Yesaya 5 – CCL & KJV

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yesaya 5:1-30

Nyimbo ya Munda Wamphesa

1Ndidzamuyimbira bwenzi langa

nyimbo yokamba za munda wake wa mpesa:

Wokondedwa wanga anali ndi munda wamphesa

pa phiri la nthaka yachonde.

2Anatipula nachotsa miyala yonse

ndipo anawokamo mipesa yabwino kwambiri.

Anamanga nsanja yolondera pakati pa mundawo

ndipo anasemanso mopsinyira mphesa mʼmundamo.

Ndipo iye anayembekezera kuti mundawo udzabala mphesa zabwino,

koma ayi, unabala mphesa zosadya.

3“Tsopano, inu amene mumakhala mu Yerusalemu ndi inu anthu a ku Yuda,

weruzani pakati pa ine ndi munda wanga wa mpesawu.

4Kodi nʼchiyaninso china chimene ndikanachitira munda wanga wa mpesa

kupambana chomwe ndawuchitira kale?

Pamene ndinkayembekezera kuti udzabala mphesa zabwino,

bwanji unabala mphesa zosadya?

5Tsopano ndikuwuzani

chimene ndidzawuchitire munda wanga wa mpesa:

ndidzachotsa mpanda wake,

ndipo mundawo udzawonongeka;

ndidzagwetsa khoma lake,

ndipo nyama zidzapondapondamo.

6Ndidzawusandutsa tsala,

udzakhala wosatengulira ndi wosalimira

ndipo mudzamera mkandankhuku ndi minga ina.

Ndidzalamula mitambo

kuti isagwetse mvula pa mundapo.”

7Munda wamphesa wa Yehova Wamphamvuzonse

ndi Aisraeli,

ndipo anthu a ku Yuda ndiwo

minda yake yomukondweretsa.

Ndipo Iye ankayembekezera chiweruzo cholungama, mʼmalo mwake anaona kuphana;

mʼmalo mwa chilungamo Iye anamva kulira kwa anthu ozunzika.

Tsoka ndi Chiweruzo

8Tsoka kwa inu amene mumangokhalira kulumikiza nyumba,

ndipo mumangokhalira kuwonjezera minda,

mpaka mutalanda malo onse

kuti muzikhalamo nokha mʼdzikomo.

9Yehova Wamphamvuzonse wayankhula ine ndikumva kuti,

“Ndithudi nyumba zambirizo zidzasanduka mabwinja,

nyumba zazikulu zokongolazo zidzakhala zopanda anthu.

10Munda wamphesa wa maekala khumi udzatulutsa vinyo wodzaza mbiya imodzi,

kufesa madengu khumi a mbewu, zokolola zake zidzangodzaza dengu limodzi.”

11Tsoka kwa iwo amene amadzuka mmamawa

nathamangira chakumwa choledzeretsa,

amene amamwa mpaka usiku

kufikira ataledzera kotheratu.

12Pa maphwando awo pamakhala azeze, apangwe,

matambolini, zitoliro ndi vinyo,

ndipo sasamala ntchito za Yehova,

salemekeza ntchito za manja ake.

13Motero anthu anga adzatengedwa ukapolo

chifukwa cha kusamvetsa zinthu;

atsogoleri awo olemekezeka adzafa ndi njala,

ndipo anthu wamba ochuluka adzafa ndi ludzu.

14Nʼchifukwa chake ku manda sikukhuta

ndipo kwayasama kwambiri kukamwa kwake;

mʼmandamo mudzagweranso anthu otchuka a mu Yerusalemu pamodzi ndi anthu wamba ochuluka;

adzagweramo ali wowowo, nʼkuledzera kwawoko.

15Ndipo munthu aliyense adzatsitsidwa,

anthu onse adzachepetsedwa,

anthu odzikuza adzachita manyazi.

16Koma Yehova Wamphamvuzonse adzalemekezedwa chifukwa cha chiweruzo chake cholungama.

Ndipo Mulungu woyera adzadzionetsa kuti ndi woyera pochita chilungamo chake.

