо Мной, – возвещает Господь, – так останется ваше потомство и ваше имя. 23И от Новолуния к Новолунию, от субботы к субботе все люди будут приходить и поклоняться Мне, – говорит Господь. – 24Тогда они выйдут и посмотрят на трупы тех, кто отступил от Меня; их червь не умрет, и огонь их не угаснет66:24 Червь … огонь – в Новом Завете этот образ ада – места, где предаются огню нераскаявшиеся грешники, – стал ключевой метафорой вечных мук и наказаний (см. 48:22; 57:20; Мк. 9:47-48)., и они будут внушать отвращение всем людям.