Yesaya 3 – CCL & BPH

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yesaya 3:1-26

Chiweruzo pa Yerusalemu ndi Yuda

1Taonani tsopano, Ambuye

Yehova Wamphamvuzonse,

ali pafupi kuchotsa mu Yerusalemu ndi mu Yuda

zinthu pamodzi ndi thandizo;

adzachotsa chakudya chonse ndi madzi onse,

2anthu amphamvu ndi asilikali ankhondo,

oweruza ndi aneneri,

anthu olosera ndi akuluakulu,

3atsogoleri a ankhondo makumi asanu ndi anthu olemekezeka,

aphungu ndi anthu amatsenga ndi akatswiri pa za kulosera.

4Ndidzawayikira anyamata kuti akhale mafumu awo;

ana akhanda ndiwo adzawalamulire.

5Anthu adzazunzana,

munthu ndi munthu mnzake, mnansi ndi mnansi wake.

Anthu wamba adzanyoza

akuluakulu.

6Munthu adzagwira mʼbale wake

mʼnyumba ya abambo awo, ndipo adzati,

“Iwe uli nawo mwinjiro, ndiye ukhale mtsogoleri wathu;

lamulira malo opasuka ano!”

7Koma tsiku limenelo mʼbale wakeyo adzafuwula kuti,

“Ayi, mavuto oterewa ndilibe mankhwala ake.

Ndilibe chakudya kapena chovala mʼnyumba mwanga;

musasankhe ine kukhala mtsogoleri wa anthu.”

8Yerusalemu akudzandira,

Yuda akugwa;

zokamba zawo ndi ntchito zawo nʼzotsutsana ndi Yehova,

sakulabadira ulemerero wa Mulungu.

9Maonekedwe a nkhope zawo amawatsutsa;

amaonetsera poyera tchimo lawo ngati Sodomu;

salibisa tchimo lawolo.

Tsoka kwa iwo

odziputira okha mavuto.

10Nena kwa olungama kuti zonse zidzawayendera bwino,

pakuti adzakondwera ndi phindu la ntchito zawo.

11Tsoka kwa anthu oyipa! Mavuto ali pa iwo!

Adzalandira malipiro a zimene manja awo anachita.

12Achinyamata akupondereza anthu anga,

ndipo amene akuwalamulira ndi akazi.

Aa, anthu anga, atsogoleri anu akukusocheretsani;

akukuchotsani pa njira yanu.

13Yehova wakhala pamalo pake mʼbwalo la milandu;

wakonzeka kuti aweruze anthu ake.

14Yehova akuwazenga milandu

akuluakulu ndi atsogoleri a anthu ake:

“Ndinu amene mwawononga munda wanga wa mpesa;

nyumba zanu zadzaza ndi zolanda kwa amphawi.

15Nʼchifukwa chiyani inu mukupsinja anthu anga,

nʼkudyera masuku pamutu amphawi?”

Akutero Ambuye Yehova Wamphamvuzonse.

16Yehova akunena kuti,

“Akazi a ku Ziyoni ngodzikuza kwambiri,

akuyenda atakweza makosi awo,

akukopa amuna ndi maso awo

akuyenda monyangʼama

akuliza zigwinjiri za mʼmiyendo yawo

17Nʼchifukwa chake Ambuye, adzatulutsa zipere pa mitu ya akazi a ku Ziyoniwo;

Yehova adzachititsa dazi mitu yawo.”

18Tsiku limenelo Ambuye adzawachotsera zodzikongoletsera zawo: za mʼmiyendo, za ku mutu za mʼkhosi, 19ndolo ndi zibangiri, nsalu zophimba pa nkhope, 20maduku, zigwinjiri za mʼmiyendo ndi malamba, mabotolo a zonunkhira ndi zithumwa, 21mphete ndi zipini, 22zovala za pa mphwando, zipewa ndi mwinjiro, zikwama, 23magalasi oyangʼanira, zovala zosalala, nduwira ndiponso nsalu za mʼmapewa.