17Tsono nkhosa zidzadya pamenepo ngati pabusa pawo;

ana ankhosa adzadya mʼmabwinja a anthu olemera.

18Tsoka kwa amene amadzikokera tchimo ndi zingwe zachinyengo,

ndipo amadzikokera zoyipa ndi zingwe zokokera ngolo,

19amene amanena kuti, “Yehova afulumire,

agwire ntchito yake mwamsanga

kuti ntchitoyo tiyione.

Ntchito zionekere,

zimene Woyerayo wa Israeli akufuna kuchita,

zichitike kuti tizione.”

20Tsoka kwa amene zoyipa amaziyesa zabwino

ndipo zabwino amaziyesa zoyipa,

amene mdima amawuyesa kuwala

ndipo kuwala amakuyesa mdima,

amene zowawasa amaziyesa zotsekemera

ndipo zotsekemera amaziyesa zowawasa.

21Tsoka kwa amene amadziona ngati anzeru

ndipo amadziyesa ochenjera.

22Tsoka kwa zidakwa zimene zimayika mtima pa vinyo

ndipo ndi akatswiri posakaniza zakumwa,

23amene amamasula olakwa chifukwa cha chiphuphu

koma amayipitsa mlandu wa munthu wosalakwa.

24Nʼchifukwa chake monga momwe moto umawonongera chiputu

ndipo monga momwe udzu wowuma umapsera mʼmalawi a moto,

momwemonso mizu yawo idzawola

ndipo maluwa awo adzafota ndi kuwuluka ngati fumbi;

chifukwa akana malamulo a Yehova Wamphamvuzonse,

ndipo anyoza mawu a Woyerayo wa Israeli.

25Nʼchifukwa chake mkwiyo wa Yehova wayakira anthu ake;

watambasula dzanja lake pa anthuwo ndipo akuwakantha

Mapiri akugwedezeka,

ndipo mitembo ya anthu yangoti mbwee mʼmisewu ngati zinyalala.

Komabe ngakhale watero, mkwiyo wake sunaleke,

dzanja lake likanali chitambasulire;

26Yehova wakweza mbendera kuyitana mtundu wa anthu akutali,

akuyitana anthuwo ndi likhweru kuti abwere kuchokera ku mathero a dziko lapansi.

Awo akubwera,

akubweradi mofulumira kwambiri!

27Palibe ndi mmodzi yemwe amene akutopa kapena kupunthwa,

palibe amene akusinza kapena kugona;

palibe lamba wa mʼchiwuno amene akumasuka,

palibe chingwe cha nsapato chimene chaduka.

28Mivi yawo ndi yakuthwa,

mauta awo onse ndi okoka,

ziboda za akavalo awo nʼzolimba ngati mwala wansagalabwi,

magaleta awo ndi aliwiro ngati kamvuluvulu.

29Kufuwula kwawo kuli ngati kubangula kwa mkango,

amabangula ngati misona ya mkango;

imadzuma pamene ikugwira nyama

ndipo imapita nayo popanda ndi mmodzi yemwe woyipulumutsa.

30Tsiku limenelo mitundu ya anthu idzabangula

ngati mkokomo wa madzi a mʼnyanja.

Ndipo wina akakayangʼana dzikolo

adzangoona mdima ndi zovuta;

ngakhale kuwala kudzasanduka mdima chifukwa cha mitambo.

King James Version

Isaiah 5:1-30

1Now will I sing to my wellbeloved a song of my beloved touching his vineyard. My wellbeloved hath a vineyard in a very fruitful hill:5.1 a very…: Heb. the horn of the son of oil 2And he fenced it, and gathered out the stones thereof, and planted it with the choicest vine, and built a tower in the midst of it, and also made a winepress therein: and he looked that it should bring forth grapes, and it brought forth wild grapes.5.2 fenced: or, made a wall about5.2 made: Heb. hewed 3And now, O inhabitants of Jerusalem, and men of Judah, judge, I pray you, betwixt me and my vineyard. 4What could have been done more to my vineyard, that I have not done in it? wherefore, when I looked that it should bring forth grapes, brought it forth wild grapes? 5And now go to; I will tell you what I will do to my vineyard: I will take away the hedge thereof, and it shall be eaten up; and break down the wall thereof, and it shall be trodden down:5.5 trodden…: Heb. for a treading 6And I will lay it waste: it shall not be pruned, nor digged; but there shall come up briers and thorns: I will also command the clouds that they rain no rain upon it. 7For the vineyard of the LORD of hosts is the house of Israel, and the men of Judah his pleasant plant: and he looked for judgment, but behold oppression; for righteousness, but behold a cry.5.7 his…: Heb. plant of his pleasures5.7 oppression: Heb. a scab

