Yesaya 17 – CCL & CCBT

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yesaya 17:1-14

Uthenga Wotsutsa Damasiko

1Uthenga wonena za Damasiko:

“Taonani, mzinda wa Damasiko sudzakhalanso mzinda,

koma udzasanduka bwinja.

2Mizinda ya Aroeri idzakhala yopanda anthu

ndipo idzakhala ya ziweto, zimene zidzagona pansi

popanda wina woziopseza.

3Ku Efereimu sikudzakhalanso linga,

ndipo ku Damasiko sikudzakhalanso ufumu;

Otsalira a ku Siriya adzachotsedwa ulemu

monga anthu a ku Israeli,”

akutero Yehova Wamphamvuzonse.

4“Tsiku limenelo ulemerero wa Yakobo udzazimirira;

ndipo chuma chake chidzasanduka umphawi.

5Israeli adzakhala ngati munda wa tirigu

umene anatsiriza kukolola.

Adzakhalanso ngati munda wa mʼchigwa cha Refaimu

anthu atatha kukunkha ngala za tirigu.

6Komabe Aisraeli ochepa okha ndiwo ati adzatsale

monga mʼmene zimatsalira zipatso ziwiri kapena zitatu pa nthambi ya pamwamba penipeni

kapena zipatso zisanu pa nthambi za mʼmunsi

mwa mtengo wa olivi akawugwedeza,”

akutero Yehova, Mulungu wa Israeli.

7Tsiku limenelo anthu adzayangʼana Mlengi wawo

ndipo adzatembenukira kwa Woyerayo wa Israeli.

8Iwo sadzakhulupiriranso maguwa ansembe,

ntchito ya manja awo,

ndipo sadzadaliranso mitengo ya mafano a Asera,

ndiponso maguwa ofukizirapo lubani amene manja awo anapanga.

9Tsiku limenelo mizinda yawo yamphamvu, imene anasiya chifukwa cha Aisraeli, idzakhala ngati malo osiyidwa kuti awirire ndi kumera ziyangoyango. Ndipo yonse idzakhala mabwinja.

10Inu mwayiwalatu Mulungu Mpulumutsi wanu;

simunakumbukire Thanthwe, linga lanu.

Choncho, ngakhale munadzala mbewu zabwino,

ndi kuyitanitsa kunja mitengo ya mpesa,

11nimuyembekeza kuti zikule tsiku lomwelo

ndi kuphukira maluwa mmawa mwake,

komabe zimenezi sizidzakupindulirani

pa tsiku la mavuto.

12Aa, mkokomo wa anthu a mitundu yambiri,

akusokosa ngati kukokoma kwa nyanja!

Aa, phokoso la anthu a mitundu ina,

akusokosa ngati mkokomo wa madzi amphamvu!

13Ngakhale ankhondo a mitundu ina akubwera ndi mkokomo ngati wa madzi ambiri,

koma adzathawira kutali Mulungu akadzawadzudzula.

Yehova adzawapirikitsa ngati mankhusu owuluka ndi mphepo pa phiri,

ndi ngati fumbi la kamvuluvulu asanayambe.

14Pofika nthawi yamadzulo zoopsa zidzayamba kuchitika,

ndipo zidzakhala zitatha pofika mmawa.

Izi ndizo zidzachitikire anthu otilanda zinthu,

gawo la amene amatibera zinthu zathu.

Chinese Contemporary Bible (Traditional)

以賽亞書 17:1-14

關於大馬士革的預言

1以下是關於大馬士革的預言:

「看啊,大馬士革城必不復存在,淪為廢墟。

2亞羅珥的眾城邑必被廢棄,

羊群將在那裡棲息,

沒有人驚擾牠們。

3以法蓮17·3 舊約中常用以法蓮代表以色列國。的堡壘必被摧毀,

大馬士革的王權必喪失。

倖存的亞蘭人必像以色列人一樣失去榮耀。」

這是萬軍之耶和華說的。

4「到那日,雅各的榮耀必消失,

他肥胖的身軀必漸漸消瘦。

5國家好像一塊已收割的田地,

又像撿淨麥穗的利乏音谷。

6倖存者寥寥無幾,就像打過的橄欖樹上剩下的果子,

或兩三個掛在樹梢,

或四五個殘存在枝頭。」

這是以色列的上帝耶和華說的。

7到那日,人們必仰望他們的創造主,向以色列的聖者求助。 8那時他們不再仰望自己製造的祭壇,也不再供奉自己指頭所造的亞舍拉神像和香壇。 9到那日,他們因以色列人到來而遺棄的堅城必變為山林和高崗,一片荒涼。

10以色列人啊,

你們忘記了拯救你們的上帝,

不記得那保護你們的磐石。

所以,你們雖然栽種佳美的秧子,

插上遠方運來的樹苗,

11使它們在栽種的當天早上就生長開花,

也必一無所獲。

你們得到的只是艱難和無盡的痛苦。

12看啊,列國喧囂,如怒海洶湧;

萬民騷動,如洪水滔滔。

13雖然萬民喧囂如洶湧的洪水,

但上帝一聲斥責,他們便逃往遠方,

像山頂上被風捲走的糠秕,

又如狂風颳走的塵埃。

14他們晚上令人恐懼,早晨已無影無蹤。這就是擄掠我們之人的下場,搶奪我們之人的報應。