Yesaya 38 – CCL & KLB

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yesaya 38:1-22

Kudwala kwa Hezekiya

1Nthawi imeneyo Mfumu Hezekiya anadwala ndipo anali pafupi kufa. Mneneri Yesaya mwana wa Amozi anapita kukamuona ndipo anati “Yehova akuti: Konza bwino nyumba yako, pakuti ukufa; suchira.”

2Hezekiya anatembenuka nayangʼana kukhoma, napemphera kwa Yehova kuti, 3“Inu Yehova, kumbukirani momwe ndayendera pamaso panu mokhulupirika ndi modzipereka ndipo ndakhala ndikuchita zabwino pamaso panu.” Ndipo Hezekiya analira mosweka mtima.

4Ndipo Yehova analamula Yesaya kuti: 5“Pita kwa Hezekiya ndipo ukamuwuze kuti, ‘Yehova, Mulungu wa kholo lake Davide akuti: Ndamva pemphero lako ndipo misozi yako ndayiona; ndidzakuwonjezera zaka 15 pa moyo wako. 6Ndipo ndidzakupulumutsa, iwe pamodzi ndi mzindawu mʼdzanja la mfumu ya ku Asiriya, Ine ndidzawuteteza mzindawu.

7“ ‘Ichi ndi chizindikiro cha Yehova kwa iwe kutsimikiza kuti Yehova adzachita zimene walonjeza: 8Chithunzithunzi chimene dzuwa likuchititsa pa makwerero a Ahazi ndidzachibweza mʼmbuyo makwerero khumi.’ ” Ndipo chithunzithunzi chinabwerera mʼmbuyo makwerero khumi.

9Ndakatulo ya Hezekiya mfumu ya ku Yuda imene analemba atadwala ndi kuchira:

10Ine ndinaganiza kuti

ndidzapita ku dziko la akufa

pamene moyo ukukoma.

11Ndinaganiza kuti, “Sindidzaonanso Yehova,

mʼdziko la anthu amoyo,

sindidzaonanso mtundu wa anthu

kapena kukhala pamodzi ndi amene amakhala pa dziko lapansi lino.

12Nyumba yanga yasasuka

ndipo yachotsedwa.

Ngati tenti ya mʼbusa mwapindapinda moyo wanga,

ngati munthu wowomba nsalu;

kuyambira usana mpaka usiku mwakhala mukundisiya.

13Ndinkalira kupempha chithandizo usiku wonse mpaka mmawa;

koma Inu Yehova munaphwanya mafupa anga ngati mkango,

ndipo mwakhala mukundisiya.

14Ndinkalira ngati namzeze kapena chumba,

ndinkabuwula ngati nkhunda yodandaula.

Maso anga anatopa nʼkuyangʼana mlengalenga.

Inu Ambuye, ine ndili mʼmavuto bwerani mudzandithandize!”

15Koma ine ndinganene chiyani?

Yehova wayankhula nane, ndipo Iye ndiye wachita zimenezi.

Chifukwa cha kuwawa kwa mtima wanga,

ine ndidzayenda modzichepetsa masiku amoyo wanga onse.

16Ambuye, masiku anga ali mʼmanja mwanu.

Mzimu wanga upeza moyo mwa Inu.

Munandichiritsa ndi

kundikhalitsa ndi moyo.

17Ndithudi, ine ndinamva zowawa zotere

kuti ndikhale ndi moyo;

Inu munandisunga

kuti ndisapite ku dzenje la chiwonongeko

chifukwa mwakhululukira

machimo anga onse.

18Pakuti akumanda sangathe kukutamandani,

akufa sangayimbe nyimbo yokutamandani.

Iwo amene akutsikira ku dzenje

sangakukhulupirireni.

19Amoyo, amoyo okha ndiwo amakutamandani,

monga mmene ndikuchitira ine lero lino;

abambo amawuza ana awo za

kukhulupirika kwanu.

20Yehova watipulumutsa.

Tiyeni tiyimbe ndi zoyimbira za zingwe

masiku onse a moyo wathu

mʼNyumba ya Yehova.

