Yesaya 49 – CCL & LCB

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yesaya 49:1-26

Mtumiki wa Yehova

1Mverani Ine, inu anthu a pa zilumba

tcherani khutu, inu anthu a mayiko akutali:

Yehova anandiyitana ine ndisanabadwe,

ananditchula dzina ndili mʼmimba ya amayi anga.

2Iye anasandutsa pakamwa panga kukhala ngati lupanga lakuthwa,

anandibisa mu mthunzi wa dzanja lake;

Iye anandisandutsa ngati muvi wakuthwa

ndipo anandibisa mʼchimake.

3Iye anati kwa ine, “Ndiwe mtumiki wanga, Israeli.

Anthu adzanditamanda chifukwa cha iwe.”

4Koma Ine ndinati, “Ine ndinkaganiza kuti ndinagwira ntchito

ndi kuwononga mphamvu zanga pachabe,

koma ayi, zondiyenera zili mʼmanja a Yehova,

ndipo mphotho yanga ili mʼmanja mwa Mulungu wanga.”

5Yehova anandiwumba ine

mʼmimba mwa amayi anga kuti ndikhale mtumiki wake

kuti ndibweze fuko la Yakobo kwa Iye

ndi kusonkhanitsa Israeli kwa Iye,

choncho ndimalemekezeka mʼmaso mwa Yehova,

ndipo ndimapeza mphamvu mwa Mulungu wanga.

6Yehovayo tsono akuti,

“Nʼchinthu chochepa kwambiri kwa iwe kuti ukhale mtumiki wanga,

kuti udzutse mafuko a Yakobo

ndi kuwabweretsa kwawo Aisraeli amene anapulumuka.

Choncho iwe udzakhala ngati chowunikira,

udzafikitsa uthenga wa chipulumutso changa ku mathero a dziko lapansi.”

7Yehova Mpulumutsi ndi Woyerayo wa Israeli akuyankhula,

Woyerayo wa Israeli akunena,

amene mitundu ya anthu inamuda,

amenenso anali kapolo wa mafumu ankhanza uja kuti,

“Mafumu adzaona ntchito ya chipulumutso changa ndipo adzayimirira.

Akalonga nawonso adzagwada pansi.

Zimenezi zidzachitika chifukwa cha Yehova amene ndi wokhulupirika

ndi Woyerayo wa Israeli amene wakusankha iwe.”

Kubwezeretsedwa kwa Israeli

8Yehova akuti,

“Pa nthawi imene ndinakukomera mtima ndinakuyankha,

ndipo pa tsiku lachipulumutso ndinakuthandiza;

ndinakusunga ndi kukusandutsa

kuti ukhale pangano kwa anthu,

kuti dziko libwerere mwakale

ndi kuti cholowa changa chowonongeka chija ndichigawegawenso.

9Ndidzawuza a mʼndende kuti atuluke

ndi a mu mdima kuti aonekere poyera.

“Adzapeza chakudya mʼmphepete mwa njira

ndi msipu pa mʼmalo owuma.

10Iwo sadzamva njala kapena ludzu,

kutentha kwa mʼchipululu kapena dzuwa silidzawapsereza;

chifukwa Iye amene amawachitira chifundo adzawatsogolera

ndi kuwaperekeza ku akasupe a madzi.

11Mapiri anga onse ndidzawasandutsa njira yoyendamo,

ndipo misewu yanga yayikulu ndidzayikweza.

12Taonani, anthu anga adzachokera kutali,

ena kumpoto, ena kumadzulo,

enanso adzachokera ku chigawo cha Asuwani.”

13Imbani mwachimwemwe, inu zolengedwa zamlengalenga;

kondwera, iwe dziko lapansi;

imbani nyimbo inu mapiri!

Pakuti Yehova watonthoza mtima anthu ake,

ndipo wachitira chifundo anthu ake ovutika.

