Yesaya 12 – CCL & NVI

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yesaya 12:1-6

Nyimbo za Mayamiko

1Tsiku limenelo aliyense wa inu adzati:

“Ndikukuyamikani, Inu Yehova;

chifukwa ngakhale munandipsera mtima,

mkwiyo wanu wachoka,

ndipo mwanditonthoza.

2Zoonadi, Mulungu ndiye Mpulumutsi wanga;

ndidzamudalira ndipo sindidzachita mantha.

Yehova ndiye mphamvu yanga ndi nyimbo yanga;

Iye wakhala chipulumutso changa.”

3Mudzakondwera popeza Yehova

ali ngati chitsime cha chipulumutso chanu.

4Tsiku limenelo mudzati:

“Yamikani Yehova, tamandani dzina lake;

mulengeze ntchito zake pakati pa mitundu ya anthu,

ndipo mulalike kuti dzina lake ndi lopambana.

5Imbirani Yehova, pakuti wachita ntchito zazikulu;

zimenezi zidziwike pa dziko lonse lapansi.

6Fuwulani ndi kuyimba mwachimwemwe, inu anthu a ku Ziyoni;

pakuti Woyerayo wa Israeli ndi wamkulu pakati panu.”

Nueva Versión Internacional

Isaías 12:1-6

Canciones de alabanza

1En aquel día tú dirás:

«Señor, yo te alabaré

porque, aunque estabas enojado conmigo,

tu ira se ha calmado

y me has dado consuelo.

2¡Dios es mi salvación!

Confiaré en él y no temeré.

El Señor es mi fuerza,

el Señor es mi canción;

¡él es mi salvación!».

3Con alegría sacarán ustedes agua

de las fuentes de la salvación.

4En aquel día dirán:

«Alaben al Señor, invoquen su nombre;

den a conocer entre los pueblos sus obras;

proclamen la grandeza de su nombre.

5Canten salmos al Señor, porque ha hecho maravillas;

que esto se dé a conocer en toda la tierra.

6¡Canta y grita de alegría, habitante de Sión,

pues es grande, en medio de ti, el Santo de Israel!».