Yesaya 26 – CCL & NIRV

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yesaya 26:1-21

Nyimbo ya Matamando

1Tsiku limenelo anthu a mʼdziko la Yuda adzayimba nyimbo iyi.

Tili ndi mzinda wolimba.

Mulungu amawuteteza ndi zipupa

ndi malinga.

2Tsekulani zipata za mzinda

kuti mtundu wolungama

ndi wokhulupirika ulowemo.

3Inu mudzamupatsa munthu

wa mtima wokhazikika

mtendere weniweni.

4Mudalireni Yehova mpaka muyaya,

chifukwa Yehova Mulungu ndiye Thanthwe losatha.

5Iye amatsitsa anthu amene amadziyika pamwamba,

iye amagwetsa pansi mzinda wodzitukumula,

amagumula makoma ake

ndi kuwagwetsa pansi pa fumbi penipeni.

6Mapazi a anthu akuwupondereza,

mapazi a anthu oponderezedwa,

mapazi anthu osauka.

7Njira ya munthu wolungama ndi yosalaza,

Inu Wolungamayo, mumasalaza njira ya wolungama.

8Inde Yehova, timayenda mʼnjira zanu zolungama,

ife timayembekezera Inu;

mitima yathu imakhumba kukumbukira

ndi kulemekeza dzina lanu.

9Moyo wanga umalakalaka Inu usiku wonse;

nthawi yammawa ndimafunafuna Inu.

Pamene muweruza dziko lapansi

anthu amaphunzira kuchita chilungamo.

10Ngakhale mukomere mtima anthu oyipa,

saphunzira chilungamo.

Amachita zoyipa mʼdziko la chilungamo,

ndipo sazindikira ululu wa Yehova.

11Inu Yehova, mwatukula dzanja lanu kuti muwalange,

koma iwo sakuliona dzanjalo.

Aloleni anthu aone ndi kuchita manyazi poona mmene mukondera anthu anu;

ndipo moto umene mwasonkhera adani anu uwapsereze.

12Yehova, mumatipatsa mtendere;

ndipo zonse zimene ife tinazichita munatichitira ndinu.

13Inu Yehova Mulungu wathu, ngakhale takhala tikulamulidwa ndi ena mʼmalo mwanu,

koma ife timalemekeza dzina lanu lokha.

14Iwo tsopano sadzadzukanso;

mizimu yawo sidzabwera kudzativutitsa

pakuti mwawalanga ndipo mwawawononga;

palibenso amene amawakumbukira.

15Inu Yehova, mwaukulitsa mtundu wathu;

mwauchulukitsa ndithu

ndipo mwalandirapo ulemu;

mwaukuza mbali zonse za dziko.

16Yehova, anthu anu anabwera kwa Inu pamene anali mʼmasautso;

pamene munawalanga,

iwo anapemphera kwa Inu.

17Monga mayi woyembekezera pamene nthawi yake yobereka yayandikira

amamva kupweteka ndipo amalira ndi ululu,

ifenso tinali chimodzimodzi pamaso panu, Inu Yehova.

18Ife chimodzimodzi tinamva ululu, ngati mayi pa nthawi yobala mwana,

koma sitinapindulepo kanthu,

kapena kupulumutsa dziko lapansi;

sitinabadwitse anthu atsopano pa dziko pano.

19Koma anthu anu amene anafa adzakhalanso ndi moyo;

matupi awo adzadzuka.

Iwo amene ali ku fumbi tsopano

adzadzuka ndi kuyimba mosangalala.

Monga mame amafewetsa pansi kutsitsimutsa zomera,

momwenso Yehova adzaukitsa anthu amene anafa kale.

20Abale anga, pitani mukalowe mʼnyumba zanu

ndipo mukadzitsekere;

mukabisale kwa kanthawi kochepa

mpaka ukali wake utatha.

21Taonani, Yehova akubwera kuchokera kumene amakhala;

akubwera kudzalanga anthu a dziko lapansi chifukwa cha machimo awo.

Dziko lapansi lidzawulula magazi amene anakhetsedwa pa dzikolo;

dziko lapansi silidzabisanso mitembo ya anthu ophedwa.

New International Reader’s Version

Isaiah 26:1-21

Another Song of Praise

1At that time a song will be sung in the land of Judah. It will say,

“We have a strong city.

God’s saving power surrounds it

like walls and towers.

2Open its gates

so that those who do what is right can enter.

They are the people who remain faithful to God.

3Lord, you will give perfect peace

to those who commit themselves to be faithful to you.

That’s because they trust in you.

4“Trust in the Lord forever.

The Lord himself is the Rock.

The Lord will keep us safe forever.

5He brings down those who are proud.

He pulls down cities that have high walls.

They fall down flat on the ground.

He throws them down to the dust.

6The feet of those who were treated badly stomp on them.

Those who were poor walk all over them.”

7The path of godly people is level.

You are the God who does what is right.

You make their way smooth.

8Lord, we are living the way your laws command us to live.

We are waiting for you to act.

We want your honor and fame to be known.

9My heart longs for you at night.

My spirit longs for you in the morning.

You will come and judge the earth.

Then the people of the world will learn to do what is right.

10Sometimes grace is shown to sinful people.

But they still don’t learn to do what is right.

They keep on doing evil even in a land where others are honest and fair.

They don’t have any respect for the majesty of the Lord.

11Lord, you have raised your hand high to punish them.

But they don’t even see it.

Let them see how much you love your people.

Then they will be put to shame.

Let the fire you are saving for your enemies burn them up.

12Lord, you give us peace.

You are the one who has done everything we’ve accomplished.

13Lord, you are our God.

Other masters besides you have ruled over us.

But your name is the only one we honor.

14Those other masters are now dead.

They will never live again.

Their spirits won’t rise from the dead.

You punished them and destroyed them.

You wiped out all memory of them.

15Lord, you have made our nation grow.

You have made it larger.

You have gained glory for yourself.

You have increased the size of our land.

16Lord, when your people were suffering, they came to you.

When you punished them,

they could barely whisper a prayer.

17Lord, you made us like a woman who is about to have a baby.

She groans and cries out in pain.

18We were pregnant and groaned with pain.

But nothing was born.

We didn’t bring your saving power to the earth.

And the people of the world have not come to life.

19Lord, your people who have died will live again.

Their bodies will rise from the dead.

Let those who lie in the grave

wake up and shout for joy.

You give life, Lord, like the dew of the morning.

So the earth will give up its dead people.

20My people, go into your houses.

Shut the doors behind you.

Hide yourselves for a little while.

Do it until the Lord’s anger is over.

21He is coming from the place where he lives.

He will punish the people of the earth for their sins.

The blood spilled on the earth will be brought out into the open.

The ground will no longer hide those who have been killed.