Yesaya 64 – CCL & CCBT

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yesaya 64:1-12

1Inu Yehova, bwanji mukanangongʼamba mlengalenga ndi kutsika pansi,

kuti mapiri agwedezeke pamaso panu!

2Monga momwe moto umatenthera tchire

ndiponso kuwiritsa madzi,

tsikani kuti adani anu adziwe dzina lanu,

ndiponso kuti mitundu ya anthu injenjemere pamaso panu.

3Pakuti nthawi ina pamene munatsika munachita zinthu zoopsa zimene sitinaziyembekezere,

ndipo mapiri anagwedezeka pamaso panu.

4Chikhalire palibe ndi mmodzi yemwe anamvapo

kapena kuona

Mulungu wina wonga Inu,

amene amachitira zinthu zotere amene amadikira pa Iye.

5Inu mumabwera kudzathandiza onse amene amakondwera pochita zolungama,

amene amakumbukira njira zanu.

Koma Inu munakwiya,

ife tinapitiriza kuchimwa.

Kodi nanga tingapulumutsidwe bwanji?

6Tonsefe takhala ngati anthu amene ndi odetsedwa,

ndipo ntchito zathu zili ngati sanza za msambo;

tonse tafota ngati tsamba,

ndipo machimo athu akutiwuluzira kutali ngati mphepo.

7Palibe amene amapemphera kwa Inu

kutekeseka kuti apemphe chithandizo kwa Inu;

pakuti mwatifulatira

ndi kutisiya chifukwa cha machimo athu.

8Komabe, Inu Yehova ndinu Atate athu.

Ife ndife chowumba, Inu ndinu wowumba;

ife tonse ndi ntchito ya manja anu.

9Inu Yehova, musatikwiyire kopitirira muyeso

musakumbukire machimo athu mpaka muyaya.

Chonde, mutiganizire, ife tikupempha,

pakuti tonsefe ndi anthu anu.

10Mizinda yanu yopatulika yasanduka chipululu;

ngakhaletu Ziyoni wasanduka chipululu, Yerusalemu ndi wamasiye.

11Nyumba yanu yopatulika ndi yaulemu, kumene makolo athu ankakutamandani,

yatenthedwa ndi moto

ndipo malo onse amene tinkawakonda asanduka bwinja.

12Inu Yehova, zonse zachitikazi, kodi mungokhala osatithandiza?

Kodi mudzapitirizabe kukhala chete ndi kutilangabe mopitirira muyeso?

Chinese Contemporary Bible (Traditional)

以賽亞書 64:1-12

1願你裂天而降!

願群山在你面前戰抖!

2求你使敵人認識你的威名,

使列國在你面前顫抖,

如火燒乾柴使水沸騰。

3你曾降臨,行超乎我們預料的可畏之事,

那時群山在你面前戰抖。

4自古以來,從未見過,

也未聽過有任何神明像你一樣為信奉他的人行奇事。

5你眷顧樂於行義、遵行你旨意的人。

我們不斷地犯罪惹你發怒,

我們怎能得救呢?

6我們的善行不過像骯髒的衣服,

我們都像污穢的人,

像漸漸枯乾的葉子,

我們的罪惡像風一樣把我們吹去。

7無人呼求你,

無人向你求助,

因為你掩面不理我們,

讓我們在自己的罪中滅亡。

8但耶和華啊,你是我們的父親。

我們是陶泥,你是窯匠,

你親手造了我們。

9耶和華啊,求你不要大發烈怒,

不要永遠記著我們的罪惡。

我們都是你的子民,

求你垂顧我們。

10你的眾聖城已淪為荒場,

甚至錫安已淪為荒場,

耶路撒冷已淪為廢墟。

11我們那聖潔、華美的殿——我們祖先頌讚你的地方已被焚毀,

我們珍愛的一切都被摧毀。

12耶和華啊,你怎能坐視不理呢?

你仍然保持緘默,使我們重重地受罰嗎?