14Koma Ziyoni anati, “Yehova wandisiya,

Ambuye wandiyiwala.”

15“Kodi amayi angathe kuyiwala mwana wawo wakubere

ndi kusachitira chifundo mwana amene anabereka iwo eni?

Ngakhale iye angathe kuyiwala,

Ine sindidzakuyiwala iwe!

16Taona, ndakulemba iwe mʼzikhantho zanga;

makoma ako ndimawaona nthawi zonse.

17Amisiri odzakumanganso akubwerera mofulumira,

ndipo amene anakupasula akuchokapo.

18Kweza maso ako ndipo uyangʼaneyangʼane

ana ako onse akusonkhana ndipo akubwera kwa iwe.

Yehova akuti, ‘Ine Yehova wamoyo,

anthu ako adzakhala ngati chinthu chodzikongoletsa

chimene mkwatibwi wavala pa mkono pake.’

19“Ngakhale unasanduka bwinja ndi kuwonongedwa

ndipo dziko lako ndi kusakazidwa,

chifukwa cha kuchuluka kwa anthu malo okhalamo adzakhala operewera

ndipo amene anakuwononga iwe aja adzakhala kutali.

20Ana obadwa nthawi yako yachisoni

adzanena kuti,

‘Malo ano atichepera,

tipatse malo ena woti tikhalemo.’

21Tsono iwe udzadzifunsa kuti,

‘Kodi ndani anandiberekera ana amenewa?

Ana anga onse anamwalira ndipo sindinathenso kukhala ndi ana ena;

ndinapita ku ukapolo ndipo ndinachotsedwa.

Ndani anawalera ana amenewa?

Ndinatsala ndekha,

nanga awa, achokera kuti?’ ”

22Zimene Ambuye Yehova akunena ndi izi,

“Taonani, Ine ndidzakodola Anthu a mitundu ina kuti abwere.

Ndidzawakwezera anthu a mitundu ina mbendera yanga kuti abwere.

Tsono adzabwera ndi ana ako aamuna atawanyamula mʼmanja mwawo

ndipo adzanyamula ana ako aakazi pa mapewa awo.

23Mafumu adzakhala abambo wongokulera

ndipo akazi a mafumu adzakhala amayi wongokulera.

Iwo adzagwetsa nkhope

zawo pansi.

Ndiye inu mudzazindikira kuti Ine ndine Yehova;

iwo amene amadalira Ine sadzakhumudwa.”

24Kodi mungathe kulanda anthu ankhondo zofunkha zawo,

kapena kupulumutsa anthu ogwidwa mʼdzanja la munthu wankhanza?

25Koma zimene Yehova akunena ndi izi,

“Ankhondo adzawalanda amʼndende awo,

ndipo munthu woopsa adzamulanda zofunkha zawo;

ndidzalimbana ndi amene amalimbana nanu,

ndipo ndidzapulumutsa ana anu.

26Anthu amene anakuponderezani adzadya mnofu wawo omwe;

adzamwa magazi awo omwe ngati aledzera ndi vinyo.

Zikadzatero anthu onse adzadziwa

kuti Ine Yehova, ndine Mpulumutsi wanu,

Momboli wanu, Wamphamvu wa Yakobo.”

Luganda Contemporary Bible

Isaaya 49:1-26

Omuweereza wa Mukama

149:1 a Is 44:24; 46:3; Mat 1:20 b Is 7:14; 9:6; 44:2; Yer 1:5; Bag 1:15Mumpulirize mmwe ebizinga,

mmwe muwulire kino amawanga agali ewala.

Nnali sinazaalibwa Mukama n’ampita.

Bwe nnali nkyali mu lubuto lwa mmange n’ayatula erinnya lyange.

249:2 Is 11:4; Kub 1:16Yakola akamwa kange ng’ekitala eky’obwogi,

nankweka mu kisiikirize ky’omukono gwe.

