Yesaya 36 – CCL & NRT

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yesaya 36:1-22

Senakeribu Awopseza Yerusalemu

1Chaka cha khumi ndi chinayi cha ulamuliro wa Mfumu Hezekiya, Senakeribu mfumu ya ku Asiriya anathira nkhondo mizinda yonse yotetezedwa ya ku Yuda, nayilanda. 2Kenaka mfumu ya ku Asiriya inatuma kazembe wake wankhondo pamodzi ndi gulu lalikulu lankhondo kuchokera ku Lakisi kupita kwa mfumu Hezekiya ku Yerusalemu. Tsono kazembeyo anayima pafupi ndi ngalande yamadzi yochokera ku Dziwe lakumtunda pa msewu wopita ku malo a munda wa mmisiri wochapa zovala. 3Panali anthu atatu. Woyamba anali Eliyakimu mwana wa Hilikiya komanso ndiye woyangʼanira nyumba ya mfumu. Wachiwiri anali Sebina amene anali mlembi wa bwalo; ndipo wachitatu anali Yowa mwana wa Asafu komanso anali wolemba zochitika. Anthu awa anatuluka kukakumana ndi kazembe wa ankhondo uja.

4Kazembe wa ankhondo anawawuza kuti, “Kamuwuzeni Hezekiya kuti,

“Mfumu yayikulu, mfumu ya ku Asiriya ikunena kuti, Kodi chikukulimbitsa mtima ndi chiyani? 5Iwe ukuti uli ndi luso ndiponso mphamvu pa nkhondo, komatu ukuyankhula mawu opanda pake. Kodi tsono iwe ukudalira yani kuti undiwukire ine? 6Taona tsono, iwe ukudalira Igupto, bango lothyokalo, limene limalasa mʼmanja mwa munthu ngati waliyesa ndodo yoyendera! Umo ndi mmene Farao mfumu ya ku Igupto imachitira aliyense amene akuyidalira. 7Ndipo ngati ukunena kwa ine kuti, ‘Ife tikudalira Yehova Mulungu wathu,’ kodi si Mulungu yemweyo amene nyumba zake ndi maguwa ake, Hezekiya anachotsa, nawuza anthu a ku Yuda ndi a ku Yerusalemu kuti, ‘Muzipembedza pa guwa lansembe ili?’

8“Ndipo tsopano bwera udzakambirane ndi mbuye wanga, mfumu ya ku Asiriya: Ine ndidzakupatsa akavalo 2,000 ngati ungathe kupeza okwerapo! 9Iwe ungathe bwanji kugonjetsa ngakhale mmodzi mwa akazembe angʼonoangʼono a mbuye wanga, pamene ukudalira Igupto kuti akupatse magaleta ndi anthu okwera pa akavalo. 10Kuwonjezera pamenepa, kodi ine ndabwera kudzathira nkhondo ndi kuwononga dziko lino popanda chilolezo cha Yehova? Yehova mwini ndiye anandiwuza kuti ndidzathire nkhondo ndi kuwononga dziko lino.”

11Pamenepo Eliyakimu, Sebina ndi Yowa anawuza kazembeyo kuti, “Chonde yankhulani kwa atumiki anufe mʼChiaramu, popeza timachimva. Musayankhule nafe mu Chihebri kuopa kuti anthu onse amene ali pa khomapa angamve.”

12Koma kazembeyo anayankha kuti, “Kodi mbuye wanga wandituma kuti ndidzanene zinthu izi kwa mbuye wanu yekha ndi inu nokha basi? Ayi, komanso kwa anthu amene akhala pa khomawa. Iwowa adzadya chimbudzi chawo chomwe ndi kumwa mkodzo wawo womwe monga momwe mudzachitire inuyonso.”

13Tsono kazembeyo anayimirira nafuwula mu Chihebri kuti, “Imvani mawu a mfumu yayikulu, mfumu ya ku Asiriya! 14Zimene mfumu ikunena ndi izi: Musalole kuti Hezekiya akunamizeni. Iye sangakupulumutseni! 15Hezekiya asakukakamizeni kudalira Yehova ndi mawu akuti, ‘Ndithu, Yehova adzatipulumutsa; ndipo sadzapereka mzindawu mʼdzanja la mfumu ya ku Asiriya.’

16“Musamumvere Hezekiya. Zimene mfumu ya ku Asiriya ikunena ndi izi: Pangani mtendere ndi ine ndipo mutuluke mu mzinda. Mukatero aliyense wa inu adzadya mphesa ndi nkhuyu za mʼmunda mwake ndiponso adzamwa madzi a mʼchitsime chake, 17mpaka mfumuyo itabwera kudzakutengani kupita ku dziko lofanana ndi lanulo, dziko limene lili ndi tirigu ndi vinyo watsopano, dziko loyenda mkaka ndi uchi.

18“Inu musalole kuti Hezekiya akusocheretseni pamene iye akuti, ‘Yehova adzatipulumutsa.’ Kodi alipo mulungu wa anthu a mtundu wina amene anapulumutsa dziko lake mʼdzanja la mfumu ya ku Asiriya? 19Kodi ili kuti milungu ya Hamati ndi Aripadi? Ili kuti milungu ya Sefaravaimu? Kodi inapulumutsa Samariya mʼdzanja langa? 20Kodi ndi milungu iti mwa milungu yonse ya mayiko awa amene anapulumutsa dziko lake mʼdzanja? Nanga tsono Yehova adzapulumutsa Yerusalemu mʼdzanja langa motani?”