21Yesaya anati, “Anthu atenge mʼbulu wankhunyu ndipo apake pa chithupsacho ndipo Hezekiya adzachira.”

22Hezekiya nʼkuti atafunsa kuti, “Kodi chizindikiro chako nʼchiyani chotsimikiza kuti ndidzapita ku Nyumba ya Yehova?”

Korean Living Bible

이사야 38:1-22

히스기야왕의 병과 회복

1이때 히스기야왕이 병들어 죽게 되었다. 그래서 아모스의 아들 예언자 이사야가 그에게 가서 이렇게 말하였다. “여호와께서는 왕이 회복되지 못할 것이므로 모든 것을 정리하고 죽을 준비를 하라고 말씀하셨습니다.”

2그러자 히스기야는 얼굴을 벽 쪽으로 돌리고

3“여호와여, 내가 마음을 다하여 주를 성실하게 섬긴 일과 내가 주 앞에서 선하게 살려고 했던 것을 기억하소서” 하고 기도하며 크게 통곡하였다.

4그때 여호와께서 이사야에게 말씀하셨다.

5“너는 히스기야에게 가서 그의 조상 다윗의 하나님 나 여호와가 이렇게 말한다고 일러 주어라. ‘나는 네 기도를 들었고 네 눈물을 보았다. 내가 네 수명을 15년 더 연장하고

6너와 이 성을 앗시리아 왕에게서 구출하여 계속 보호하겠다.

7나 여호와가 말한 것이 사실임을 증명할 표적은 이것이다.

8내가 아하스왕의 일영표에 해 그림자가 10도 뒤로 물러가게 하겠다.’ ” 그리하여 그 일영표의 해 그림자가 10도 뒤로 물러갔다.

9히스기야왕은 병에서 회복된 후에 이런 시를 지었다:

10나는 생의 전성기에

죽음의 문턱을 넘어

수명대로 살지 못할 것으로 생각하였다.

11나는 또 이 세상에서

다시는 여호와를 뵙지 못하고

이 세상에 살아 있는 사람도

다시 보지 못할 것으로 알았다.

12목자의 천막을 걷듯이

내 육체의 생명이 내게서 떠나고

직조공이 베틀에서

베를 잘라 말듯이

내가 내 생명을 말았으니

내 명이 조만간에

곧 끝나 버릴 것 같았다.

13마치 사자가 내 뼈를 꺾는 것처럼

내가 밤새도록 신음하고

괴로워하였으니

정말 내 생명이 곧 끝나 버릴 것 같았다.

14내가 제비나 학처럼 지껄이고

비둘기처럼 슬피 울며

하늘을 바라보다가 지쳐

“여호와여, 내가 죽게 되었습니다.

나를 구해 주소서” 하고 외쳤다.

15여호와께서 나에게 말씀하시고

이 일을 행하셨으니

내가 무슨 말을 할 수 있겠는가?

내가 이 고통을 생각하며

여생을 겸손한 마음으로

살아가리라.

16여호와여, 이와 같은 주의 훈계로

사람이 살게 되니

내 영혼의 생명도 여기에 있습니다.

주여, 나를 고치시고 살려 주소서.

17내가 이런 고통을 당한 것은

나에게 유익이었습니다.

주는 내 영혼을 사랑하셔서

나를 죽음에서 건지시고

나의 모든 죄를 용서하셨습니다.

18죽은 사람이 주를 찬양할 수 없고

무덤에 들어간 자가

주의 신실하심을 바랄 수 없습니다.

19아버지가 자기 자녀들에게

주의 신실하심을 말해 주듯이

오늘 나처럼

주를 찬양할 수 있는 사람은

오직 살아 있는 사람뿐입니다.

20여호와께서 나를 구원하실 것이니

우리가 평생 여호와의 성전에서

수금으로 노래하며 찬양하리라.

2138:21 어떤 번역본에는 21-22절을 6절과 7절 사이에 삽입시켰다.이사야가 히스기야에게 으깬 무화과 뭉치를 상처에 바르면 나을 것이라고 말했을 때

22히스기야는 여호와께서 자기를 고쳐 주실 표적이 무엇이냐고 물었던 것이다.