Yeremiya 9 – CCL & KLB

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yeremiya 9:1-26

1Aa, ndikanakonda kuti mutu wanga ukanakhala chitsime cha madzi,

ndi maso anga ngati kasupe wa misozi!

Ndikanalira usana ndi usiku

kulirira anthu anga amene aphedwa.

2Ndani adzandipatsa malo

ogona mʼchipululu

kuti ndiwasiye anthu anga

ndi kuwachokera kupita kutali;

pakuti onse ndi achigololo,

ndiponso gulu la anthu onyenga.

3“Amapinda lilime lawo ngati uta.

Mʼdzikomo mwadzaza

ndi mabodza okhaokha

osati zoonadi.

Amapitirirabe kuchita zoyipa;

ndipo sandidziwa Ine.”

Akutero Yehova.

4“Aliyense achenjere ndi abwenzi ake;

asadalire ngakhale abale ake.

Aliyense amafuna kumudyera mʼbale wake masuku pa mutu.

Choncho aliyense amachitira bwenzi lake ugogodi.

5Aliyense amamunamiza mʼbale wake

ndipo palibe amene amayankhula choonadi.

Anapazoloweza pakamwa pawo kunena zabodza;

amalimbika kuchita machimo.

6Iwe wakhalira mʼchinyengo

ndipo ukukana kundidziwa Ine,”

akutero Yehova.

7Nʼchifukwa chake Yehova Wamphamvuzonse akuti,

“Taonani, Ine ndidzawasungunula ngati chitsulo ndi kuwayesa.

Kodi ndingachite nawonso

bwanji chifukwa cha machimo awo?

8Lilime lawo lili ngati muvi wakuthwa;

limayankhula zachinyengo.

Aliyense ndi pakamwa pake amayankhula mawu achikondi kwa mnansi wake,

koma mu mtima mwake amakonzekera zomuchita chiwembu.

9Kodi ndilekerenji kuwalanga chifukwa cha zimenezi?

akutero Yehova.

‘Kodi ndisawulipsire

mtundu wotere wa anthu?’ ”

10Ndidzakhetsa misozi ndi kulira kwamphamvu chifukwa cha mapiri

ndipo ndidzadandaula chifukwa cha msipu wa ku chipululu.

Malo onsewo awonongeka ndipo palibe amene amapitako,

ndipo sikumveka kulira kwa ngʼombe.

Mbalame zamlengalenga zathawa

ndipo nyama zakuthengo zachokako.

11Ndipo Yehova anati, “Ndidzasandutsa Yerusalemu kukhala bwinja,

malo okhalamo ankhandwe;

ndipo ndidzawononga mizinda ya Yuda

kotero kuti palibe munthu amene adzakhalemo.”

12Ine ndinati, “Kodi munthu wanzeru ndani woti nʼkumvetsa zimenezi? Kodi ndani amene Yehova anayankhula naye zimenezi kuti akafotokozere ena? Nʼchifukwa chiyani dziko lawonongeka ndi kusanduka chipululu, mʼmene anthu sadutsamo?”

13Yehova anati, “Nʼchifukwa chakuti anthuwa analeka kutsata malamulo anga amene ndinawapatsa; sanandimvere kapena kuwasamala. 14Mʼmalo mwake, anatsatira zolakwa za mʼmitima yawo; anapembedza Abaala ngati momwe makolo awo anawaphunzitsira.” 15Tsono chimene Ine Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli ndidzachite ndi anthu amenewa ndi ichi: “Ndidzawadyetsa chakudya cha ziphe ndi kuwamwetsa madzi a ndulu. 16Ndidzawabalalitsa pakati pa mitundu ya anthu imene iwowo kapena makolo awo sanayidziwe, ndipo ndidzawalondola ndi ankhondo mpaka nditawawononga.”

17Yehova Wamphamvuzonse akuti,

“Tsopano ganizirani! Muyitane akazi olira mwachisoni kuti abwere;

itanani akazi odziwa kulira bwino.”

18Anthu akuti, “Abwere mofulumira

kuti adzatilire

mpaka mʼmaso mwathu mutatuluka misozi

ndi kuti msidze zathu zinyowe ndi madzi.

19Kulira mwachisoni kukumveka kuchokera mu Ziyoni akuti,

‘Aa! Ife tawonongeka!

Tachita manyazi kwambiri!

Tiyenera kuchoka mʼdziko lathu

chifukwa atipirikitsa mʼnyumba zathu.’ ”

20Tsono inu amayi, imvani mawu a Yehova;

tcherani makutu anu kuti mumve mawu a Yehova.

Phunzitsani ana anu aakazi kulira mwachisoni;

aliyense aphunzitse mnzake nyimbo ya maliro.

21Imfa yatifikira kudzera mʼmazenera athu

ndipo yalowa mʼnyumba zathu zotetezedwa;

yapha ana athu mʼmisewu,

ndi achinyamata athu mʼmabwalo.

22Yehova anandiwuza kuti ndinene izi kuti,

“ ‘Mitembo ya anthu

idzakhala ili lambalamba ngati ndowe mʼminda,

ngati mapesi mʼmbuyo mwa wokolola,

popanda munthu woyitola.’ ”

23Yehova akuti,

“Munthu wanzeru asanyadire nzeru zake,

kapena munthu wamphamvu kunyadira nyonga zake,

kapena munthu wolemera kunyadira chuma chake,

24koma ngati munthu akufuna kunyadira, anyadire chinthu ichi:

kuti iye amamvetsa za Ine ndipo amandidziwa,

kuti ndine Yehova, amene ndimakonda chifundo,

chilungamo ndiponso ungwiro pa dziko lapansi.

Zimenezi ndizo ndimakondwera nazo,”

akutero Yehova.