21Koma anthu anakhala chete ndipo sanayankhepo kanthu, chifukwa mfumu inawalamula kuti, “Musayankhe.”

22Pamenepo anthu atatu aja Eliyakimu, mwana wa Hilikiya amene ankayangʼanira nyumba ya mfumu; Sebina mlembi wa bwalo; ndi Yowa, mwana wa Asafu mlembi wa zochitika anapita kwa Hezekiya atangʼamba zovala zawo ndipo anamuwuza zonse zimene anayankhula kazembe uja.

New Russian Translation

Исаия 36:1-22

Синаххериб угрожает Иерусалиму

(4 Цар. 18:13-37; 2 Пар. 32:1-19)

1На четырнадцатом году правления царя Езекии36:1 в 701 г. до н. э. Синаххериб36:1 Синаххериб был сыном и преемником Саргона II. Он правил с 705 по 681 гг. до н. э., царь Ассирии, напал на все укрепленные города Иудеи и захватил их. 2Затем царь Ассирии послал из Лахиша36:2 Лахиш – город, расположенный в юго-западной части удела, принадлежавшего роду Иуды, был важным пунктом в войне Езекии с Синаххерибом, поскольку охранял дорогу, которая вела на юг Иудеи (ср. Иер. 34:7). к царю Езекии в Иерусалим главный виночерпий36:2 Главный виночерпий был одним из самых важных лиц при дворе, которому царь доверял свою жизнь. с большим войском. Когда полководец остановился у водопровода Верхнего пруда на дороге к Сукновальному полю, 3к нему вышли распорядитель дворца Элиаким, сын Хелкии, писарь Шевна и летописец Иоах, сын Асафа.

4Главный виночерпий сказал им:

– Скажите Езекии: «Так говорит великий царь, царь Ассирии: „Откуда у тебя эта уверенность? 5Ты думаешь, что пустые слова – то же самое, что военное искусство и сила? На кого же ты надеешься, что восстал против меня? 6Вот, ты надеешься на Египет, эту надломленную трость, которая пронзит ладонь всякому, кто на нее обопрется! Фараон, царь Египта, таков со всеми, кто на него надеется. 7А если ты скажешь мне: «Мы надеемся на Господа, нашего Бога», то не Его ли святилища на возвышенностях и жертвенники убрал Езекия36:7 Благочестивый Езекия истребил множество святилищ Господу по всей Иудее, которые были за пределами Иерусалима (см. 4 Цар. 18:4; 2 Пар. 31:1), что, без сомнения, не могло не вызвать злобы и ненависти к царю многих ее жителей., сказав Иудее и Иерусалиму: «Поклоняйтесь только перед этим жертвенником»?“

8Итак, заключи сделку с господином моим, царем Ассирии: я дам тебе две тысячи коней, только найдешь ли ты для них всадников? 9Как ты сможешь отразить хотя бы наименьшего начальника из слуг господина моего, даже надеясь на египетские колесницы и всадников?36:9 Или: «колесничих». 10Да и разве не по воле Господа я двинулся на эту страну, чтобы уничтожить ее? Господь Сам сказал мне пойти на эту страну и уничтожить ее».

11Тогда Элиаким, Шевна и Иоах сказали главному виночерпию:

– Пожалуйста, говори с твоими слугами по-арамейски, ведь мы понимаем этот язык. Не говори с нами по-еврейски36:11 Букв.: «по-иудейски». при народе, что на стене.

12Но главный виночерпий ответил:

– Разве мой господин послал меня сказать это только вашему господину и вам, а не людям, находящимся на стене, которые, как и вы сами, будут есть свой кал и пить свою мочу?

13Главный виночерпий встал и громко закричал по-еврейски:

– Слушайте слово великого царя, царя Ассирии! 14Так говорит царь: «Не давайте Езекии обманывать вас. Он не может избавить вас. 15Не давайте Езекии убедить вас положиться на Господа, когда он говорит: „Господь непременно спасет нас; этот город не будет отдан в руки царя Ассирии“. 16Не слушайте Езекию».

Так говорит царь Ассирии: «Заключите со мной мир и выходите ко мне. Тогда все вы будете есть со своей лозы и инжирных деревьев и пить воду из своего колодца, 17пока я не приду и не возьму вас в страну, такую же, как ваша, в страну зерна и вина, страну хлеба и виноградников.

18Не давайте Езекии сбить себя с толку, говоря: „Господь спасет нас“. Разве какой-либо бог другого народа избавил свою страну от руки царя Ассирии? 19Где боги Хамата и Арпада? Где боги Сепарваима? Разве кто-нибудь избавил от моей руки Самарию? 20Кто из богов всех этих стран смог избавить от меня свою страну? Как же Господь сможет избавить от моей руки Иерусалим?»

21Но народ молчал и не говорил в ответ ничего, потому что царь приказал: «Не отвечайте ему». 22И распорядитель дворца Элиаким, сын Хелкии, писарь Шевна и летописец Иоах, сын Асафа, пришли к Езекии в разорванных одеждах и передали ему то, что сказал главный виночерпий.