Yesaya 43 – CCL & APSD-CEB

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yesaya 43:1-28

Yehova Yekha Mpulumutsi wa Israeli

1Koma tsopano, Yehova

amene anakulenga, iwe Yakobo,

amene anakuwumba, iwe Israeli akuti,

“Usaope, pakuti ndakuwombola;

Ndinakuyitanitsa mokutchula dzina lako, ndiwe wanga.

2Pamene ukuwoloka nyanja,

ndidzakhala nawe;

ndipo pamene ukuwoloka mitsinje,

sidzakukokolola.

Pamene ukudutsa pa moto,

sudzapsa;

lawi la moto silidzakutentha.

3Chifukwa Ine Yehova, Mulungu wako,

Woyera wa Israeli, ndine Mpulumutsi wako.

Ndinapereka Igupto pofuna kuti ndiwombole iwe,

ndinapereka Kusi ndi Seba mʼmalo mwa iwe.

4Popeza kuti ndiwe wamtengowapatali wolemekezeka ndi wapamtima panga,

ndipo chifukwa ndimakukonda,

ndidzapereka anthu mʼmalo mwa iwe,

ndidzapereka mitundu ya anthu pofuna kuwombola moyo wako.

5Usachite mantha, pakuti Ine ndili nawe;

ndidzabweretsa ana ako kuchokera kummawa,

ndipo ndidzakusonkhanitsani kuchokera kumadzulo.

6Ndidzawuza a kumpoto kuti, ‘Amasuleni,’

ndidzawuza akummwera kuti, ‘Musawagwire.’

Bweretsani ana anga aamuna kuchokera ku mayiko akutali,

ana anga a akazi kuchokera kumalekezero a dziko lapansi;

7onsewo amadziwika ndi dzina langa;

ndinawalenga chifukwa cha ulemerero wanga,

ndinawawumba, inde ndinawapanga.”

8Tulutsa anthu amene ali nawo maso koma sakupenya,

anthu amene ali nawo makutu koma sakumva.

9Mitundu yonse ya anthu isonkhane pamodzi,

anthu a mitundu ina akhale pamodzi pabwalo la milandu.

Ndani wa iwo amene ananeneratu zimenezi?

Ndani wa iwo anatifotokozerapo zinthu zakalekale?

Abweretu ndi mboni zawo kuti adzatsimikizire kuti ananena zoona,

kuti anthu ena amve ndi kunena kuti, “Ndi zoona.”

10Yehova akunena kuti, “Inu Aisraeli ndinu mboni zanga,

ndi mtumiki wanga amene ndinakusankha,

kuti mundidziwe ndi kundikhulupirira, ndipo mudzamvetsa kuti Mulungu ndine ndekha.

Patsogolo panga sipanapangidwepo mulungu wina,

ngakhale pambuyo panga

sipadzakhalaponso wina.”

11Akutero Yehova, “Ine, Inetu ndine Yehova,

ndipo palibe Mpulumutsi wina koma Ine ndekha.

12Ndine amene ndinaneneratu, amene ndinakupulumutsa;

ndine, osati mulungu wina wachilendo pakati panu amene ndinalengezeratu.

Inu ndinu mboni zanga, kuti Ine ndine Mulungu,” akutero Yehova.

13“Ine ndine Mulungu kuyambira nthawi yamakedzana, ndipo ndidzakhalabe Mulungu ku nthawi zonse.

Palibe amene angathe kuthawa mʼmanja mwanga,

ndipo chimene ndachita palibe angathe kuchisintha.”

Chifundo cha Mulungu ndi Kusakhulupirika kwa Israeli

14Yehova akuti,

Mpulumutsi wanu, Woyerayo wa Israeli akuti,

“Chifukwa cha inu ndidzatuma gulu lankhondo kukalimbana ndi Babuloni

ndi kukupulumutsani.

Ndidzagwetsa zitseko zonse za mzindawo, ndipo kukondwa kwa anthu ake kudzasanduka kulira.

15Ine ndine Yehova, Woyera wanu uja,

Mlengi wa Israeli. Ine ndine Mfumu yanu.”