Yanfuula akasaale akazigule

era nankweka mu mufuko gwe.

349:3 a Zek 3:8 b Is 44:23Era n’aŋŋamba nti, “Ggwe muweereza wange, Isirayiri,

mu ggwe mwe ndiweerwa ekitiibwa.”

449:4 a Is 65:23 b Is 35:4Naye ne njogera nti, “Nteganidde bwereere,

amaanyi gange ng’amalidde bwereere era gafudde busa.

Kyokka ate Mukama yannamula,

n’empeera yange eri ne Katonda wange!”

549:5 a Is 11:12 b Is 43:4Era kaakano Mukama ayogera,

oyo eyammumba mu lubuto okubeera omuweereza we,

okukomyawo Yakobo gy’ali

era n’okukuŋŋaanya Isirayiri gy’ali.

Kubanga ndi wa kitiibwa mu maaso ga Mukama

era Katonda wange afuuse amaanyi gange.

649:6 a Luk 2:32 b Bik 13:47*Mukama agamba nti,

“Eky’okubeera omuweereza wange

n’okuzza amawanga ga Yakobo

era n’okukomyawo abantu ba Isirayiri kintu kitono nnyo.

Nzija kukufuula ekitangaala eri abamawanga,

olyoke oleete obulokozi bwange eri ensi yonna.”

749:7 a Is 48:17 b Zab 22:6; 69:7-9 c Is 52:15Bw’ati bw’ayogera Mukama,

Omununuzi era Omutukuvu wa Isirayiri,

eri oyo eyanyoomebwa n’akyayibwa amawanga,

eri omuweereza w’abafuzi nti,

“Bakabaka baliyimirira ne bakuwa ekitiibwa,

abalangira balikulaba ne bakuvuunamira.

Kino kiribaawo ku lwa Mukama, omwesigwa Omutukuvu wa Isirayiri,

oyo akulonze.”

Isirayiri Azzibwawo

849:8 a Zab 69:13 b 2Ko 6:2* c Is 26:3 d Is 42:6 e Is 44:26Bw’ati bw’ayogera Mukama nti,

“Ndikwanukula mu biro mwe ndisiimira,

ku lunaku olw’obulokozi ndikuyamba.

Ndikukuuma ne nkufuula endagaano eri abantu,

muliddayo ku ttaka lyammwe ne muddizibwa ebitundu byammwe ebyazika,

949:9 a Is 42:7; 61:1; Luk 4:19 b Is 41:18nga mugamba abasibe nti, ‘Muveemu,’

n’abo abali mu kizikiza nti, ‘Mube n’eddembe!’

“Banaaliranga ku mabbali g’ekkubo,

ne ku ntikko z’obusozi bwonna obwereere banasangangako omuddo.

1049:10 a Is 33:16 b Zab 121:6; Kub 7:16 c Is 14:1 d Is 35:7Tebaalumwenga njala newaakubadde ennyonta,

ebbugumu ly’omu ddungu teriibakwatenga newaakubadde omusana okubookya.

Oyo abakwatirwa ekisa alibakulembera,

anaabatwalanga awali enzizi z’amazzi.

1149:11 a Is 11:16 b Is 40:4Era ndifuula ensozi zange zonna okuba amakubo

era enguudo zange ennene zirigulumizibwa.

1249:12 Is 43:5-6Laba, abantu bange balidda okuva ewala,

abamu, baliva mu bukiikakkono

n’abalala ebuvanjuba, n’abalala bave mu nsi ye Sinimu.”

1349:13 a Is 44:23 b Is 40:1Yogerera waggulu n’essanyu, era jjaguza ggwe ensi.

Muyimbe mmwe ensozi!

Kubanga Mukama agumya abantu be era alisaasira abantu be ababonyaabonyezebwa.

14Naye Sayuuni n’ayogera nti, “Mukama andese,

era Mukama wange anneerabidde.”

