Yesaya 60 – CCL & CCB

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yesaya 60:1-22

Ulemerero wa Ziyoni

1“Dzuka, wala, pakuti kuwala kwako kwafika,

ndipo ulemerero wa Yehova wakuwalira.

2Taona, mdima waphimba dziko lapansi

ndipo mdima wandiweyani wagwa pa anthu a mitundu ina,

koma Yehova adzakuwalira iwe,

ndipo ulemerero wake udzaoneka pa iwe.

3Mitundu ya anthu idzatsata kuwunika kwako

ndipo mafumu adzalondola kunyezimira kwa mʼbandakucha wako.

4“Tukula maso ako, yangʼanayangʼana ndipo ona zimene zikuchitika.

Onse akusonkhana ndipo akubwera kwa iwe;

ana ako a amuna akubwera kuchokera kutali

ndipo ana ako aakazi anyamulidwa mʼmanja.

5Ukadzaona zimenezi udzasangalala kwambiri,

mtima wako udzalumpha ndi kudzaza ndi chimwemwe;

chuma chakunyanja chidzabwera kwa iwe

chuma cha mitundu ya anthu chidzabwera kwa iwe.

6Gulu la ngamira lidzaphimba dziko lako,

ngamira zingʼonozingʼono zidzachokera ku Midiyani ndi ku Efai.

Ndipo onse a ku Seba adzabwera

atanyamula golide ndi lubani

uku akutamanda Yehova.

7Ziweto zonse za ku Kedara adzazisonkhanitsa kwa inu,

nkhosa zazimuna za ku Nabayoti zidzakutumikirani;

zidzalandiridwa monga chopereka pa guwa langa la nsembe,

ndipo ndidzakongoletsa Nyumba yanga.

8“Kodi ndi zayani izo zikuwuluka ngati mitambo,

ngati kapena nkhunda zobwerera ku zisa zawo?

9Ndithu, izi ndi sitima za pa madzi zochokera ku mayiko akutali;

patsogolo pali sitima zapamadzi za ku Tarisisi,

zikubweretsa ana ako ochokera kutali,

pamodzi ndi siliva wawo ndi golide wawo,

kudzalemekeza Yehova Mulungu wako,

Woyerayo wa Israeli,

pakuti Iye wakuvekani inu ulemerero.

10“Alendo adzamanganso malinga ako,

ndipo mafumu awo adzakutumikira.

Ngakhale ndinakukantha ndili wokwiya,

koma tsopano ndidzakukomera mtima ndikukuchitira chifundo.

11Zipata zako zidzakhala zotsekula nthawi zonse,

sadzazitseka nthawi zonse, usana ndi usiku,

kotero anthu adzabwera kwa iwe ndi chuma chawo,

akuyenda pa mdipiti mafumu awo ali patsogolo.

12Pakuti mtundu wa anthu ndi mafumu amene sakutumikira iwe;

adzawonongeka kotheratu.

13“Adzabwera nayo kwa iwe mitengo ya payini,

mkuyu ndi naphini imene ili mʼnkhalango ya Lebanoni

kuti adzakongoletsere malo a nyumba yanga yopatulika;

ndipo ndidzalemekeza malo amene Ine ndimapondapo.

14Ana aja amene anakuzunzani adzabwera ndipo adzakugwadirani;

onse amene anakunyozani adzagwada pansi pa mapazi anu.

Ndipo adzakutchani kuti Mzinda wa Yehova;

Ziyoni mzinda wa Woyerayo wa Israeli.

15“Ngakhale anthu anakusiya nadana nawe,

koma Ine ndidzakukuza mpaka muyaya,

ndipo udzakhala malo a chimwemwe

cha anthu amibado yonse.

16Udzamwa mkaka wa mitundu ya anthu

ndi kuleredwa pa maere aufumu,

motero udzadziwa kuti Ine Yehova, ndine Mpulumutsi wako,

Momboli wako ndiye Wamphamvu wa Yakobo.

17Ndidzakupatsa golide mʼmalo mwa mkuwa,

ndi siliva mʼmalo mwa chitsulo.

Ndidzakupatsa mkuwa mʼmalo mwa thabwa

ndi chitsulo mʼmalo mwa miyala.

Olamulira ako adzakhala a mtendere.

Ndidzasandutsa okulamulira kuti akhale achilungamo.

