Yesaya 33 – CCL & NIVUK

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yesaya 33:1-24

Msautso ndi Thandizo

1Tsoka kwa iwe, iwe wowonongawe,

amene sunawonongedwepo!

Tsoka kwa iwe, iwe mthirakuwiri,

iwe amene sunanyengedwepo!

Iwe ukadzaleka kuwononga,

udzawonongedwa,

ukadzasiya umʼthirakuwiri, adzakuwononga,

ndipo ukadzaleka kuchita zachinyengo adzakunyenga.

2Inu Yehova, mutikomere mtima ife;

tikulakalaka Inu.

Tsiku ndi tsiku mutitchinjirize ndi mkono wanu,

ndipo mutipulumutse pa nthawi ya masautso.

3Mukatulutsa liwu lanu longa bingu mitundu ya anthu imathawa;

pamene Inu mwadzambatuka mitundu ya anthu imabalalika.

4Zofunkha za ku nkhondo za mitundu ina Aisraeli adzazisonkhanitsa ngati mmene limachitira dzombe.

Iwo adzalumphira zofunkhazo monga mmene limachitira dzombe.

5Yehova wakwezeka kwambiri pakuti amakhala pamwamba pa zonse

adzadzaza Ziyoni ndi chilungamo ndi chipulumutso.

6Iye adzakupatsani mtendere pa nthawi yanu,

adzakupatsani chipulumutso chochuluka, nzeru zambiri ndi chidziwitso chochuluka;

kuopa Yehova ngati madalitso.

7Taonani, anthu awo amphamvu akulira mofuwula mʼmisewu;

akazembe okhazikitsa mtendere akulira kwambiri.

8Mʼmisewu yayikulu mulibe anthu,

mʼmisewu mulibe anthu a paulendo.

Mdaniyo ndi wosasunga pangano.

Iye amanyoza mboni.

Palibe kulemekezana.

9Dziko likulira ndipo likunka likutha.

Nkhalango ya Lebanoni ikuchita manyazi, yafota.

Chigwa cha chonde cha Saroni chasanduka chachidalala.

Masamba a mitengo ya ku Basani ndi Karimeli akuyoyoka.

10Yehova akunena kuti, “Tsopano ndidzadzambatuka

ndipo ndidzaonetsa mphamvu zanga,

ndipo ndidzakwezedwa.

11Zolingalira zanu nʼzachabechabe

ngati udzu wamanyowa.

Mpweya wamoto udzakupserezani.

12Anthu a mitundu ina adzatenthedwa ngati miyala ya njereza;

ndi ngati minga yodulidwa.”

13Inu amene muli kutali, imvani zimene ndachita;

inu amene muli pafupi, dziwani mphamvu zanga

14Mu mzinda wa Ziyoni anthu ochimwa agwidwa ndi mantha;

anthu osapembedza Mulungu akunjenjemera:

Iwo akunena kuti, “Ndani wa ife angathe kukhala mʼmoto wonyeketsa?

Ndani wa ife angathe kukhala moto wosatha?”

15Angathe kuti ndi amene amachita zolungama

ndi kuyankhula zoona,

amene amakana phindu lolipeza monyenga

ndipo salola manja ake kulandira ziphuphu,

amene amatseka makutu ake kuti angamve mawu opangana kupha anzawo

ndipo amatsinzina kuti angaone zoyipa.

16Munthu wotere ndiye adzakhale pa nsanja,

kothawira kwake kudzakhala mʼmalinga a mʼmapiri.

Azidzalandira chakudya chake

ndipo madzi sadzamusowa.

17Nthawi imeneyo maso a ana adzaona mfumu ya maonekedwe wokongola

ndi kuona dziko lotambasukira kutali.

18Mu mtima mwanu muzidzalingalira zoopsa zinachitika kale zija:

“Ali kuti mkulu wa Asilikali uja?

Ali kuti wokhometsa misonkho uja?

Ali kuti mkulu woyangʼanira nsanja?”

19Simudzawaonanso anthu odzikuza aja,

anthu aja achiyankhulo chosadziwika,

chachilendo ndi chosamveka.