1549:15 Is 44:21“Nnyina w’omwana ayinza okwerabira omwana we gw’ayonsa,

n’atasaasira mwana eyava mu lubuto lwe?

Weewaawo, wadde ng’ayinza okumwerabira

naye nze sirikwerabira.

1649:16 a Lu 8:6 b Zab 48:12-13; Is 62:6Laba, nkuwandiise mu bibatu by’engalo zange;

ebisenge byo binaabeeranga mu maaso gange.

1749:17 Is 10:6Abaana bo banguwa okujja era abakuzimba balisukkuluma ku bakuzikiriza

era abo abaakuzikirizanga balikuvaamu bagende.

1849:18 a Is 43:5; 54:7; 60:4 b Is 45:23 c Is 52:1Yimusa amaaso go otunule enjuuyi zonna olabe.

Abantu bo beekuŋŋaanya bajja gy’oli.

Nga bwe ndi Katonda omulamu,

balikwesiimisa, obambale ng’ebikomo n’emidaali ebyebbeeyi

ng’omugole bw’ayambala malidaadi,” bw’ayogera Mukama.

1949:19 a Is 54:1, 3 b Is 5:6 c Zek 10:10“Wadde nga wazika n’olekebwa awo ensi yo n’ezikirizibwa,

kaakano ojja kubeera mufunda nga toja mu bantu bo,

era abo abakuteganya

banaakubeeranga wala.

2049:20 Is 54:1-3Abantu bo abazaalibwa mu buwaŋŋanguse

lumu balyogera ng’owulira nti,

‘Ekifo kino nga kifuuse kifunda bulala;

tuwe ekifo aw’okubeera.’

2149:21 a Is 5:13 b Is 1:8N’olyoka oyogera mu mutima gwo nti,

‘Ani eyanzaalira abaana bano bonna?

Nafiirwa abaana bange bonna ng’ate ndi mugumba.

Nawaŋŋangusibwa ne nsigala nzekka.

Bano baava ludda wa?

Nasigala nzekka,

naye ate bano, baava wa?’ ”

Okuzzibwawo kwa Isirayiri mu Kitiibwa

2249:22 a Is 11:10 b Is 60:4Bw’atyo bw’ayogera Mukama Katonda nti, “Laba, ndikolera abamawanga obubonero

era ndiyimusiza abantu ebbendera yange:

era balireeta batabani bo nga babasitulidde mu bifuba

ne bawala bo nga babasitulidde ku bibegabega byabwe.

2349:23 a Is 60:3, 10-11 b Is 60:16 c Zab 72:9 d Mi 7:17Era bakabaka be balibeera ba kitammwe babalabirire,

ne bannabagereka babeere bamaama ababayonsa.

Balivuunama mu maaso go nga batunudde wansi;

balikomba enfuufu y’omu bigere byo.

Olwo lw’olimanya nti nze Mukama,

abo bonna abannindirira n’abansuubiriramu tebalikwatibwa nsonyi.”

2449:24 Mat 12:29; Luk 11:21Omunyago guyinza okuggyibwa ku mutabaazi,

oba omuwambe omutuukirivu okuwona omutabaazi?

2549:25 a Is 14:2 b Yer 50:33-34 c Is 25:9; 35:4Naye bw’ati bw’ayogera Mukama:

“N’oyo eyawambibwa omutabaazi alisumululwa ateebwe,

n’omunyago guggyibwe ku mulabe wo,

kubanga ndiyomba n’oyo ayomba naawe,

era ndirokola mponye abaana bo.

2649:26 a Is 9:4 b Is 9:20 c Kub 16:6 d Ez 39:7Ndiriisa abakujooga ennyama yaabwe bo.

Era balittiŋŋana batamiire omusaayi gwabwe, nga wayini.

Olwo abalina omubiri bonna bamanye nti nze Mukama Omulokozi wo,

Omununuzi wo,

ow’Amaanyi owa Yakobo.”