Yesaya 44 – CCL & APSD-CEB

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yesaya 44:1-28

Israeli Wosankhidwa wa Yehova

1Yehova akuti, “Mvera tsopano, iwe Yakobo, mtumiki wanga,

Israeli, amene ndinakusankha.

2Yehova

amene anakupanga iwe, anakuwumba iwe mʼmimba ya amayi ako,

ndi amene adzakuthandiza iwe. Iye akuti,

Usachite mantha, iwe Yakobo, mtumiki wanga,

Yesuruni, amene ndinakusankha.

3Pakuti ndidzathira madzi pa nthaka yowuma,

ndi kuyendetsa mitsinje mʼdziko lowuma;

ndidzatumiza Mzimu wanga pa ana anu,

ndi kutsitsa madalitso anga pa zidzukulu zanu.

4Iwo adzakula ngati udzu wothirira bwino

ndi ngati bango lomera mʼmbali mwa mitsinje ya madzi oyenda.

5Wina adzanena kuti, ‘Ine ndine wa Yehova;’

wina adzadzitcha yekha wa banja la Yakobo;

winanso adzalemba pa dzanja lake, ‘Wa Yehova’

ndipo adzadzitcha wa banja la Israeli.

Yehova, Osati Mafano

6“Yehova Mfumu

ndi Mpulumutsi wa Israeli, Yehova Wamphamvuzonse akuti:

Ine ndine woyamba ndi wotsiriza;

palibenso Mulungu wina koma Ine ndekha.

7Ndani nanga angafanane ndi Ine? Muloleni kuti ayankhule.

Muloleni andifotokozere ndi kundiyalira bwino lomwe

zimene zinachitika kuyambira pamene ndinkakhazikitsa anthu anga akalekale,

ndi ziti zimene zidzachitike;

inde, muloleni alosere zimene zikubwera.

8Musanjenjemere, musachite mantha.

Kodi sindinakuwuzeni zimenezi ndi kuzilosera kalekale lomwe?

Inu ndinu mboni zanga. Kodi aliponso Mulungu wina kupatula Ine?

Ayi, palibe Thanthwe linanso limene sindikulidziwa.”

9Onse amene amapanga mafano ngachabe,

ndipo milungu imene amayilemekeza ndi yopanda phindu.

Iwo amene amapembedza mafano ndi wosaona;

ndipo sazindikira kanthu. Choncho adzawachititsa manyazi.

10Ndani amasema mulungu ndi kuwumba fano,

limene silingamupindulire?

11Iye pamodzi ndi anzake onse adzawachititsa manyazi;

amisiri a mafano ndi anthu chabe.

Aloleni onse asonkhane ndi kuyima pabwalo la milandu;

onse adzaopsedwa ndipo adzachita manyazi.

12Mmisiri wa zitsulo amatenga chitsulo

ndipo amachiyika pa makala amoto;

ndi dzanja lake lamphamvu

amachisula pochimenya ndi nyundo.

Pambuyo pake mʼmisiri uja amamva njala natha mphamvu;

iye samwa madzi, ndipo amalefuka.

13Mmisiri wa matabwa nayenso amayeza mtengo ndi chingwe

ndipo amajambula chithunzi ndi cholembera;

amasema bwinobwino ndi chipangizo chake

ndipo amachiwongola bwino ndi chida chake.

Amachipanga ngati munthu,

munthu wake wokongola

kuti aliyike mʼnyumba yake yachipembedzo.

14Amagwetsa mitengo ya mkungudza,

mwinanso amatenga mtengo wa payini kapena wa thundu

nʼkudzisankhira mtengo wabwino pakati pa mitengo ya mʼnkhalango,

ndipo amadzala mtengo wa payini ndi kuwuleka kuti ukule ndi mvula.

15Mitengoyo munthu amachitako nkhuni;

nthambi zina amasonkhera moto wowotha,

amakolezera moto wophikira buledi

ndi mbali ina ya mtengowo amapangira mulungu ndipo amapembedza;

iye amapanga fano ndi kumaligwadira.

16Chigawo china cha mtengowo amasonkhera moto

wowotcherapo nyama imene

amadya, nakhuta.

Iye amawotha motowo ndipo amanena kuti,

“Aa! Ndikumva kutentha; pano pali moto.”

17Chigawo chotsala amapanga kamulungu, fano lake limenelo;

amaligwadira ndi kulipembedza.

Amapemphera kwa fanolo ndipo amanena kuti,

“Iwe ndiwe mulungu wanga, ndipulumutse.”

18Anthu otere sadziwa kanthu, samvetsa kanthu kalikonse;

maso awo ndi omatirira ndipo sangathe kuona,

ndipo mitu yawo ndi yogontha kotero sangathe kumvetsa.

19Palibe amene amayima nʼkulingalira.