20Taonani Ziyoni, mzinda wa zikondwerero zachipembedzo chathu;

maso anu adzaona Yerusalemu,

mzinda wamtendere, tenti imene sidzachotsedwa,

zikhomo zake sizidzazulidwa,

kapena zingwe zake kuduka.

21Kumeneko Yehova adzaonetsa ulemerero wake

ndipo mzindawo udzakhala kasupe wa mitsinje yayikulu.

Ngalawa za zopalasa sizidzapitamo,

sitima zapamadzi zikuluzikulu sizidzayendamo.

22Pakuti Yehova ndi woweruza wathu,

Yehova ndiye wotilamulira,

Yehova ndiye mfumu yathu;

ndipo ndiye amene adzatipulumutse.

23Zingwe za sitima zapamadzi za adani athu zamasuka,

sizikutha kulimbitsa mlongoti wake,

matanga ake sakutheka kutambasuka.

Ngakhale tidzagawana zofunkha zochuluka kwambiri

ndipo ngakhale olumala adzatenga zofunkhazo.

24Palibe ndi mmodzi yemwe wokhala mʼZiyoni adzanene kuti, “Ndikudwala”

ndipo anthu onse okhala mʼmenemo machimo awo adzakhululukidwa.

New International Version – UK

Isaiah 33:1-24

Distress and help

1Woe to you, destroyer,

you who have not been destroyed!

Woe to you, betrayer,

you who have not been betrayed!

When you stop destroying,

you will be destroyed;

when you stop betraying,

you will be betrayed.

2Lord, be gracious to us;

we long for you.

Be our strength every morning,

our salvation in time of distress.

3At the uproar of your army, the peoples flee;

when you rise up, the nations scatter.

4Your plunder, O nations, is harvested as by young locusts;

like a swarm of locusts people pounce on it.

5The Lord is exalted, for he dwells on high;

he will fill Zion with his justice and righteousness.

6He will be the sure foundation for your times,

a rich store of salvation and wisdom and knowledge;

the fear of the Lord is the key to this treasure.33:6 Or is a treasure from him

7Look, their brave men cry aloud in the streets;

the envoys of peace weep bitterly.

8The highways are deserted,

no travellers are on the roads.

The treaty is broken,

its witnesses33:8 Dead Sea Scrolls; Masoretic Text / the cities are despised,

no-one is respected.

9The land dries up and wastes away,

Lebanon is ashamed and withers;

Sharon is like the Arabah,

and Bashan and Carmel drop their leaves.

10‘Now will I arise,’ says the Lord.

‘Now will I be exalted;

now will I be lifted up.

11You conceive chaff,

you give birth to straw;

your breath is a fire that consumes you.

12The peoples will be burned to ashes;

like cut thorn-bushes they will be set ablaze.’

13You who are far away, hear what I have done;

you who are near, acknowledge my power!

14The sinners in Zion are terrified;

trembling grips the godless:

‘Who of us can dwell with the consuming fire?

Who of us can dwell with everlasting burning?’

15Those who walk righteously

and speak what is right,

who reject gain from extortion

and keep their hands from accepting bribes,

who stop their ears against plots of murder

and shut their eyes against contemplating evil –

16they are the ones who will dwell on the heights,

whose refuge will be the mountain fortress.

Their bread will be supplied,

and water will not fail them.

17Your eyes will see the king in his beauty

and view a land that stretches afar.

18In your thoughts you will ponder the former terror:

‘Where is that chief officer?

Where is the one who took the revenue?

Where is the officer in charge of the towers?’

19You will see those arrogant people no more,

people whose speech is obscure,

whose language is strange and incomprehensible.

20Look on Zion, the city of our festivals;

your eyes will see Jerusalem,

a peaceful abode, a tent that will not be moved;

its stakes will never be pulled up,

nor any of its ropes broken.

21There the Lord will be our Mighty One.

It will be like a place of broad rivers and streams.

No galley with oars will ride them,

no mighty ship will sail them.

22For the Lord is our judge,

the Lord is our lawgiver,

the Lord is our king;

it is he who will save us.

23Your rigging hangs loose:

the mast is not held secure,

the sail is not spread.

Then an abundance of spoils will be divided

and even the lame will carry off plunder.

24No-one living in Zion will say, ‘I am ill’;

and the sins of those who dwell there will be forgiven.