Yesaya 47 – CCL & CARST

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yesaya 47:1-15

Kugwa kwa Babuloni

1“Tsika, ndi kukhala pa fumbi,

iwe namwali, Babuloni;

khala pansi wopanda mpando waufumu,

iwe namwali, Kaldeya

pakuti sadzakutchulanso wanthete kapena woyenera

kumugwira mosamala.

2Tenga mphero ndipo upere ufa;

chotsa nsalu yako yophimba nkhope

kwinya chovala chako mpaka ntchafu

ndipo woloka mitsinje.

3Maliseche ako adzakhala poyera

ndipo udzachita manyazi.

Ndidzabwezera chilango

ndipo palibe amene adzandiletse.”

4Woyerayo wa Israeli ndiye Mpulumutsi wathu,

dzina lake ndi Yehova Wamphamvuzonse.

5“Khala chete, ndipo lowa mu mdima,

iwe namwali, Kaldeya;

chifukwa sadzakutchulanso

mfumukazi ya maufumu.

6Ndinawakwiyira anthu anga,

osawasamalanso.

Ndinawapereka manja mwako,

ndipo iwe sunawachitire chifundo.

Iwe unachitira nkhanza

ngakhale nkhalamba.

7Iwe unati, ‘Ine ndidzakhalapo nthawi zonse

ngati mfumukazi.’

Koma sunaganizire zinthu izi

kapena kusinkhasinkha za mmene ziti zidzathere.

8“Ndipo tsopano, tamvera, iwe wongokonda zokondweretsawe,

amene ukukhala mosatekesekawe,

umaganiza mu mtima mwako kuti,

‘Ine ndi Ine, ndipo kupatula ine palibenso wina.

Sindidzakhala konse mkazi wamasiye,

ndipo ana anga sadzamwalira.’

9Koma mʼkamphindi, ndiponso tsiku limodzi,

zinthu ziwiri izi zidzakuchitikira:

ana ako kukufera komanso kukhala mkazi wamasiye.

Zimenezi zidzakuchitikira kwathunthu

ngakhale ali ndi amatsenga ambiri

ndi mawula amphamvu.

10Iwe unkadalira kuyipa kwako

ndipo unati, ‘Palibe amene akundiona.’

Kuchenjera ndi nzeru zako zidzakusokoneza,

choncho ukuganiza mu mtima mwako kuti,

‘Ine ndine basi, ndipo kupatula ine palibenso wina.’

11Ngozi yayikulu idzakugwera

ndipo sudzadziwa momwe ungayipewere ndi matsenga ako.

Mavuto adzakugwera

ndipo sudzatha kuwachotsa;

chipasupasu chimene iwe sukuchidziwa

chidzakugwera mwadzidzidzi.

12“Pitiriza tsono kukhala ndi matsenga ako,

pamodzi ndi nyanga zako zochulukazo,

wakhala ukuzigwiritsa ntchito kuyambira ubwana wako.

Mwina udzatha kupambana

kapena kuopsezera nazo adani ako.

13Malangizo onse amene unalandira angokutopetsa basi!

Abwere patsogolopa anthu amene amatanthauzira za kumwamba kuti adzakupulumutseni.

Abwere amene amayangʼana nyenyezi, ndi kumalosera mwezi ndi mwezi

zimene ziti zidzakuchitikire.

14Ndithudi, anthuwo ali ngati phesi;

adzapsa ndi moto.

Sangathe kudzipulumutsa okha

ku mphamvu ya malawi a moto.

Awa si makala a moto woti wina nʼkuwotha;

kapena moto woti wina nʼkuwukhalira pafupi.

15Umu ndi mmene adzachitire amatsenga,

anthu amene wakhala ukugwira nawo ntchito

ndi kuchita nawo malonda chiyambire cha ubwana wako.

Onse adzamwazika ndi mantha,

sipadzakhala ndi mmodzi yemwe wokupulumutsa.”

Священное Писание (Восточный перевод), версия для Таджикистана

Исаия 47:1-15

Падение Вавилона

1– Сойди, сядь в пыли,

девственная дочь Вавилона47:1 Девственная дочь Вавилона – олицетворение Вавилона и его жителей. Так же и «дочь халдеев» в ст. 1 и 5.;

сядь на землю, а не на трон,

дочь халдеев.

Больше не назовут тебя

нежной и утончённой.

2Возьми жернова, мели муку;

сними своё покрывало.

Подбери свои юбки, оголи свои ноги,

переходи через реки.

3Пусть обнажится твоя нагота,

откроются взглядам твои срамные места.

Я отомщу,

никого не пощажу.

4Наш Искупитель – святой Бог Исроила;

имя Его – Вечный, Повелитель Сил.

5– Сиди в молчании, ступай во тьму,

дочь халдеев;

не назовут тебя больше

владычицей царств.

6Разгневался Я на народ Мой

и унизил Своё наследие;

Я отдал их в руки твои,

и ты не явила им милосердия.

Даже на стариков

положила ты крайне тяжёлое ярмо.

7Ты сказала: «Вовеки пребуду владычицей!»

Но не задумалась,

не подумала о том,

что может произойти.

8Итак, послушай, искательница удовольствий,

живущая в безопасности

и говорящая себе:

«Со мной никто не сравнится.

Никогда я не овдовею,

не познаю потери детей».

9И то и другое постигнет тебя,

внезапно, в один день –

утрата детей и вдовство.

В полной мере постигнут они тебя,

невзирая на множество твоих чародейств

и великую силу твоих заклинаний.

10Ты полагалась на своё злодейство

и говорила: «Никто меня не видит».

Твоя мудрость и знание сбили тебя с толку,

когда ты сказала себе:

«Со мной никто не сравнится».

11Придёт к тебе беда,

и не будешь знать, как её отвести.

Обрушится на тебя несчастье,

и не отвратишь его выкупом.

Внезапно постигнет тебя крушение,

которого ты не предвидишь.

12Ну что ж, держись своих заклинаний

и множества своих чародейств,

в которых ты с юности преуспела.

Может быть, получится,

может быть, внушишь кому-то ужас.

13Многочисленные советы лишь утомили тебя!

Пусть встанут твои астрологи,

эти звездочёты, предсказывающие по новолуниям;

пусть спасут тебя от того, что тебя постигнет.

14Вот они как солома,

палит их огонь.

Самих себя не могут спасти

от власти пламени.

Это не угли, чтобы погреться,

не костёр, чтобы посидеть перед ним!

15Вот что они для тебя –

те, с кем трудилась ты,

с кем торговала с юности!

Каждый из них бредёт в свою сторону;

спасти тебя некому.