Ufumu Wachilungamo
1Taonani, kudzakhala mfumu ina imene idzalamulira mwachilungamo,
ndipo akalonga ake adzaweruza molungama.
2Munthu aliyense adzakhala ngati pothawirapo mphepo
ndi malo obisalirapo namondwe,
adzakhala ngati mitsinje ya mʼchipululu,
ngati mthunzi wa thanthwe lalikulu la mʼdziko lowuma.
3Ndipo maso a anthu openya sadzakhalanso otseka,
ndipo makutu a anthu akumva adzamvetsetsa.
4Anthu a mtima wopupuluma adzadziwa ndi kuchita zinthu mofatsa,
ndipo anthu ovutika kuyankhula adzayankhula mosadodoma ndi momveka.
5Chitsiru sichidzatchedwanso munthu waulemu wake
ndipo munthu woyipa sadzalemekezedwa.
6Pakuti munthu opusa amayankhula zauchitsiru,
amaganiza kuchita zoyipa:
Iye amachita zoyipira Mulungu,
ndipo amafalitsa zolakwika zokhudza Yehova;
anjala sawapatsa chakudya
ndipo aludzu sawapatsa madzi.
7Munthu woyipa njira zake ndi zoyipanso,
iye kwake nʼkulingalira zinthu zoyipa.
Amalingalira zakuti awononge anthu aumphawi ndi mabodza ake
ngakhale kuti waumphawiyo akuyankhula zoona.
8Koma munthu wolemekezeka amalingaliranso kuchita zinthu zabwino,
Iye amakhazikika pa zinthu zabwinozo.
Akazi a ku Yerusalemu
9Khalani maso, inu akazi
amene mukungokhala wopanda kulingalira kuti kunja kulinji
ndipo imvani mawu anga.
Inu akazi odzitama, imvani zimene ndikunena!
10Pakapita chaka ndi masiku pangʼono
inu akazi amatama mudzanjenjemera;
chifukwa mitengo ya mphesa idzakanika
ndipo zipatso sizidzaoneka.
11Nthunthumirani inu okhala mosatekesekanu;
ndipo njenjemerani, inu akazi omadzikhulupirira nokhanu.
Vulani zovala zanu,
ndipo valani ziguduli mʼchiwuno mwanu.
12Dzigugudeni pachifuwa mwachisoni chifukwa minda yachonde,
ndi mphesa yawonongeka.
13Mʼdziko la anthu anga
mwamera minga ndi mkandankhuku.
Zoona, mulilire nyumba zonse zachikondwerero
ndi mzinda uno umene unali wachisangalalo.
14Nyumba yaufumu idzasiyidwa,
mzinda waphokoso udzakhala wopanda anthu;
malinga ndi nsanja zidzasanduka chipululu mpaka muyaya.
Abulu adzasangalalamo ndipo ziweto zidzapezamo msipu.
15Yehova adzatipatsa mzimu wake,
ndipo dziko lachipululu lidzasanduka munda wachonde,
ndipo munda wachonde udzakhala ngati nkhalango.
16Tsono mʼchipululu mudzakhala chiweruzo cholungama
ndipo mʼminda yachonde mudzakhala chilungamo.
17Mtendere udzakhala chipatso chachilungamo;
zotsatira za chilungamo zidzakhala bata ndi kudzidalira mpaka muyaya.
18Anthu anga adzakhala mʼmidzi yamtendere,
mʼnyumba zodalirika,
ndi malo osatekeseka a mpumulo.
19Ngakhale nkhalango idzawonongedwa ndi matalala
ndipo mzinda udzagwetsedwa mpaka pansi,
20inutu mudzakhala odalitsika ndithu.
Mudzadzala mbewu zanu mʼmbali mwa mtsinje uliwonse,
ndipo ngʼombe zanu ndi abulu anu zidzadya paliponse.
The kingdom of righteousness
1See, a king will reign in righteousness
and rulers will rule with justice.
2Each one will be like a shelter from the wind
and a refuge from the storm,
like streams of water in the desert
and the shadow of a great rock in a thirsty land.
3Then the eyes of those who see will no longer be closed,
and the ears of those who hear will listen.
4The fearful heart will know and understand,
and the stammering tongue will be fluent and clear.
5No longer will the fool be called noble
nor the scoundrel be highly respected.
6For fools speak folly,
their hearts are bent on evil:
they practise ungodliness
and spread error concerning the Lord;
the hungry they leave empty
and from the thirsty they withhold water.
7Scoundrels use wicked methods,
they make up evil schemes
to destroy the poor with lies,
even when the plea of the needy is just.
8But the noble make noble plans,
and by noble deeds they stand.
The women of Jerusalem
9You women who are so complacent,
rise up and listen to me;
you daughters who feel secure,
hear what I have to say!
10In little more than a year
you who feel secure will tremble;
the grape harvest will fail,
and the harvest of fruit will not come.
11Tremble, you complacent women;
shudder, you daughters who feel secure!
Strip off your fine clothes
and wrap yourselves in rags.
12Beat your breasts for the pleasant fields,
for the fruitful vines
13and for the land of my people,
a land overgrown with thorns and briers –
yes, mourn for all houses of merriment
and for this city of revelry.
14The fortress will be abandoned,
the noisy city deserted;
citadel and watchtower will become a wasteland for ever,
the delight of donkeys, a pasture for flocks,
15till the Spirit is poured on us from on high,
and the desert becomes a fertile field,
and the fertile field seems like a forest.
16The Lord’s justice will dwell in the desert,
his righteousness live in the fertile field.
17The fruit of that righteousness will be peace;
its effect will be quietness and confidence for ever.
18My people will live in peaceful dwelling-places,
in secure homes,
in undisturbed places of rest.
19Though hail flattens the forest
and the city is levelled completely,
20how blessed you will be,
sowing your seed by every stream,
and letting your cattle and donkeys range free.