Nyimbo za Mayamiko
1Tsiku limenelo aliyense wa inu adzati:
“Ndikukuyamikani, Inu Yehova;
chifukwa ngakhale munandipsera mtima,
mkwiyo wanu wachoka,
ndipo mwanditonthoza.
2Zoonadi, Mulungu ndiye Mpulumutsi wanga;
ndidzamudalira ndipo sindidzachita mantha.
Yehova ndiye mphamvu yanga ndi nyimbo yanga;
Iye wakhala chipulumutso changa.”
3Mudzakondwera popeza Yehova
ali ngati chitsime cha chipulumutso chanu.
4Tsiku limenelo mudzati:
“Yamikani Yehova, tamandani dzina lake;
mulengeze ntchito zake pakati pa mitundu ya anthu,
ndipo mulalike kuti dzina lake ndi lopambana.
5Imbirani Yehova, pakuti wachita ntchito zazikulu;
zimenezi zidziwike pa dziko lonse lapansi.
6Fuwulani ndi kuyimba mwachimwemwe, inu anthu a ku Ziyoni;
pakuti Woyerayo wa Israeli ndi wamkulu pakati panu.”
Canciones de alabanza
1En aquel día tú dirás:
«Señor, yo te alabaré
porque, aunque estabas enojado conmigo,
tu ira se ha calmado
y me has dado consuelo.
2¡Dios es mi salvación!
Confiaré en él y no temeré.
El Señor es mi fuerza,
el Señor es mi canción;
¡él es mi salvación!».
3Con alegría sacarán ustedes agua
de las fuentes de la salvación.
4En aquel día dirán:
«Alaben al Señor, invoquen su nombre;
den a conocer entre los pueblos sus obras;
proclamen la grandeza de su nombre.
5Canten salmos al Señor, porque ha hecho maravillas;
que esto se dé a conocer en toda la tierra.
6¡Canta y grita de alegría, habitante de Sión,
pues es grande, en medio de ti, el Santo de Israel!».