Israeli ndi Nkhutukumve
1“Mverani izi, inu nyumba ya Yakobo,
inu amene amakutchani dzina lanu Israeli,
ndinu a fuko la Yuda,
inu mumalumbira mʼdzina la Yehova,
ndi kupemphera kwa Mulungu wa Israeli,
ngakhale osati mʼchoonadi kapena mʼchilungamo.
2Komabe inu mumadzitcha nzika za mzinda wopatulika
ndipo mumadalira Mulungu wa Israeli,
amene dzina lake ndi Yehova Wamphamvuzonse:
3Zimene zinachitika poyamba ndinalosera kalekale,
zinatuluka mʼkamwa mwanga ndipo ndinazilengeza;
tsono mwadzidzidzi ndinachitapo kanthu ndipo zinachitikadi.
4Pakuti Ine ndinadziwa kuti iwe ndiwe nkhutukumve
wa nkhongo gwaa,
wa mutu wowuma.
5Ine ndinakuwuziratu zinthu izi kalekale lomwe;
zisanachitike ndinazilengezeratu kwa iwe
kuti unganene kuti,
‘Fano langa ndilo lachita zimenezi,
kapena kuti fano langa losema ndi kamulungu kanga kachitsulo ndiwo analamula kuti zimenezi zichitike.’
6Inu munamva zinthu zimenezi.
Kodi inu simungazivomereze?
“Kuyambira tsopano mpaka mʼtsogolo ndidzakuwuzani zinthu zatsopano
zinthu zobisika zimene simunazidziwe konse.
7Zinthu zimenezi zikulengedwa tsopano lino, osati kalekale;
munali musanazimve mpaka lero lino.
Choncho inu simunganene kuti,
‘Zimenezi ndiye ayi, ndinazidziwa kale.’
8Inu simunazimvepo kapena kuzidziwa;
makutu anu sanali otsekuka.
Tsono Ine ndinadziwa bwino kuti ndinu anthu achiwembu ndi kuti
chiyambire ubwana wanu munatchedwa owukira.
9Ine ndikuchedwetsa mkwiyo wanga chifukwa cha dzina langa.
Ndikukulezerani ukali wanga kuti anthu andilemekeze.
Sindidzakuwonongani kotheratu.
10Taonani, ndinakuyeretsani ngati siliva;
ndinakuyesani mʼngʼanjo yamasautso.
11Chifukwa cha ulemu wanga, chifukwa cha ulemu wanga Ine ndikuchita zimenezi.
Ndingalole bwanji kuti ndinyozeke?
Ulemerero wanga sindidzawupereka kwa wina.
Kumasulidwa kwa Israeli
12“Tamvera Ine, iwe Yakobo,
Israeli, amene ndinakuyitana:
Mulungu uja Woyamba
ndi Wotsiriza ndine.
13Inde dzanja langa linamanga maziko a dziko lapansi,
dzanja langa lamanja linafunyulula mlengalenga.
Ndi mawu anga ndinalenga kumwamba
ndi dziko lapansi.
14“Sonkhanani pamodzi inu nonse ndipo mvetserani:
Ndani mwa mafano anu amene analoseratu za zinthu izi?
Wokondedwa wa Yehova uja adzachita
zomwe Iye anakonzera Babuloni;
dzanja lake lidzalimbana ndi Kaldeya.
15Ine, Inetu, ndayankhula;
ndi kumuyitana
ndidzamubweretsa ndine
ndipo adzakwaniritsa zolinga zake.
16“Bwerani pafupi ndipo mvetserani izi:
“Kuyambira pachiyambi sindinayankhule mobisa;
pa nthawi imene zinkachitika zimenezi Ine ndinali pomwepo.”
Ndipo tsopano Ambuye Yehova wandipatsa Mzimu wake
ndi kundituma.
17Yehova, Mpulumutsi wanu,
Woyerayo wa Israeli akuti,
“Ine ndine Yehova Mulungu wanu,
amene ndimakuphunzitsa kuti upindule,
ndimakutsogolera pa njira yoyenera kuyitsata.
18Ngati iwe ukanangosamalira zolamulira zanga,
bwenzi mtendere wako ukanakhala ngati mtsinje,
ndi chipulumutso chako ngati mafunde a pa nyanja.