Palibe wanzeru kapena womvetsa zinthu bwino woti nʼkunena kuti,

chigawo china cha mtengowo ndinasonkhera moto;

pa makala ake ndinaphikira buledi,

ndinawotchapo nyama ndipo ndinadya.

Chigawo chotsalachi ndipangire chinthu chonyansachi.

Kodi ndidzagwadira mtengo?

20Munthu wotere ali ngati wodya phulusa, maganizo ake opusa amusocheretsa;

motero kuti sangathe kudzipulumutsa yekha kapena kudzifunsa kuti,

“Kodi chinthu chili mʼmanja mwangachi si chabodza?”

21Yehova akuti, “Iwe Yakobo, kumbukira zinthu izi

popeza kuti ndiwe mtumiki wanga, iwe Israeli.

Ine ndinakupanga iwe, ndiwe mtumiki wanga;

iwe Israeli, sindidzakuyiwala.

22Ndachotsa zolakwa zako ngati mitambo,

ndi machimo ako ngati nkhungu ya mmawa.

Bwerera kwa Ine,

popeza ndakupulumutsa.”

23Imbani mwachimwemwe, inu zolengedwa zamlengalenga, pakuti Yehova wachita zimenezi;

fuwula, iwe dziko lapansi.

Imbani nyimbo, inu mapiri,

inu nkhalango ndi mitengo yonse,

chifukwa Yehova wawombola Yakobo,

waonetsa ulemerero wake mwa Israeli.

Anthu Adzakhalanso mu Yerusalemu

24Yehova Mpulumutsi wanu, amene

anakuwumbani mʼmimba ya amayi anu akuti:

“Ine ndine Yehova,

amene anapanga zinthu zonse,

ndinatambasula ndekha zinthu zakuthambo,

ndinayala ndekha dziko lapansi.

25Ndine amene ndinalepheretsa mipingo ya anthu onyenga,

ndipo ndimapusitsa owombeza mawula.

Ndimasokoneza anthu a nzeru,

ndi kuonetsa kuti nzeru zawo nʼzopusa.

26Ndine amene ndimatsimikiza mawu a atumiki ake

ndi kukwaniritsa zimene analosera amithenga ake.

“Ndine amene ndinanena za Yerusalemu kuti mudzakhalanso anthu.

Ndinanenanso za mizinda ya Yuda kuti idzamangidwanso.

Za mabwinja awo ndinanena kuti ndidzawawutsanso.

27Ndine amene ndinawuza nyanga yayikulu kuti, ‘Uma’

ndipo ndidzawumitsa mitsinje yako.

28Ndine amene ndinanena kwa Koresi kuti, ‘Iye ndiye mʼbusa wanga,’

ndipo adzachita zonse zimene ndikufuna;

iye adzalamula kuti, ‘Yerusalemu amangidwenso’

ndi kuti, ‘Maziko a Nyumba ya Mulungu ayikidwenso.’ ”

Ang Pulong Sa Dios

Isaias 44:1-28

Ang Saad sa Dios ngadto sa Israel

1“Apan karon, pamati, O Israel nga akong alagad, ang katawhan nga akong pinili, nga mga kaliwat ni Jacob. 2Ako, ang Ginoo, mao ang naghimo ug nagtabang kanimo. Ayaw kahadlok, ikaw nga akong alagad ug pinili nga katawhan. 3Kay hatagan ko ikaw ug tubig nga mohupay sa imong kauhaw ug mobasa sa imong malang yuta. Gamhan ko sa akong Espiritu ang imong mga kaliwat ug panalanginan ko sila. 4Mouswag sila sama sa labong nga mga sagbot nga abunda sa tubig o sa mga kahoy sa daplin sa sapa. 5May moingon, ‘Iya ako sa Ginoo,’ ug may ubang moingon, ‘Kaliwat ako ni Jacob.’ May mosulat usab diha sa ilang kamot sa ngalan sa Ginoo, ug maghunahuna sa ilang kaugalingon nga sakop sa katawhan sa Israel.

Walay Kapuslanan ang mga dios-dios

6“Mao kini ang giingon sa Ginoo, ang Hari ug Manluluwas sa Israel, ang Makagagahom nga Ginoo: Ako ang una ug ang kataposan. Wala nay laing Dios gawas kanako. 7Kinsa ang sama kanako? Ipasulti siya sa akong atubangan kon unsay nahitabo sukad sa panahon nga gitukod ang usa ka nasod, ang akong katawhan, ug kon unsa ang mahitabo sa umaabot. 8Ayaw kamo kahadlok o kalisang. Dili ba nga gipadayag ko na man kaninyo kaniadto pa ang akong katuyoan? Ug kamo mismo ang akong mga saksi. May lain pa bang Dios gawas kanako? Wala gayod! Wala na akoy nahibaloan pa nga dakong bato nga salipdanan.44:8 salipdanan: sa literal, bato.9Walay pulos ang tanang naghimog mga dios-dios. Ug kining mga dios-dios nga ilang gipakamahal walay bili. Sila mismo makapamatuod nga wala kini bili. Kay dili kini makakita ug walay nahibaloan. Mao gani nga maulawan ang mga nagasimba niini. 10Buang-buang ang tawo nga naghimo ug mga dios-dios nga dili man lang niya mapuslan. 11Pamati! Maulawan ang tanang nagasimba sa mga dios-dios, kay ang naghimo niini mga tawo lang usab. Tigoma silang tanan aron sa pagpanalipod sa ilang kaugalingon, kay malisang sila kanako ug maulawan.

