Yesaya 13 – CCL & NVI

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yesaya 13:1-22

Kulangidwa Kwa Babuloni

1Uthenga onena za Babuloni umene Yesaya mwana wa Amozi anawulandira:

2Kwezani mbendera yankhondo pa phiri loti see,

muwafuwulire ankhondo;

muwakodole kuti adzalowe pa zipata

za anthu olemekezeka.

3Ine Yehova, ndalamulira ankhondo anga;

ndasonkhanitsa ankhondo anga kuti akhale zida zanga zolangira

amene amadzikuza ndi chipambano changa.

4Tamvani phokoso ku mapiri,

likumveka ngati phokoso la gulu lalikulu la anthu!

Tamvani phokoso pakati pa maufumu,

ngati kuti mitundu ya anthu ikusonkhana pamodzi!

Yehova Wamphamvuzonse akukhazika asilikali ake mokonzekera

kuchita nkhondo.

5Iwo akuchokera ku mayiko akutali,

kuchokera kumalekezero a dziko

Yehova ali ndi zida zake za nkhondo

kuti adzawononge dziko la Babuloni.

6Lirani mofuwula, pakuti tsiku la Yehova layandikira;

lidzabwera ngati chiwonongeko chochokera kwa Wamphamvuzonse.

7Zimenezi zinafowoketsa manja onse,

mtima wa munthu aliyense udzachokamo.

8Anthu adzagwidwa ndi mantha aakulu,

zowawa ndi masautso zidzawagwera;

adzamva zowawa zonga amamva mayi pobereka.

Adzayangʼanana mwamantha,

nkhope zawo zikufiira ngati malawi amoto.

9Taonani, tsiku la Yehova likubwera,

tsiku lopanda chisoni, lawukali ndi lamkwiyo;

kudzasandutsa dziko kuti likhale chipululu

ndi kuwononga anthu ochimwa a mʼmenemo.

10Nyenyezi zakumwamba ndiponso zonse zamlengalenga

sizidzaonetsa kuwala kwawo.

Dzuwa lidzada potuluka,

ndipo mwezi sudzawala konse.

11Ndidzalanga dziko lonse chifukwa cha zolakwa zake,

anthu oyipa ndidzawalanga chifukwa cha machimo awo.

Ndidzathetsa kunyada kwa odzikuza,

ndipo ndidzatsitsa kudzitukumula kwa anthu ankhanza.

12Ndidzasandutsa anthu kukhala ovuta kupeza kuposa mmene amasowera golide wabwino.

Iwo sazidzapezekapezeka kuposa mmene amasowera golide wa ku Ofiri.

13Tsono ndidzagwedeza miyamba

ndipo dziko lapansi lidzachoka pa maziko ake.

Izi zidzachitika chifukwa cha ukali wa Wamphamvuzonse

pa tsiku la mkwiyo wake woopsa.

14Ngati mbawala zosakidwa,

ngati nkhosa zopanda wozikusa,

munthu aliyense adzabwerera kwa anthu akwawo,

aliyense adzathawira ku dziko lake.

15Aliyense amene atadzapezeke ndi kugwidwa

adzaphedwa momubaya ndi lupanga.

16Ana awo akhanda adzaphwanyidwa iwo akuona;

nyumba zawo zidzafunkhidwa ndipo akazi awo adzagwiriridwa.

17Taona, Ine ndidzadzutsa Amedi amene safuna siliva

ndipo sasangalatsidwa ndi golide,

kuti amenyane ndi Ababuloni.

18Adzapha anyamata ndi mauta awo;

sadzachitira chifundo ana

ngakhale kumvera chisoni ana akhanda.

19Babuloni, ufumu wake ndi waulemerero kuposa mafumu onse.

Anthu ake amawunyadira.

Koma Yehova adzawuwononga

ngati mmene anawonongera Sodomu ndi Gomora.

