Yesaya 27 – CCL & NIRV

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yesaya 27:1-13

Za Munda Wamphesa wa Yehova

1Tsiku limenelo,

Yehova ndi lupanga lake

lakuthwa, lalikulu ndi lamphamvu,

adzalanga Leviyatani chinjoka chothawa chija,

Leviyatani chinjoka chodzikulunga;

adzapha chirombo choopsa cha mʼnyanja.

2Tsiku limenelo Yehova adzati,

“Tidzayimba nyimbo ya munda wamphesa wobereka bwino:

3Ine, Yehova, ndimawuyangʼanira;

ndimawuthirira nthawi zonse.

Ndimawulondera usana ndi usiku

kuti wina angawononge.

4Ine sindinakwiye.

Ngati mkandankhuku ndi minga zikanaoneka ndikanalimbana nazo!

Ndikachita nazo nkhondo;

ndikanazitentha zonse ndi moto.

5Koma ngati apo ayi, abweretu kwa Ine adani angawo kuti ndidzawateteze;

apangane nane za mtendere,

ndithu, apangane nane za mtendere.”

6Masiku akubwerawo Yakobo adzazika mizu,

Israeli adzaphukira ndi kuchita maluwa,

ndipo adzadzaza dziko lonse lapansi ndi zipatso.

7Kodi Yehova anakantha Israeli

ngati momwe anakanthira anthu amene anazunza Israeli?

Kapena kodi Yehova anapha Israeli

ngati mmene anthu ena anaphera Israeli?

8Yehova mwawalanga powapirikitsa ndi kuwatumiza ku ukapolo,

mwawachotsa ndi mpweya wanu woopsa,

monga zimachitikira pa tsiku la mkuntho wochokera kummawa.

9Yehova adzakhululuka kulakwa kwa Yakobo.

Iwo adzaonetsa kuti alapadi pamene adzaphwanya miyala yonse ya guwa lachikunja,

ngati mmene anthu amaphwanyira miyala yanjereza

mpaka kukhala ngati fumbi lokhalokha.

Sipadzapezekanso mafano a Asera

kapena maguwa ofukiza lubani.

10Mzinda wamalinga uja wasanduka bwinja,

wasanduka malo osiyidwa, ndi kutayidwa ngati chipululu;

kumeneko amadyetselako ana angʼombe

kumeneko zimapumulako ziweto

ndi kumwetula nthambi za mitengo kotheratu.

11Pamene nthambi za mitengoyo zauma, zimathyoka

ndipo amayi amabwera nazitola ndi kuzisandutsa nkhuni.

Pakuti awa ndi anthu opanda nzeru;

kotero Mulungu amene anawapanga sadzachitira chisoni,

ndipo Mlengi wawo sawakomera mtima.

12Tsiku limenelo Yehova adzasonkhanitsa pamodzi anthu ake mmodzimmodzi kumalo opunthira tirigu, kuchokera ku mtsinje wa Yufurate mpaka ku mtsinje wa ku Igupto. 13Ndipo tsiku limenelo lipenga lalikulu lidzalira. Amene akuzunzika ku Asiriya iwo amene ali ku ukapolo ku Igupto adzabwera ndi kudzalambira Yehova pa phiri lopatulika mu Yerusalemu.

New International Reader’s Version

Isaiah 27:1-13

Israel Will Be Saved

1At that time

the Lord will punish Leviathan with his sword.

His great, powerful and deadly sword will punish

the serpent that glides through the sea.

He will kill that twisting sea monster.

2At that time the Lord will sing about his fruitful vineyard. He will say,

3“I am the Lord. I watch over my vineyard.

I water it all the time.

I guard it day and night.

I do it so no one can harm it.

4I am not angry with my vineyard.

I wish thorns and bushes would come up in it.

Then I would march out against them in battle.

I would set all of them on fire.

5So the enemies of my people should come to me for safety.

They should make peace with me.

I will say it again.

They should make peace with me.”

6In days to come, Jacob’s people will put down roots like a vine.

Israel will bud and bloom.

They will fill the whole world with fruit.

7The Lord struck down those who struck down Israel.

But he hasn’t punished Israel as much.

The Lord killed those who killed many of his people.

But he hasn’t punished his people as much.

8The Lord will use war to punish Israel.

He will make them leave their land.

With a strong blast of his anger he will drive them out.

It will be as if the east wind were blowing.

9The people of Jacob will have to pay for their sin.

Here is how they will show that their sin has been removed.

They will make all the altar stones like limestone.

They will crush them to pieces.

No poles used to worship the female god named Asherah will be left standing.

No incense altars will be left either.

10Cities that have high walls around them will become empty.

They will be settlements with no one in them.

They will be like a desert.

Calves will eat and lie down in them.

They will strip bare the branches of their trees.

11When their twigs are dry, they will be broken off.

Then women will come and make fires with them.

The people of Jacob don’t understand the Lord.

So the God who made them won’t be concerned about them.

Their Creator won’t be kind to them.

12At that time the Lord will separate Israel from other people. He will gather the Israelites together one by one. He will gather them from the Euphrates River to the Wadi of Egypt. 13At that time a loud trumpet will be blown. Those who were dying in Assyria will come and worship the Lord. So will those who were taken away to Egypt. All of them will worship the Lord on his holy mountain in Jerusalem.