18Ziwawa sizidzamvekanso mʼdziko lako,

bwinja kapena chiwonongeko sizidzapezeka mʼdziko lako,

ndidzakhala malinga ako okuteteza

ndipo udzanditamanda.

19Sipadzakhala dzuwa kuti likuwunikire,

kapena mwezi kuti uwunikire usiku,

pakuti Yehova ndiye adzakhale kuwunika kwako kwa muyaya,

ndipo Mulungu wako adzakhala ulemerero wako.

20Dzuwa lako silidzalowanso,

ndipo mwezi wako sudzazimiriranso;

Yehova adzakhala kuwunika kwako kwamuyaya,

ndipo masiku a mavuto ako adzatha.

21Ndipo anthu ako onse adzakhala olungama

ndipo dzikolo lidzakhala lawo mpaka muyaya.

Iwo ndi mphukira imene Ine ndayidzala,

ntchito ya manja anga,

kuti aonetse ulemerero wanga.

22Kabanja kakangʼono kadzasanduka fuko,

kafuko kakangʼono kudzasanduka mtundu wamphamvu.

Ine ndine Yehova,

nthawi yake ikafika ndidzazichita zimenezi mofulumira.”

Chinese Contemporary Bible (Simplified)

以赛亚书 60:1-22

锡安将来的荣耀

1起来,发光吧!因为你的光已经来到,

耶和华的荣耀已经照在你身上。

2看啊,黑暗遮盖大地,

幽暗笼罩万民,

但耶和华必照耀你,

祂的荣耀必照在你身上。

3万国要来就你的光,

君王要来就你的曙光。

4耶和华说:“举目四望吧,

众人正聚到你面前,

你的儿子们从远方来,

你的女儿们被护送回来。

5你看见后就容光焕发,

心花怒放,

因为海上的货物要归给你,

列国的财富都要归给你。

6米甸以法的骆驼必成群结队而来,

布满你的地面;

示巴人必带着黄金和乳香来颂赞耶和华。

7基达的羊群必集合到你那里,

尼拜约的公羊必供你使用,

它们在我的坛上必蒙悦纳。

我要使我荣美的殿更荣美。

8“这些好像云彩飞来,

又像鸽子飞回巢穴的是谁?

9众海岛的人都等候我,

他施的船只行在前面,

从远处把你的儿子和他们的金银财宝一同带来,

以尊崇你的上帝耶和华——以色列的圣者,

因为我已经使你得到荣耀。

10“外族人要为你建造城墙,

他们的君王要服侍你。

我曾发怒击打你,

如今我要施恩怜悯你。

11你的城门要一直敞开,

昼夜不关,

好让各国的君王带着他们的人民和财物列队前来向你朝贡。

12不肯向你俯首称臣的国家必灭亡,被彻底摧毁。

13黎巴嫩引以为荣的松树、杉树和黄杨树都要运到你这里,

用来装饰我的圣所;

我要使我脚踏之处充满荣耀。

14欺压你之人的子孙要向你下拜,

藐视你的人要在你脚前跪拜。

他们要称你为耶和华的城,

以色列圣者的锡安

15“虽然你曾被撇弃、被厌恶,

无人从你那里经过,

但我要使你永远尊贵,

世世代代都充满欢乐。

16你必吸各国的乳汁,

吃王室的奶水。

那时,你就知道我耶和华是你的救主,

是你的救赎主,是雅各的大能者。

17“我要以金代替铜,

以银代替铁,

以铜代替木头,

以铁代替石头。

我要使和平做你的官长,

使公义做你的首领。

18你国中再没有暴力,

境内再没有破坏和毁灭的事;

你必给你的城墙取名叫‘拯救’,

给你的城门取名叫‘赞美’。

19“太阳不再作你白昼的光,

月亮也不再给你光辉,

因为耶和华要作你永远的光,

你的上帝要成为你的荣耀。

20你的太阳不再落下,

你的月亮也不再消失,

因为耶和华要作你永远的光,

你悲哀的日子将要结束。

21你的人民都必成为义人,

永远拥有这土地。

他们是我亲手栽种的树苗,

以彰显我的荣耀。

22最小的家族要变成千人的大家族,

最弱的一国要成为强国。

时候一到,我耶和华必迅速成就这些事。”