Yesaya 12 – CCL & NIV

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yesaya 12:1-6

Nyimbo za Mayamiko

1Tsiku limenelo aliyense wa inu adzati:

“Ndikukuyamikani, Inu Yehova;

chifukwa ngakhale munandipsera mtima,

mkwiyo wanu wachoka,

ndipo mwanditonthoza.

2Zoonadi, Mulungu ndiye Mpulumutsi wanga;

ndidzamudalira ndipo sindidzachita mantha.

Yehova ndiye mphamvu yanga ndi nyimbo yanga;

Iye wakhala chipulumutso changa.”

3Mudzakondwera popeza Yehova

ali ngati chitsime cha chipulumutso chanu.

4Tsiku limenelo mudzati:

“Yamikani Yehova, tamandani dzina lake;

mulengeze ntchito zake pakati pa mitundu ya anthu,

ndipo mulalike kuti dzina lake ndi lopambana.

5Imbirani Yehova, pakuti wachita ntchito zazikulu;

zimenezi zidziwike pa dziko lonse lapansi.

6Fuwulani ndi kuyimba mwachimwemwe, inu anthu a ku Ziyoni;

pakuti Woyerayo wa Israeli ndi wamkulu pakati panu.”

New International Version

Isaiah 12:1-6

Songs of Praise

1In that day you will say:

“I will praise you, Lord.

Although you were angry with me,

your anger has turned away

and you have comforted me.

2Surely God is my salvation;

I will trust and not be afraid.

The Lord, the Lord himself, is my strength and my defense12:2 Or song;

he has become my salvation.”

3With joy you will draw water

from the wells of salvation.

4In that day you will say:

“Give praise to the Lord, proclaim his name;

make known among the nations what he has done,

and proclaim that his name is exalted.

5Sing to the Lord, for he has done glorious things;

let this be known to all the world.

6Shout aloud and sing for joy, people of Zion,

for great is the Holy One of Israel among you.”