Yesaya 21 – CCL & KJV

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yesaya 21:1-17

Za Chilango cha Babuloni

1Uthenga wonena za chipululu cha mʼmbali mwa Nyanja.

Ankhondo a ku Elamu ndi Mediya adzabwera ngati kamvuluvulu amene akuwomba modutsa mʼmbali ya nyanja,

kuchokera ku chipululu,

dziko lochititsa mantha.

2Ine ndaona zinthu zoopsa mʼmasomphenya:

Wonyenga akunyenga, wofunkha akufunkha komanso owononga akuwononga.

Elamu, yambani nkhondo! Mediya, zingani mzinda!

Ine ndidzathetsa mavuto onse amene anayambitsa Ababuloni.

3Chifukwa cha zimenezi thupi langa likunjenjemera ndi mantha,

ndikumva ululu ngati wa mayi amene akubereka;

ndikuvutika kwambiri ndi zimene ndikumva,

ndathedwa nzeru ndi zimene ndikuziona.

4Mtima wanga ukugunda,

ndipo ndikunjenjemera ndi mantha;

chisisira chimene ndakhala ndikuchifuna

chasanduka chinthu choopsa kwa ine.

5Ankhondo a ku Elamu ndi Mediya akukonza matebulo,

akuyala mphasa,

akudya komanso kumwa!

Mwadzidzidzi anamva mawu akuti, “Dzukani inu ankhondo,

pakani mafuta zishango zanu!”

6Zimene Ambuye akunena kwa ine ndi izi;

“Pita, kayike mlonda

kuti azinena zimene akuziona.

7Taonani, anthu akubwera ali pa akavalo

ndipo akuyenda awiriawiri,

okwera pa bulu

kapena okwera pa ngamira,

mlondayo akhale tcheru kwambiri.”

8Ndipo mlondayo anafuwula kuti,

“Ambuye anga, tsiku ndi tsiku ndimakhala pa nsanja yolondera;

Usiku uliwonse ndimakhala pa malo anga olondera.

9Taonani, uyo munthu akubwera atakwera pa galeta

ali ndi gulu la akavalo.

Mmodzi wa iwo akuti,

‘Babuloni wagwa, wagwa!

Mafano onse a milungu yake

agwa pansi ndipo aphwanyika!’ ”

10Inu anthu anga opunthidwa ndi kupetedwa ngati tirigu,

ine ndikukuwuzani zimene ndamva

ndikukuwuzani Uthenga wochokera kwa Yehova Wamphamvuzonse,

Mulungu wa Israeli.

Za Chilango cha Edomu

11Uthenga wonena za Duma:

Munthu wina akundiyitana kuchokera ku Seiri kuti,

“Iwe mlonda, usikuwu utha liti?

Iwe mlonda, utha liti kodi usikuwu?”

12Mlonda akuyankha kuti,

“Kukucha, koma kudanso.

Ngati ukufuna kufunsa, funsa tsopano;

ndipo ubwerenso udzafunse.”

Za Chilango cha Arabiya

13Uthenga wonena za Arabiya:

Inu anthu amalonda a ku Dedani,

amene usiku mumagona mʼzithukuluzi za ku Arabiya,

14perekani madzi kwa anthu aludzu.

Inu anthu a ku Tema

perekani chakudya kwa anthu othawa nkhondo.

15Iwo akuthawa malupanga,

lupanga losololedwa,

akuthawa uta wokokakoka

ndiponso nkhondo yoopsa.

16Zimene Ambuye akunena kwa ine ndi izi: “Chaka chimodzi chisanathe, potsata mmene amawerengera munthu waganyu, ulemerero wonse wa Kedara udzatheratu. 17Mwa anthu okoka uta, ankhondo a ku Kedara opulumuka adzakhala owerengeka.” Wayankhula ndi Yehova Mulungu wa Israeli.

King James Version

Isaiah 21:1-17

1The burden of the desert of the sea. As whirlwinds in the south pass through; so it cometh from the desert, from a terrible land. 2A grievous vision is declared unto me; the treacherous dealer dealeth treacherously, and the spoiler spoileth. Go up, O Elam: besiege, O Media; all the sighing thereof have I made to cease.21.2 grievous: Heb. hard 3Therefore are my loins filled with pain: pangs have taken hold upon me, as the pangs of a woman that travaileth: I was bowed down at the hearing of it; I was dismayed at the seeing of it. 4My heart panted, fearfulness affrighted me: the night of my pleasure hath he turned into fear unto me.21.4 heart…: or, mind wandered21.4 turned: Heb. put 5Prepare the table, watch in the watchtower, eat, drink: arise, ye princes, and anoint the shield. 6For thus hath the Lord said unto me, Go, set a watchman, let him declare what he seeth. 7And he saw a chariot with a couple of horsemen, a chariot of asses, and a chariot of camels; and he hearkened diligently with much heed: 8And he cried, A lion: My lord, I stand continually upon the watchtower in the daytime, and I am set in my ward whole nights:21.8 he…: or, cried as a lion21.8 whole…: or, every night 9And, behold, here cometh a chariot of men, with a couple of horsemen. And he answered and said, Babylon is fallen, is fallen; and all the graven images of her gods he hath broken unto the ground. 10O my threshing, and the corn of my floor: that which I have heard of the LORD of hosts, the God of Israel, have I declared unto you.21.10 corn: Heb. son

11¶ The burden of Dumah. He calleth to me out of Seir, Watchman, what of the night? Watchman, what of the night? 12The watchman said, The morning cometh, and also the night: if ye will enquire, enquire ye: return, come.

13¶ The burden upon Arabia. In the forest in Arabia shall ye lodge, O ye travelling companies of Dedanim. 14The inhabitants of the land of Tema brought water to him that was thirsty, they prevented with their bread him that fled.21.14 brought: or, bring ye 15For they fled from the swords, from the drawn sword, and from the bent bow, and from the grievousness of war.21.15 from the swords: or, for fear, etc: Heb. from the face, etc 16For thus hath the Lord said unto me, Within a year, according to the years of an hireling, and all the glory of Kedar shall fail: 17And the residue of the number of archers, the mighty men of the children of Kedar, shall be diminished: for the LORD God of Israel hath spoken it.21.17 archers: Heb. bows