8¶ Woe unto them that join house to house, that lay field to field, till there be no place, that they may be placed alone in the midst of the earth!5.8 they: Heb. ye 9In mine ears said the LORD of hosts, Of a truth many houses shall be desolate, even great and fair, without inhabitant.5.9 In…: or, This is in mine ears, saith the LORD, etc5.9 Of a…: Heb. If not, etc 10Yea, ten acres of vineyard shall yield one bath, and the seed of an homer shall yield an ephah.

11¶ Woe unto them that rise up early in the morning, that they may follow strong drink; that continue until night, till wine inflame them!5.11 inflame: of, pursue 12And the harp, and the viol, the tabret, and pipe, and wine, are in their feasts: but they regard not the work of the LORD, neither consider the operation of his hands.

13¶ Therefore my people are gone into captivity, because they have no knowledge: and their honourable men are famished, and their multitude dried up with thirst.5.13 honourable…: Heb. glory are men of famine 14Therefore hell hath enlarged herself, and opened her mouth without measure: and their glory, and their multitude, and their pomp, and he that rejoiceth, shall descend into it. 15And the mean man shall be brought down, and the mighty man shall be humbled, and the eyes of the lofty shall be humbled: 16But the LORD of hosts shall be exalted in judgment, and God that is holy shall be sanctified in righteousness.5.16 God…: or, the holy God: Heb. the God the holy 17Then shall the lambs feed after their manner, and the waste places of the fat ones shall strangers eat.

18Woe unto them that draw iniquity with cords of vanity, and sin as it were with a cart rope: 19That say, Let him make speed, and hasten his work, that we may see it: and let the counsel of the Holy One of Israel draw nigh and come, that we may know it!

20¶ Woe unto them that call evil good, and good evil; that put darkness for light, and light for darkness; that put bitter for sweet, and sweet for bitter!5.20 call…: Heb. say concerning evil, It is good, etc 21Woe unto them that are wise in their own eyes, and prudent in their own sight!5.21 in their own sight: Heb. before their face 22Woe unto them that are mighty to drink wine, and men of strength to mingle strong drink: 23Which justify the wicked for reward, and take away the righteousness of the righteous from him! 24Therefore as the fire devoureth the stubble, and the flame consumeth the chaff, so their root shall be as rottenness, and their blossom shall go up as dust: because they have cast away the law of the LORD of hosts, and despised the word of the Holy One of Israel.5.24 fire: Heb. tongue of fire 25Therefore is the anger of the LORD kindled against his people, and he hath stretched forth his hand against them, and hath smitten them: and the hills did tremble, and their carcases were torn in the midst of the streets. For all this his anger is not turned away, but his hand is stretched out still.5.25 torn: or, as dung

26¶ And he will lift up an ensign to the nations from far, and will hiss unto them from the end of the earth: and, behold, they shall come with speed swiftly: 27None shall be weary nor stumble among them; none shall slumber nor sleep; neither shall the girdle of their loins be loosed, nor the latchet of their shoes be broken: 28Whose arrows are sharp, and all their bows bent, their horses’ hoofs shall be counted like flint, and their wheels like a whirlwind: 29Their roaring shall be like a lion, they shall roar like young lions: yea, they shall roar, and lay hold of the prey, and shall carry it away safe, and none shall deliver it. 30And in that day they shall roar against them like the roaring of the sea: and if one look unto the land, behold darkness and sorrow, and the light is darkened in the heavens thereof.5.30 sorrow: or, distress5.30 and the light…: or, when it is light, it shall be dark in the destructions thereof