12Ang panday sa puthaw mobutang ug puthaw sa baga. Masohon niya kini ug kusog aron pormahon nga dios-dios. Maluya siya sa kagutom ug malipong sa kauhaw. 13Ang panday sa kahoy mosukod ug usa ka putol sa kahoy. Markahan niya kini ug pormahong tawo pinaagi sa iyang mga gamit. Unya kuliton niya kini sa matahom nga dagway sa tawo aron ibutang sa usa ka templo. 14Aron may gamiton siyang kahoy, magputol siyag sedro, o sipres, o terebinto nga iyang gipatubo sa kakahoyan. Magtanom usab siyag kahoyng pino, ug pinaagi sa ulan motubo kini. 15Gamiton niyang sugnod ang ubang mga kahoy, aron makapainit siya ug makaluto ug pan. Ug ang uban himuon niyang dios-dios, ug unya ludhan niya kini ug simbahon. 16Ihaling niya ang ubang mga kahoy ug magsugba siyag karne diha sa baga niini. Unya mokaon siya sa sinugba ug mabusog. Magpainit-init usab siya sa kalayo ug moingon, “Maayo kay nainitan ako.” 17Ug ang ubang kahoy, himuon niyang dios-dios. Moluhod siya ug mosimba niining mga dios-dios, ug mag-ampo nga nagaingon, “Luwasa ako, kay ikaw ang akong dios.”

18Kining mga tawhana wala masayod o makasabot sa ilang gihimo. Ang ilang mga mata nataptapan, mao nga dili sila makakita. Ang ilang mga hunahuna natak-opan, busa dili sila makasabot. 19Wala gayod kanilay makapamalandong ug makahunahuna aron sa pag-ingon, “Gisugnod ko ang ubang kahoy ug nagluto akog pan. Nagsugba akog karne diha sa baga niini, ug mikaon ako. Ug karon himuon ko bang usa ka ngil-ad nga butang ang nahibiling kahoy? Mosimba ba ako sa usa ka putol sa kahoy?”

20Sama lang siya sa nagkaon ug abo. Ang nalimbongan niyang hunahuna nagpahisalaag kaniya. Ug dili niya maluwas ang iyang kaugalingon, ni makaamgo ug makapangutana sa iyang kaugalingon. Dili niya madawat nga ang dios-dios sa iyang mga kamot dili tinuod nga dios.

21Miingon ang Ginoo, “Hinumdomi kining mga butanga, O Israel, kay ikaw akong alagad. Gihimo ko ikaw, aron moalagad kanako, ug dili ko gayod ikaw kalimtan. 22Wad-on ko na ang imong mga sala sama sa dag-om o gabon. Balik kanako, O Israel, kay luwason ko gayod ikaw.”

23Pag-awit sa kalipay, O kalangitan! Singgit ug kusog, O kalibotan! Pag-awit kamong mga bukid ug mga kakahoyan, kay giluwas na sa Ginoo ang mga kaliwat ni Jacob; gipakita niya ang iyang pagkagamhanan sa Israel.

24Mao kini ang giingon sa Ginoo nga inyong Manluluwas, nga nagbuhat kaninyo: Ako ang Ginoo nga naghimo sa tanang butang. Ako lang gayod ang nagbukhad sa kalangitan, ug nagmugna sa kalibotan. 25Gisanta ko ang mga tagna sa bakakong mga propeta. Ug gihimo kong mga buang-buang ang mga manalagna. Gituis ko ang kahibalo sa mga maalamon, ug gihimong kawang ang ilang kahibalo. 26Gituman ko ang mga panagna sa akong alagad44:26 alagad: o, mga alagad. ug mga mensahero. Miingon ako nga ang Jerusalem pagapuy-an pag-usab, ug ang uban pang mga lungsod sa Juda tukoron pag-usab. 27Kon momando ako nga momala ang mga suba, momala kini. 28Moingon ako kang Cyrus, “Ikaw ang magbalantay sa akong katawhan, ug himuon mo ang tanan kong gusto. Magmando siya nga tukoron pag-usab ang Jerusalem ug ang templo niini.”