19Zidzukulu zako zikanachuluka ngati mchenga,
ana ako akanachuluka ngati fumbi;
dzina lawo silikanachotsedwa pamaso panga
ndipo silikanafafanizidwa konse.”
20Tulukani mʼdziko la Babuloni!
Thawani dziko la Kaldeya!
Lengezani zimenezi ndi mawu a chisangalalo
ndipo muzilalikire
mpaka kumathero a dziko lapansi;
muzinena kuti, “Yehova wawombola Yakobo mtumiki wake.”
21Iwo sanamve ludzu pamene Yehova ankawatsogolera mʼchipululu;
anawapatsa madzi otuluka mʼthanthwe;
anangʼamba thanthwelo ndipo
munatuluka madzi.
22“Palibe mtendere kwa anthu ochimwa,” akutero Yehova.
Откровение упрямому Исроилу
1– Слушайте это, потомки Якуба,
вы, кто зовётся именем Исроила
и ведёт свой род от Иуды,
вы, кто клянётся именем Вечного
и призывает Бога Исроила –
но не в истине и не в праведности;
2вы, кто зовёт себя жителями святого города Иерусалима
и полагается на Бога Исроила;
Его имя – Вечный, Повелитель Сил.
3Я предрекал минувшее заранее,
уста Мои возвещали его,
и Я объявлял о нём;
затем внезапно Я действовал,
и всё исполнялось.
4Потому что знал Я, что вы упрямы,
сухожилия шеи вашей – железные,
лоб ваш – медный.
5Поэтому Я и говорил вам заранее;
прежде чем всё исполнится, Я возвещал вам,
чтобы вы не сказали:
«Наши идолы сделали это;
наши деревянные истуканы и литые боги предначертали это».
6Вы слышали об этом – взгляните же!
Неужели вы это не признаёте?
Отныне и впредь Я буду говорить вам о новом,
о скрытом, неведомом вам.
7Это исполняется сейчас, а не раньше;
до сегодняшнего дня вы об этом не слышали,
и не сможете сказать:
«Да, мы это знали».
8Вы не слышали и не понимали;
издревле не было ухо ваше открыто.
Ведь Я знаю, как вы вероломны;
вы с рождения был наречены отступниками.
9Ради Своего имени Я сдерживал гнев;
ради Своей славы Я удерживал его от вас,
чтобы вас не искоренить.
10Вот Я очистил вас, хотя и не как серебро;
Я испытал вас в печи страданий.
11Ради Себя, ради Самого Себя Я делаю это.
Зачем Моему имени быть в поругании?
Славы Своей не отдам другому.
Освобождение Исроила
12– Слушай Меня, Якуб,
Исроил, призванный Мой!
Я – Тот же;
Я – первый, и Я – последний.
13Моя рука заложила основания земли,
Моя правая рука распростёрла небеса;
когда Я призову их,
они вместе предстанут.
14Соберитесь, вы все, и слушайте:
кто из идолов это предрёк?
Избранник Вечного исполнит Его замысел о Вавилоне
и обратит свою руку на вавилонян48:14 Здесь подразумевается Куруш, царь Персии. См. также сноски на 41:2 и 44:28..
15Я, Я сказал и призвал его.
Я его приведу,
и он преуспеет в деле своём.
16Приблизьтесь ко Мне и слушайте:
с самого начала Я говорил не в тайне;
с тех пор, как это началось, Я – там.
И ныне Владыка Вечный
послал Меня и Духа Своего48:16 Или: «И ныне Владыка Вечный и Его Дух послали Меня»..
17Так говорит Вечный,
твой Искупитель, святой Бог Исроила:
– Я – Вечный, Бог твой,
Тот, Кто учит тебя полезному,
Тот, Кто ведёт тебя по пути,
которым ты должен идти.
18О, если бы ты внимал Моим повелениям,
твой мир стал бы как река,
твоя праведность – словно волны морские.
19Твоих потомков было бы много, как песка,
твоих детей – как бессчётных песчинок.
Их имя не стёрлось бы
и не исчезло бы предо Мной.
20Уходите из Вавилона,
бегите от вавилонян!
Возвещайте эту весть с криком радости,
объявляйте и распространяйте до краёв земли:
«Вечный искупил Своего раба Якуба!»
21Они не томились жаждой,
когда вёл Он их через пустыни;
из скалы источал Он им воду,
рассекал Он скалу, и струились воды.
22– Но нет мира нечестивым, –
говорит Вечный.