Yesaya 50 – CCL & LCB

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yesaya 50:1-11

Tchimo la Israeli, Kumvera kwa Mtumiki

1Yehova akuti,

“Kalata imene ndinasudzulira amayi

anu ili kuti?

Kapena mwa anthu amene ndili nawo ngongole,

ndinakugulitsani kwa ati?

Inu munagulitsidwa ku ukapolo chifukwa cha machimo anu;

amayi anu anachotsedwa chifukwa cha kulakwa kwanu.

2Nʼchifukwa chiyani pamene ndinabwera kudzakupulumutsani panalibe munthu?

Pamene ndinayitana, nʼchifukwa chiyani panalibe wondiyankha?

Kodi dzanja langa ndi lalifupi kuti nʼkulephera kukuwombolani?

Kodi ndilibe mphamvu zokupulumutsirani?

Ndi kudzudzula kokha ndinawumitsa nyanja yayikulu,

mitsinje ndinayisandutsa chipululu;

nsomba za mʼmenemo zinawola chifukwa chosowa madzi;

ndipo zinafa ndi ludzu.

3Ndinaphimba thambo ndi mdima

ndipo chiguduli chinakhala chofunda chake.”

4Ambuye Yehova anandiphunzitsa mawu oyenera kuyankhula

kudziwa mawu olimbitsa mtima anthu ofowoka.

Mmawa mulimonse amandidzutsa,

amathwetsa khutu langa kuti ndimve monga amachitira munthu amene akuphunzira.

5Ambuye Yehova wanditsekula makutu anga,

ndipo sindinakhale munthu wowukira

ndipo sindinabwerere mʼmbuyo.

6Ndinapereka msana wanga kwa ondimenya

masaya anga ndinawapereka kwa anthu ondizula ndevu;

sindinawabisire nkhope yanga

anthu ondinyoza ndi ondilavulira.

7Popeza Ambuye Yehova amandithandiza,

sindidzachita manyazi.

Tsono ndalimba mtima ngati msangalabwi,

chifukwa ndikudziwa kuti sindidzachita manyazi.

8Wondikhalira kumbuyo ali pafupi,

ndaninso amene adzandiyimba mlandu?

Abwere kuti tionane maso ndi maso!

Mdani wanga ndi ndani?

Abweretu kuti tilimbane!

9Ambuye Yehova ndiye amene amandithandiza.

Ndaninso amene adzanditsutsa?

Onse adzatha ngati chovala

chodyedwa ndi njenjete.

10Ndani mwa inu amaopa Yehova

ndi kumvera mawu a mtumiki wake?

Aliyense woyenda mu mdima,

popanda chomuwunikira,

iye akhulupirire dzina la Yehova

ndi kudalira Mulungu wake.

11Koma tsopano inu nonse amene mumasonkha moto

ndi kuyatsa sakali za moto kufuna kuwononga anzanu,

lowani mʼmoto wanu womwewo.

Pitani mu sakali za moto zimene mwayatsa.

Ndipo ine Yehova

ndiye amene ndidzakugwetsereni mazunzowo.

Luganda Contemporary Bible

Isaaya 50:1-11

Ekibi Kyawukanya Isirayiri ku Katonda

150:1 a Ma 24:1; Yer 3:8; Kos 2:2 b Nek 5:5; Mat 18:25 c Ma 32:30; Is 52:3Bw’ati bw’ayogera Mukama nti,

“Ebbaluwa egoba nnyammwe, kwe namugobera eri ludda wa?

Oba nabatunda eri ani?

Mwatundibwa lwa bikolwa byammwe ebibi;

olw’obutali butuukirivu bwammwe nnyammwe kyeyava agobwa.

250:2 a Is 41:28 b Kbl 11:23; Is 59:1 c Lub 18:14 d Kuv 14:22; Yos 3:16Lwaki bwe najja tewaali muntu n’omu?

Bwe nakoowoola lwaki tewaali muntu n’omu annyanukula?

Omukono gwange gwali mumpi nnyo okukununula?

Mbuliddwa amaanyi agakununula?

Laba nnyinza okwogera obwogezi ennyanja n’ekalira,

emigga ne ngifuula eddungu,

ebyennyanja byamu ne bifa ennyonta,

ne bivunda olw’okubulwa amazzi.

350:3 Kub 6:12Nyambaza eggulu,

n’ekizikiza ne nkiwa ebibukutu okulibikka.”

450:4 a Kuv 4:12 b Mat 11:28 c Zab 5:3; 119:147; 143:8Mukama Ayinzabyonna ampadde olulimi

oluyigirizibbwa, mmanye ebigambo ebigumya abo abakooye.

Anzukusa buli nkya,

buli nkya anzukusa okuwulira by’anjigiriza.

550:5 a Is 35:5 b Mat 26:39; Yk 8:29; 14:31; 15:10; Bik 26:19; Beb 5:8Mukama Ayinzabyonna azibudde okutu kwange

ne siba mujeemu.

Sizzeeyo mabega.

650:6 a Is 53:5; Mat 27:30; Mak 14:65; 15:19; Luk 22:63 b Kgb 3:30; Mat 26:67N’awaayo omugongo gwange eri abankuba,

n’amatama gange eri abo abankunyuulako ekirevu.

Saakweka maaso gange eri abo abansekerera

n’eri abo abanfujjira amalusu.

750:7 a Is 42:1 b Ez 3:8-9Kubanga Mukama Ayinzabyonna anyamba

kyennaava siswazibwa.

Noolwekyo kyenvudde n’egumya

era mmanyi nti siriswazibwa.

850:8 a Is 43:26; Bar 8:32-34 b Is 41:1Kubanga oyo ampolereza ali kumpi.

Ani alinnumiriza omusango?

Twolekagane obwenyi.

Ani annumiriza?

Ajje annumbe.

950:9 a Is 41:10 b Yob 13:28; Is 51:8Mukama Ayinzabyonna y’anyamba.

Ani alinsalira omusango?

Bonna balikaddiwa bayulike ng’ekyambalo;

ennyenje ziribalya.

1050:10 a Is 49:3 b Is 26:4Ani ku mmwe atya Mukama,

agondera ekigambo ky’omuweereza we?

Oyo atambulira mu kizikiza,

atalina kitangaala

yeesige erinnya lya Mukama

era yeesigame ku Katonda we.

1150:11 a Nge 26:18 b Yak 3:6 c Is 65:13-15Naye mmwe mwenna abakoleeza omuliro,

ne mwekoleereza ettaala z’omuliro,

mutambulire mu kitangaala ky’omuliro gwammwe,

ne mu kitangaala kye ttaala ze mukoleezeza.

Naye kino kye munaafuna okuva mu mukono gwange;

muligalamira mu nnaku.