16Yehova

anapanga njira pa nyanja,

anapanga njira pakati pa madzi amphamvu.

17Iye anasonkhanitsa magaleta, akavalo,

gulu lankhondo ndi asilikali amphamvu,

ndipo onse anagwa pamenepo, osadzukanso

anazimitsidwa kutheratu ngati chingwe cha nyale. Yehova ameneyu akuti,

18“Iwalani zinthu zakale;

ndipo musaganizirenso zinthu zimene zinachitika kale.

19Taonani, Ine ndikuchita zinthu zatsopano!

Tsopano zayamba kale kuoneka; kodi simukuziona?

Ine ndikulambula msewu mʼchipululu

ndi kupanga mitsinje mʼdziko lowuma.

20Nyama zakuthengo, nkhandwe ndi akadzidzi

zinandilemekeza.

Ndidzayendetsa mitsinje mʼdziko lowuma

kuti ndiwapatse madzi anthu anga

osankhidwa.

21Anthu amene ndinadziwumbira ndekha

kuti aziyimba nyimbo yotamanda Ine.

22“Komatu simunapemphera kwa Ine, Inu a mʼbanja la Yakobo,

munatopa nane, Inu Aisraeli.

23Simunabweretse kwa Ine nkhosa za nsembe zopsereza,

kapena kundilemekeza ndi nsembe zanu.

Ine sindinakulemetseni pomakupemphani zopereka za chakudya

kapena kukutopetsani pomakupemphani nsembe zofukiza.

24Simunandigulire bango lonunkhira

kapena kundipatsa Ine mafuta okwanira a nsembe zanu.

Koma inu mwandilemetsa Ine ndi machimo anu

ndipo mwanditopetsa Ine ndi zolakwa zanu.

25“Ine, Inetu, ndi amene ndimafafaniza

zolakwa zanu, chifukwa cha Ine mwini,

ndipo sindidzakumbukiranso machimo anu.

26Mundikumbutse zakale,

ndipo titsutsane nkhaniyi pamodzi;

fotokozani mlandu wanu kuti muonetse kuti ndinu osalakwa.

27Kholo lanu loyamba linachimwa;

ndipo Atsogoleri anu achipembedzo anandiwukira.

28Chifukwa chake Ine ndidzanyazitsa akuluakulu a Nyumba yanu ya mapemphero,

ndipo ndidzapereka Yakobo kuti awonongedwe

ndi Israeli kuti achitidwe chipongwe.”

Ang Pulong Sa Dios

Isaias 43:1-28

Nagsaad ang Dios sa Pagluwas sa Israel

1Apan karon mao kini ang giingon sa Ginoo nga nagbuhat kanimo, O Israel, “Ayaw kahadlok kay luwason ko gayod ikaw.43:1 luwason ko gayod ikaw: o, ikaw giluwas ko na. Gitawag ko ikaw sa imong ngalan, ug akoa ka. 2Kon moagi ka sa tubig, mouban ako kanimo. Kon motabok ka sa mga suba dili ka malumos. Kon moagi ka sa kalayo, dili ka mapaso; ang dilaab niini dili makalamoy kanimo. 3Kay ako ang Ginoo nga imong Dios, ang Balaang Dios sa Israel, nga imong Manluluwas. Itugyan ko sa ubang nasod ang Ehipto, Etiopia,43:3 Etiopia: sa Hebreo, Cush. ug Seba puli kanimo. 4Itugyan ko ang ubang katawhan puli kanimo, tungod kay bililhon ug dungganon ka alang kanako, ug tungod kay gihigugma ko ikaw. 5Ayaw kahadlok kay kauban mo ako. Tigomon ko ang imong mga kaliwat gikan sa sidlakan ug kasadpan. 6Ingnan ko ang mga nasod sa amihan ug habagatan nga pasagdan ang imong mga kaliwat nga mobalik sa ilang yuta, nga papaulion sila gikan sa layong mga dapit. 7Sila ang mga katawhan nga akong gitawag; gibuhat ko sila alang sa akong kadungganan.”

