Yesaya 58 – CCL & KJV

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yesaya 58:1-14

Kusala Kwenikweni

1“Fuwula kwambiri, usaleke.

Mawu ako amveke ngati lipenga.

Uwawuze anthu anga za kulakwa kwawo;

uwuze nyumba ya Yakobo za machimo awo.

2Pakuti tsiku ndi tsiku amafunafuna Ine;

amaoneka ngati a chidwi chofuna kudziwa zimene ndimafuna,

kukhala ngati kuti ndi dziko limene limachita zolondola

ndipo silinasiye zolamulira za Mulungu wake.

Amandipempha kuti ndigamule mlandu wawo mwachilungamo

ndipo amaonetsa chidwi chofuna kukhala pafupi ndi Mulungu.

3Anthu akufunsa kuti, ‘Chifukwa chiyani ife tasala

kudya pamene Inu simukulabadirapo?

Kodi ife tavutikiranji nʼkudzichepetsa

pamene Inu simunasamalepo?’ ”

Yehova akuti, “Komatu tsiku lanu losala kudya, mumachita zinthu zokukondweretsani,

ndipo mumazunza antchito anu onse.

4Mumati uku mukusala kudya, uku mukukangana ndi kumenyana,

mpaka kumenyana ndi nkhonya zopweteka.

Kusala kudya mukuchitiramu musayembekezere kuti mawu anu amveka kumwamba.

5Kodi kusala kudya kumene ndimakufuna Ine nʼkumeneku,

kungokhala tsiku loti munthu adzichepetse basi?

Kodi ndi tsiku loti munthu angowerama pansi ngati bango

ndi kumayala ziguduli nʼkuthirapo phulusa nʼkugonapo?

Kodi ndiye mumati kusala kudya kumeneko,

tsiku lokondweretsa Yehova?

6“Kodi si uku kusala kudya kumene Ine ndimakufuna:

Kumasula maunyolo ozunzizira anthu

ndi kumasula zingwe za goli,

kupereka ufulu kwa oponderezedwa

ndi kuphwanya goli lililonse?

7Anthu anjala kodi mwawagawira chakudya chanu?

Osowa ndi ongoyendayenda,

kodi mwawapatsa malo ogona?

Munthu wausiwa kodi mwamupatsa chovala?

8Mukatero chipulumutso chanu chidzabwera ngati mʼbandakucha,

ndipo mabala anu adzachira msangamsanga;

chilungamo chanu chidzakutsogolerani

ndipo ulemerero wa Yehova udzakhala chokutchinjirizani kumbuyo kwanu.

9Mukamadzapemphera Yehova adzakuyankhani;

mukadzapempha thandizo, Iye adzati: Ine ndili pano.

“Ngati muleka kuzunza anzanu,

ngati musiya kuloza chala ndiponso kunena zoyipa za anzanu.

10Ndipo ngati mudyetsa anthu anjala,

ndi kuthandiza anthu oponderezedwa,

pamenepo kuwala kwanu kudzaonekera mu mdima,

ndipo usiku wanu udzakhala ngati usana.

11Yehova adzakutsogolerani nthawi zonse;

adzakwaniritsa zosowa zanu mʼdziko longʼalukangʼaluka dzuwa

ndipo adzalimbitsa matupi anu.

Mudzakhala ngati dimba la madzi ambiri,

ngati kasupe amene madzi ake saphwa.

12Anthu ako adzamanganso nyumba zimene zakhala mabwinja nthawi yayitali,

ndipo adzamanganso pa maziko akalekale;

inu mudzatchedwa okonza makoma opasuka.

Anthu okonza misewu ndi nyumba zake.

13“Muzisunga osaphwanya Sabata;

musamachite zimene mukufuna pa masiku anga opatulika,

tsiku la Sabata lizikhala tsiku lachisangalalo.

Tsiku lopatulika la Yehova muzililemekeza

posayenda mʼnjira zanu,

kapena kuchita zimene mukufuna ndi kuyankhula zopandapake,

14mukatero mudzapeza chimwemwe mwa Yehova,

ndipo ndidzakukwezani ndi kukupambanitsani pa dziko lonse lapansi.

Mudzadyerera dziko limene ndinapatsa Yakobo kholo lanu.”

Yehova wayankhula ndi pakamwa pake.

King James Version

Isaiah 58:1-14

1Cry aloud, spare not, lift up thy voice like a trumpet, and shew my people their transgression, and the house of Jacob their sins.58.1 aloud: Heb. with the throat 2Yet they seek me daily, and delight to know my ways, as a nation that did righteousness, and forsook not the ordinance of their God: they ask of me the ordinances of justice; they take delight in approaching to God.

3¶ Wherefore have we fasted, say they, and thou seest not? wherefore have we afflicted our soul, and thou takest no knowledge? Behold, in the day of your fast ye find pleasure, and exact all your labours.58.3 labours: or, things wherewith ye grieve others: Heb. griefs 4Behold, ye fast for strife and debate, and to smite with the fist of wickedness: ye shall not fast as ye do this day, to make your voice to be heard on high.58.4 ye shall…: or, ye fast not as this day 5Is it such a fast that I have chosen? a day for a man to afflict his soul? is it to bow down his head as a bulrush, and to spread sackcloth and ashes under him? wilt thou call this a fast, and an acceptable day to the LORD?58.5 a day…: or, to afflict his soul for a day? 6Is not this the fast that I have chosen? to loose the bands of wickedness, to undo the heavy burdens, and to let the oppressed go free, and that ye break every yoke?58.6 the heavy…: Heb. the bundles of the yoke58.6 oppressed: Heb. broken 7Is it not to deal thy bread to the hungry, and that thou bring the poor that are cast out to thy house? when thou seest the naked, that thou cover him; and that thou hide not thyself from thine own flesh?58.7 cast…: or, afflicted

8¶ Then shall thy light break forth as the morning, and thine health shall spring forth speedily: and thy righteousness shall go before thee; the glory of the LORD shall be thy rereward.58.8 be…: Heb. gather thee up 9Then shalt thou call, and the LORD shall answer; thou shalt cry, and he shall say, Here I am. If thou take away from the midst of thee the yoke, the putting forth of the finger, and speaking vanity; 10And if thou draw out thy soul to the hungry, and satisfy the afflicted soul; then shall thy light rise in obscurity, and thy darkness be as the noonday: 11And the LORD shall guide thee continually, and satisfy thy soul in drought, and make fat thy bones: and thou shalt be like a watered garden, and like a spring of water, whose waters fail not.58.11 drought: Heb. droughts58.11 fail: Heb. lie, or, deceive 12And they that shall be of thee shall build the old waste places: thou shalt raise up the foundations of many generations; and thou shalt be called, The repairer of the breach, The restorer of paths to dwell in.

13¶ If thou turn away thy foot from the sabbath, from doing thy pleasure on my holy day; and call the sabbath a delight, the holy of the LORD, honourable; and shalt honour him, not doing thine own ways, nor finding thine own pleasure, nor speaking thine own words: 14Then shalt thou delight thyself in the LORD; and I will cause thee to ride upon the high places of the earth, and feed thee with the heritage of Jacob thy father: for the mouth of the LORD hath spoken it.