24Mʼmalo mwa kununkhira azidzanunkha,

mʼmalo mwa lamba, adzavala chingwe;

mʼmalo mwa tsitsi lopesa bwino, adzakhala ndi dazi;

mʼmalo mwa zovala zabwino, adzavala chiguduli;

mʼmalo mwa kunyadira kukongola adzachita manyazi.

25Iwe Yerusalemu anthu ako aamuna adzaphedwa ndi lupanga,

asilikali ako adzafera ku nkhondo.

26Pa zipata za Ziyoni padzakhala kubuma ndi kulira;

Iweyo udzasakazidwa nʼkukhala pansi, ukugubuduzika pa fumbi.

Bibelen på hverdagsdansk

Esajasʼ Bog 3:1-26

Dom over folkets ledere

1Herren, den Almægtige, vil afskære Jerusalem og Juda fra al hjælp og alle forsyninger af mad og vand. 2Han vil fjerne landets ledere—helte og krigere, dommere og profeter, spåmænd og slægtsoverhoveder, 3delingsførere og magtfulde mænd, rådgivere, troldmænd og slangetæmmere.

4De får drenge som ledere, kåde knægte skal herske over dem. 5Der bliver anarki og kaos. Folk bekæmper hinanden, de unge gør oprør mod de ældre, slyngler overfuser hæderlige folk. 6Når den tid kommer, vil en mand gribe fat i sin slægtning og sige: „Du har i det mindste tøj på kroppen. Tag ledelsen, så vi kan få ryddet op i det her rod!” 7Men hans slægtning vil svare: „Nej tak! Jeg vil ikke overtage et fallitbo. Jeg har slet ikke ressourcer til at klare den opgave.” 8Jerusalem falder og Judariget går i opløsning, fordi de har trodset Herren med deres ord og handlinger og ringeagtet hans ære og værdighed. 9Deres ansigtsudtryk er nok til at afsløre dem. De er stolte over deres synder som Sodomas mænd, de har ikke skygge af skam i livet. De har nedkaldt dommen over sig selv.

10Lad de retskafne glæde sig, for dem skal det gå godt. De skal nyde frugten af deres gode gerninger. 11Men ve de onde, for med dem står det skidt til. De skal få, hvad de har fortjent.

12Folkets ledere er som selviske børn og dominerende kvinder. De vejleder jer ikke, de vildleder jer! De fører jer på afveje, så I ender i afgrunden.

13Herren rejser sig, parat til at dømme folkene. 14Herren, den Almægtige, anklager folkets ledere og siger: „Det er jer, der har plyndret vinmarkerne og røvet kornhøsten fra de magtesløse bønder. 15Hvor vover I at knuse mit folk og træde de fattige ned i støvet?”

Dom over de stolte kvinder

16Herren siger: „Jerusalems kvinder tripper stolte af sted med ringlende ankelkæder og næsen i sky, med knejsende nakke og kælne blikke. 17Derfor vil jeg gøre dem skaldede, så de må gå skamfulde omkring.”

18-19Herren vil fjerne al deres pynt: ankelkæder, månetegn og soltegn, øreringe, armbånd, slør, 20tørklæder, ankellænker,3,20 Meningen uklar. Måske er det en kort lænke, som tvang dem til at tage små skridt. bælter, lugtedåser, amuletter, 21fingerringe, næseringe, 22festdragter, kapper, slag, tasker, 23spejle, kjortler, turbaner og sjaler. 24I stedet for duft af parfume bliver der stank, i stedet for et bælte om livet får de reb, i stedet for kunstfærdige frisurer skaldethed, i stedet for festtøj sækkelærred, i stedet for skønhed skam.

Dommen over landets og byens krigere

25Landets mænd vil falde for sværdet, Jerusalems krigere dø i kamp. 26På byens torve vil man jamre og klage, for byen er som en kvinde, der sidder på jorden, berøvet alt.