Yesaya 61 – CCL & CCB

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yesaya 61:1-11

Uthenga Wabwino wa Yehova

1Mzimu wa Ambuye Yehova uli pa ine,

chifukwa Yehova wandidzoza

kuti ndilalikire uthenga wabwino kwa anthu osauka.

Wandituma kuti ndikatonthoze anthu osweka mtima,

ndikalengeze kwa akapolo kuti alandire ufulu

ndiponso kuti ndikamasule a mʼndende.

2Wandituma kuti ndikalengeze nthawi imene Yehova adzapulumutsa anthu ake;

za tsiku limene Yehova adzalanga adani a anthu ake.

Wandituma kuti ndikatonthoze olira.

3Wandituma kuti ndiwakonzere olira a ku Ziyoni,

nkhata ya maluwa yokongola

mʼmalo mwa phulusa,

ndiwapatse mafuta achikondwerero

mʼmalo mwa kulira.

Ndiwapatse chovala cha matamando

mʼmalo mwa mtima wopsinjika.

Ndipo iwo adzatchedwa mitengo ya thundu yamphamvu yachilungamo,

yoyidzala Yehova

kuti Iye mwini apezemo ulemerero wake.

4Adzamanganso mabwinja akale a mzinda

ndipo malo amene anawonongeka kalekale aja adzakonzanso.

Adzakonzanso mizinda imene inapasuka,

imene yakhala yowonongeka kwa nthawi yayitali kwambiri.

5Anthu achilendo adzakutumikirani; adzazidyetsa ziweto zanu;

iwo adzagwira ntchito mʼminda yanu ya mpesa.

6Ndipo inu mudzatchedwa ansembe a Yehova,

adzakutchulani kuti ndinu atumiki a Mulungu wathu.

Mudzadyerera chuma cha mitundu ya anthu,

ndipo mudzanyadira ulemu umene mwalandira.

7Chifukwa manyazi awo anali owirikiza;

ndi kuti munalandira

chitonzo ndi kutukwana,

adzakondwera ndi cholowa chawo,

tsono adzalandira cholowa chawo cha chigawo cha dziko mowirikiza,

ndipo chimwemwe chamuyaya chidzakhala chawo.

8“Pakuti Ine Yehova, ndimakonda chilungamo;

ndimadana ndi zakuba ndi zoyipa.

Anthu anga ndidzawapatsa mphotho mokhulupirika

ndikupangana nawo pangano losatha.

9Ana awo adzakhala odziwika pakati pa mitundu ya anthu

ndipo adzukulu awo adzakhala otchuka pakati pa anthu a mitundu ina.

Aliyense wowaona adzazindikira

kuti ndi anthu amene Yehova wawadalitsa.”

10Ine ndikusangalala kwambiri chifukwa cha Yehova;

moyo wanga ukukondwera chifukwa cha Mulungu wanga.

Pakuti Iye wandiveka zovala zachipulumutso,

ndipo wandiveka mkanjo wachilungamo.

Zili ngati mkwati wovala nkhata ya maluwa mʼkhosi mwake,

ndiponso ngati mkwatibwi wovala mikanda yamtengowapatali.

11Monga momwe nthaka imameretsa mbewu

ndiponso monga munda umakulitsa mbewu zimene anadzala,

momwemonso Ambuye Yehova adzaonetsa chilungamo ndi matamando

pamaso pa mitundu yonse ya anthu.

Chinese Contemporary Bible (Simplified)

以赛亚书 61:1-11

大喜的讯息

1主耶和华的灵在我身上,因为耶和华膏立了我,

让我传福音给贫穷的人,

差遣我医治伤心的人,

宣告被掳的人得释放、

被囚的人得自由;

2宣告我们上帝耶和华的恩年和祂报仇的日子,

安慰一切悲哀的人;

3以华冠取代锡安哀伤者头上的灰尘,

以喜乐的膏油取代他们的哀伤,

以颂赞的外袍取代他们的沮丧。

他们将被称为耶和华所栽种的公义橡树,

以彰显祂的荣耀。

4他们必重修古老的荒场,

在久已毁坏之地重建荒废的城邑。

5异乡人要为你们牧放羊群,

外族人要为你们耕种田地、

照料葡萄园。

6你们要被称为耶和华的祭司,

我们上帝的臣仆。

你们必享用各国的财宝,

夸耀自己拥有他们的财富。

7你们曾经蒙受耻辱,

如今将得到双倍的福分;

你们曾经遭受屈辱,

如今将因得到产业而快乐。

你们将在自己的土地上得到双倍的福分,

享受永远的快乐。

8“因为我耶和华喜爱公正,

憎恶抢劫之罪。

我必凭信实赏赐我的子民,

与他们立永远的约。

9他们的后代必享誉列国,

子孙必名闻万邦,

看见的人都承认他们是蒙上帝赐福之民。”

10我因耶和华而无比喜乐,

因我的上帝而心里快乐,

因为祂给我穿上救恩的衣服、

披上公义的袍子,

使我像戴上华冠的新郎,

又像戴上饰物的新娘。

11大地怎样使嫩苗长出,

园子怎样使种子发芽,

主耶和华必照样使公义与颂赞在万民中滋长。