20Anthu sadzakhalamonso

kapena kukhazikikamo pa mibado yonse;

palibe Mwarabu amene adzayimike tenti yake,

palibe mʼbusa amene adzawetamo ziweto zake.

21Koma nyama zakuthengo ndizo zidzakhale kumeneko,

nyumba zake zidzadzaza ndi nkhandwe;

mu mzindamo muzidzakhala akadzidzi,

ndipo atonde akuthengo azidzalumphalumphamo.

22Mu nsanja zake muzidzalira afisi,

mʼnyumba zake zokongola muzidzalira nkhandwe.

Nthawi yake yayandikira

ndipo masiku ake ali pafupi kutha.

Nueva Versión Internacional

Isaías 13:1-22

Profecía contra Babilonia

1Profecía contra Babilonia que recibió Isaías, hijo de Amoz:

2Sobre un monte alto agiten la bandera;

llámenlos a gritos;

háganles señales con la mano

para que entren por las puertas de los nobles.

3Ya he dado orden a mis consagrados;

he reclutado a mis guerreros,

a los que se alegran de mi triunfo, para que ejecuten mi ira.

4¡Escuchen! Se oye tumulto en las montañas,

como el de una gran multitud.

¡Escuchen! Se oye un estruendo de reinos,

de naciones que se han reunido.

El Señor de los Ejércitos pasa revista

a un ejército para la batalla.

5Vienen de tierras lejanas,

de los confines de los cielos.

Viene el Señor con las armas de su ira

para destruir toda la tierra.

6¡Giman, que el día del Señor está cerca!

Llega de parte del Todopoderoso como una devastación.

7Por eso todas las manos desfallecen,

todo el mundo pierde el ánimo.

8Quedan todos aterrados;

dolores y angustias los atrapan:

¡se retuercen de dolor, como si estuvieran de parto!

Espantados, se miran unos a otros;

¡tienen el rostro encendido!

9¡Miren! ¡Ya viene el día del Señor

—día cruel, de furor y ardiente ira—;

dejará la tierra devastada

y exterminará en ella a los pecadores!

10Las estrellas y las constelaciones del cielo

dejarán de irradiar su luz;

se oscurecerá el sol al salir

y no brillará más la luna.

11Castigaré por su maldad al mundo

y por su iniquidad a los malvados.

Pondré fin a la soberbia de los arrogantes

y humillaré el orgullo de los violentos.

12Voy a hacer que haya menos gente que oro fino,

menos mortales que oro de Ofir.

13Por eso haré que tiemble el cielo

y que la tierra se mueva de su sitio,

por el furor del Señor de los Ejércitos,

en el día de su ardiente ira.

14Como gacela acosada,

como rebaño sin pastor,

cada uno se volverá a su propio pueblo,

cada cual huirá a su propia tierra.

15Al que atrapen lo traspasarán;

el que caiga preso morirá a filo de espada.

16Ante sus propios ojos estrellarán a sus pequeños,

saquearán sus casas y violarán a sus mujeres.

17¡Miren! Yo incito contra ellos a los medos,

pueblo al que no le importa la plata

ni se deleita en el oro.

18Con sus arcos traspasarán a los jóvenes;

no se apiadarán del fruto del vientre

ni tendrán compasión de los niños.

19Babilonia, la perla de los reinos,

la gloria y el orgullo de los babilonios,13:19 Lit. caldeos.

quedará como Sodoma y Gomorra

cuando Dios las destruyó.

20Nunca más volverá a ser habitada

ni poblada en los tiempos venideros.

No volverá a acampar allí el beduino,

ni hará el pastor descansar a su rebaño.

21Allí descansarán las fieras del desierto;

sus casas se llenarán de chacales.

Allí habitarán los avestruces

y brincarán las cabras salvajes.

22En sus fortalezas aullarán las hienas

y en sus lujosos palacios, los chacales.

Su hora está por llegar

y no se prolongarán sus días.