8Miingon usab ang Ginoo, “Tawga ang akong katawhan nga may mga mata apan dili makakita, may mga dalunggan apan dili makadungog! 9Papundoka ang tanang katawhan sa nasod. Kinsa sa ilang mga dios-dios ang makatagna sa umaabot? Kinsa kanila ang nagpadayag kaniadto sa mga panghitabo karon? Padad-a silag mga saksi sa pagpamatuod nga husto sila aron makadungog niini ang uban ug moingon nga tinuod gayod. 10Mga katawhan sa Israel, kamo akong mga saksi. Gipili ko kamo nga akong alagad aron makaila kamo ug motuo kanako, ug masabtan ninyo nga ako lang ang Dios. Wala gayoy laing Dios nga una kanako o mosunod pa kanako. 11Ako lang gayod ang Ginoo. Gawas kanako, wala nay lain pa nga Manluluwas. 12Nagpahibalo ako nga luwason ko kamo, ug gituman ko kini. Walay lain nga dios nga naghimo niini kaninyo; kamo ang akong mga saksi.”

Miingon pa ang Ginoo, “Ako mao ang Dios. 13Sukad pa kaniadto ako na ang Dios. Walay makalingkawas sa akong mga kamot. Walay makausab sa akong mga binuhatan.”

Nagsaad ang Dios nga Tabangan Niya ang Iyang Katawhan

14Mao kini ang giingon sa Ginoo, ang inyong Manluluwas, ang Balaan nga Dios sa Israel, “Aron maluwas kamo, ipasulong ko ang Babilonia sa mga sundalo sa usa ka nasod, ug mangikyas ang mga taga-Babilonia43:14 taga-Babilonia: sa literal, Kaldeanhon. Mao kini ang laing tawag sa mga taga-Babilonia. ngadto sa mga barko nga ilang gipasigarbo. 15Ako mao ang Ginoo, ang inyong Balaang Dios, ang magbubuhat sa Israel, ang inyong Hari. 16Ako ang Ginoo nga naghimo ug agianan taliwala sa dagat. 17Gitigom ko ang mga karwahe, mga kabayo, ug mga sundalo sa Ehipto, ug gilaglag sila didto sa dagat, ug dili na gayod sila makabangon pa. Sama sila sa suga nga napalong. 18Apan ayaw na ninyo sigehag hunahuna ang nangagi, 19kay maghimo akog bag-ong butang. Nagakahitabo na gani kini. Wala ba ninyo nakita? Maghimo akog dalan ug mga tuboran diha sa disyerto. 20Bisan ang ihalas nga mga mananap magapasidungog kanako, apil ang ihalas nga mga iro43:20 ihalas nga mga iro: sa English, jackals. ug ang mga kuwago, kay magahatag akog mga tuboran diha sa disyerto, aron may mainom ang akong piniling katawhan. 21Sila ang katawhan nga akong gibuhat aron mahimong ako, ug aron modayeg kanako.

22“Apan wala ka mangayo ug tabang gikan kanako, Israel, kondili, gipul-an ka na hinuon kanako! 23Wala ka mohalad kanakog mga karnero ingon nga halad nga sinunog. Wala mo ako pasidunggi sa imong mga halad nga wala ko man unta ikaw lisod-lisora ug hasola pinaagi sa pagpangayo kanimog mga halad sa pagpasidungog ug mga insenso. 24Wala mo gayod ako palitig insenso, ni tagbawa sa tambok sa imong mga halad. Apan gipabug-atan mo hinuon ako ug gisamok sa imong mga sala.

25“Ako mismo mao ang nagpala sa imong sala alang sa akong kadungganan, ug dili ko na kini hinumdoman pa. 26Hisgotan ta pagbalik ang mga nanglabay; maghusay kita. Ipahayag ang imong katarungan sa pagpamatuod nga ikaw inosente. 27Nakasala ang imong unang katigulangan, ug misupak kanako ang imong mga pangulo. 28Busa gipakaulawan ko ang imong mga pari ug gitugyan ko ikaw, Israel, ngadto sa kalaglagan ug kaulawan.