25“Nthawi ikubwera,” akutero Yehova, “pamene ndidzalanga onse amene anachita mdulidwe koma mu mtima sasamala nʼkomwe. 26Ndidzalanga anthu a ku Igupto, Yuda, Edomu, Amoni, Mowabu, ndiponso onse amene amakhala kutali ku chipululu. Mitundu ina yonseyi ndi yosachita mdulidwe, ngakhalenso Aisraeli nawonso sanachite mdulidwe wa mu mtima.”

Korean Living Bible

예레미야 9:1-26

1내 머리가 우물이 되고 내 눈이 눈물의 샘이 된다면 죽음을 당한 내 백성들을 위하여 내가 밤낮 울 수 있을 텐데!

2내가 광야에 머물 곳이 있다면 내 백성을 멀리 떠날 수 있을 텐데. 그들은 다 간음하는 자들이며 반역의 무리이다.

3여호와께서 말씀하신다. “그들이 활을 당기듯이 혀를 놀려 거짓말을 쏘아대니 이 땅에는 진실이 아닌 거짓이 판을 친다. 그들은 악에서 악으로 줄달음치며 나를 자기들의 하나님으로 인정하지 않는다.

4“너희는 너희 친구를 조심하고 너희 형제를 함부로 믿지 말아라. 형제도 속이고 친구도 다니면서 비방한다.

5그들은 다 자기 친구를 속이며 진실을 말하지 않고 자기들의 혀에게 거짓말을 하라고 가르치며 악을 행하는 데 지칠 줄 모른다.

6너는 그들의 기만 가운데 살고 있다. 그들은 기만으로 나를 인정하려고 하지 않는다. 이것은 나 여호와의 말이다.”

7그러므로 전능하신 여호와께서 말씀하신다. “보라, 내가 내 백성을 시련의 도가니에 넣어 금속처럼 연단하고 시험하겠다. 이 밖에 내가 달리 무엇을 할 수 있겠는가?

8그들의 혀는 사람을 죽이는 화살과 같다. 그들은 항상 거짓을 말하고 입으로는 자기 이웃에게 다정히 말하면서도 마음속으로는 그를 잡을 덫을 놓고 있다.

9내가 이런 일을 보고서도 어찌 그들을 벌하지 않겠느냐? 어찌 내가 이런 나라에 보복하지 않겠느냐?”

10내가 산들을 위해 울고 부르짖으며 광야의 목장을 위해 슬퍼할 것이니 그것들이 황폐하므로 지나다니는 자가 없고 가축의 소리가 들리지 않으며 공중의 새와 짐승이 다 도망가고 없어졌기 때문이다.

11여호와께서 말씀하신다. “내가 예루살렘을 폐허의 무더기로 만들며 이리의 소굴이 되게 하고 유다 성들로 황폐하게 하여 사람이 살지 않게 하겠다.”

12지혜로워서 이 일을 깨달을 만한 자가 누구인가? 여호와의 말씀을 받아서 그것을 선포할 자가 누구인가? 어떻게 하다가 이 땅이 멸망하여 사막처럼 황폐해져서 지나다니는 자가 없게 되었는가?

13여호와께서 말씀하셨다. “이것은 내 백성들이 내가 준 법을 저버리고 나에게 복종하지 않으며 내 말대로 행하지 않고

14오히려 그 마음의 악한 고집을 따라 그들의 조상들이 가르친 바알 우상들을 섬겼기 때문이다.

15그러므로 전능한 여호와 이스라엘의 하나님 내가 말한다. 보라, 내가 이 백성에게 쑥을 먹이며 독물을 마시게 하고

16그들과 그 조상들이 알지 못하던 나라로 그들을 흩어 버리며 그들을 전멸시킬 때까지 칼로 그들을 추격할 것이다.”

17전능하신 여호와께서 말씀하신다. “너희는 생각해 보고 제일 잘 우는 여자들을 불러

18빨리 와서 너희를 위해 울게 하여 너희 눈에서 눈물이 쏟아지게 하라.

19너희는 시온에서 들려오는 통곡 소리를 들어 보아라. ‘우리는 망하였다! 우리가 크게 수치를 당하는구나. 우리 집들이 헐렸으니 우리 땅을 떠날 수밖에 없구나.’ ”

20부녀들아, 여호와의 말씀을 듣고 그의 말씀에 귀를 기울여라. 너희 딸들에게 곡하는 법을 가르치고 서로 애가를 가르쳐라.

21죽음이 우리 창문으로 기어들어오고 우리 궁전에 들어와서 거리에 있는 아이들과 광장에 있는 젊은이들의 생명을 끊어 버리려고 한다.

22“너는 나 여호와가 이렇게 말한다고 외쳐라. ‘사람의 시체가 똥처럼 들에 흩어져, 추수하는 자의 뒤에 떨어져도 거두어들일 자가 없는 곡식단처럼 될 것이다.’ ”

23여호와께서 말씀하신다. “지혜로운 자는 자기 지혜를 자랑하지 말고 강한 자는 자기 힘을 자랑하지 말며 부자는 자기의 부요함을 자랑하지 말아라.

24자랑하는 사람은 나를 이해하고 아는 것과 그리고 내가 자비를 베풀며 옳고 공정한 일을 행하는 여호와임을 아는 것으로 자랑하라. 나는 이런 것을 기뻐한다. 이것은 나 여호와의 말이다.”

25여호와께서 말씀하신다. “포피를 베어 할례를 받은 자나 받지 못한 자를 내가 다 벌할 날이 올 것이다.

26이들은 이집트, 유다, 에돔, 암몬, 모압 사람들과 그리고 옆 머리를 잘라내고 광야에서 사는 사람들이다. 이방 민족들은 할례를 받지 못하였고 이스라엘 민족은 마음의 할례를 받지 못하였다.”