Yesaya 11 – CCL & NIV

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yesaya 11:1-16

Za Ufumu Wamtendere wa Mesiya

1Padzatuluka mphukira pa tsinde la Yese

ndipo nthambi idzaphukira kuchokera ku mizu yake.

2Mzimu wa Yehova udzakhala pa iye

Mzimu wanzeru ndi wa kumvetsa zinthu,

Mzimu wauphungu ndi wamphamvu,

Mzimu wachidziwitso ndi wakuopa Yehova.

3Ndipo kuopa Yehova ndiye chidzakhale chinthu chomukondweretsa.

Iye sadzaweruza potsata zooneka pamaso,

kapena kugamula mlandu potsata zakumva;

4koma amphawi adzawaweruza mwachilungamo,

adzaweruza mwachilungamo mlandu wa anthu osauka a dziko lapansi.

Iye adzakantha dziko lapansi ndi mawu ake;

atalamula Iyeyu anthu oyipa adzaphedwa.

5Chilungamo chidzakhala ngati lamba wake

ndipo kukhulupirika kudzakhala ngati chomangira mʼchiwuno mwake.

6Mʼmbulu udzakhala pamodzi ndi mwana wankhosa,

kambuku adzagona pansi pamodzi ndi mwana wambuzi,

mwana wangʼombe ndi mwana wa mkango adzadyera limodzi

ndipo mwana wamngʼono adzaziweta.

7Ngʼombe yayikazi ndi chimbalangondo zidzadya pamodzi,

ana awo adzagona pamodzi,

ndipo mkango udzadya udzu ngati ngʼombe.

8Mwana wakhanda adzasewera pa dzenje la mamba,

ndipo mwana wamngʼono adzapisa dzanja lake ku phanga la mphiri osalumidwa.

9Sipadzakhala chilichonse chopweteka kapena chowononga

pa phiri lopatulika la Yehova,

pakuti anthu a dziko lapansi adzadzaza ndi nzeru yotha kudziwa Yehova

monga momwe nyanja imadzazira ndi madzi.

10Tsiku limenelo mfumu yatsopano yochokera pa Muzu wa Yese idzakhala ngati chizindikiro kwa anthu a mitundu yonse. Mitundu ya anthu idzasonkhana kwa Iye, ndipo malo awo okhalapo adzakhala aulemerero. 11Tsiku limenelo Ambuye adzatambasula dzanja lake kachiwiri kuti awombole anthu ake otsalira ku Asiriya, ku Igupto, ku Patirosi, Kusi, ku Elamu, ku Sinana, ku Hamati ndi pa zilumba za nyanja yamchere.

12Adzakwezera mitundu ya anthu mbendera,

ndipo adzasonkhanitsa otayika a ku Israeli;

Iye adzasonkhanitsa anthu obalalika a ku Yuda

kuchokera ku mbali zonse zinayi za dziko lapansi.

13Nsanje ya Efereimu idzatha,

ndipo adani a Yuda adzatha;

Efereimu sadzachitira nsanje Yuda,

ngakhale Yuda sadzamuda Efereimu.

14Yuda ndi Efereimu adzathira nkhondo pa Afilisti mbali ya kumadzulo;

ndipo onsewo pamodzi adzalanda zinthu za anthu a kummawa.

Adzalimbana ndi Edomu ndi Mowabu,

ndipo Aamoni adzawagonjera.

15Yehova adzaphwetsa

mwendo wa nyanja ya Igupto;

adzatambasula dzanja lake ndipo adzawombetsa mphepo yotentha

pa mtsinje wa Yufurate.

Iye adzawugawa mtsinjewo kukhala timitsinje tisanu ndi tiwiri

kuti anthu athe kuwoloka powuma atavala nsapato.

16Padzakhala msewu waukulu woti ayendepo anthu ake otsalira

amene anatsalira ku Asiriya,

monga mmene panali msewu waukulu woyendapo Israeli

pamene amachokera ku Igupto.

New International Version

Isaiah 11:1-16

The Branch From Jesse

1A shoot will come up from the stump of Jesse;

from his roots a Branch will bear fruit.

2The Spirit of the Lord will rest on him—

the Spirit of wisdom and of understanding,

the Spirit of counsel and of might,

the Spirit of the knowledge and fear of the Lord

3and he will delight in the fear of the Lord.

He will not judge by what he sees with his eyes,

or decide by what he hears with his ears;

4but with righteousness he will judge the needy,

with justice he will give decisions for the poor of the earth.

He will strike the earth with the rod of his mouth;

with the breath of his lips he will slay the wicked.

5Righteousness will be his belt

and faithfulness the sash around his waist.

6The wolf will live with the lamb,

the leopard will lie down with the goat,

the calf and the lion and the yearling11:6 Hebrew; Septuagint lion will feed together;

and a little child will lead them.

7The cow will feed with the bear,

their young will lie down together,

and the lion will eat straw like the ox.

8The infant will play near the cobra’s den,

and the young child will put its hand into the viper’s nest.

9They will neither harm nor destroy

on all my holy mountain,

for the earth will be filled with the knowledge of the Lord

as the waters cover the sea.

10In that day the Root of Jesse will stand as a banner for the peoples; the nations will rally to him, and his resting place will be glorious. 11In that day the Lord will reach out his hand a second time to reclaim the surviving remnant of his people from Assyria, from Lower Egypt, from Upper Egypt, from Cush,11:11 That is, the upper Nile region from Elam, from Babylonia,11:11 Hebrew Shinar from Hamath and from the islands of the Mediterranean.

12He will raise a banner for the nations

and gather the exiles of Israel;

he will assemble the scattered people of Judah

from the four quarters of the earth.

13Ephraim’s jealousy will vanish,

and Judah’s enemies11:13 Or hostility will be destroyed;

Ephraim will not be jealous of Judah,

nor Judah hostile toward Ephraim.

14They will swoop down on the slopes of Philistia to the west;

together they will plunder the people to the east.

They will subdue Edom and Moab,

and the Ammonites will be subject to them.

15The Lord will dry up

the gulf of the Egyptian sea;

with a scorching wind he will sweep his hand

over the Euphrates River.

He will break it up into seven streams

so that anyone can cross over in sandals.

16There will be a highway for the remnant of his people

that is left from Assyria,

as there was for Israel

when they came up from Egypt.