Yeremiya 5 – CCL & KJV

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yeremiya 5:1-31

Palibe Munthu Wolungama

1“Pitani uku ndi uku mʼmisewu ya Yerusalemu,

mudzionere nokha,

funafunani mʼmabwalo ake.

Ngati mungapeze munthu mmodzi

amene amachita zachilungamo ndi kufunafuna choonadi,

ndipo ndidzakhululukira mzinda uno.

2Ngakhale anthu akulumbira kuti, ‘Pali Yehova wamoyo,’

komabe akungolumbira mwachinyengo.”

3Inu Yehova, kodi suja mumafuna anthu onena zoona?

Inu munawakantha anthuwo, koma sanamve kupweteka;

munawaphwanya anthuwo, koma sanatengepo phunziro.

Anawumitsa mitima yawo ngati mwala

ndipo anakaniratu kulapa.

4Ndiye ndinati, “Awa ndi amphawi chabe;

anthu ochita zopusa.

Sadziwa njira ya Yehova,

sazindikira zimene Mulungu wawo amafuna.

5Tsono ndidzapita kwa atsogoleri

ndi kukayankhula nawo;

ndithu iwo amadziwa njira ya Yehova,

amadziwa zomwe Mulungu wawo amafuna.”

Koma ayi, iwonso anathyola goli la Yehova

ndipo anadula msinga zawo.

6Choncho mkango wochokera ku nkhalango udzawapha,

mmbulu wochokera ku thengo udzawawononga,

kambuku adzawabisalira pafupi ndi mizinda yawo

kuti akhadzule aliyense amene adzayesera kutuluka mʼmizindamo

pakuti kuwukira kwawo ndi kwakukulu

ndipo abwerera mʼmbuyo kwambiri.

7Yehova akuti, “Kodi ndingakukhululukireni bwanji ndi zimene mwachita?

Ana anu andisiya Ine

ndipo amapembedza milungu imene si milungu konse.

Ine ndinawapatsa zonse zimene ankasowa,

komabe iwo anachita chigololo

namasonkhana ku nyumba za akazi achiwerewere.

8Monga amachitira akavalo onenepa akamamemesa,

aliyense wa iwo ankathamangira mkazi wa mnzake.

9Tsono ndingaleke kuwalanga chifukwa cha zimenezi?”

akutero Yehova.

“Kodi nʼkuleka kuwulipsira

mtundu woterewu?

10“Pitani ku minda yake ya mipesa ndi kukayiwononga,

koma musakayiwononge kotheratu.

Sadzani nthambi zake

pakuti anthu amenewa si a Yehova.

11Nyumba ya Israeli ndi nyumba ya Yuda

onse akhala osakhulupirika kotheratu kwa Ine.”

12Iwowa ankanama ponena za Yehova kuti,

“Yehova sangachite zimenezi!

Choyipa sichidzatigwera;

sitidzaona nkhondo kapena njala.

13Mawu a aneneri azidzangopita ngati mphepo;

ndipo mwa iwo mulibe uthenga wa Yehova.

Choncho zimene amanena zidzawachitikira okha.”

14Chifukwa chake Yehova Mulungu Wamphamvuzonse akuti,

“Popeza kuti anthu awa ayankhula mawu amenewa,

tsono mawu anga ndidzawasandutsa moto mʼkamwa mwako

ndipo anthu awa ndidzawasandutsa nkhuni zimene moto udzapserezeretu.

15Inu Aisraeli,” Yehova akuti,

“Ndikukubweretserani mtundu wa anthu ochokera kutali,

ndi mtundu umene sunagonjetsedwepo,

mtundu wakalekale umene chiyankhulo chawo inu simuchidziwa,

zimene akunena inu simungazimvetse.

16Zida zawo za nkhondo zapha anthu ambirimbiri;

onsewo ndi ankhondo amphamvu okhaokha.

17Adzakudyerani zokolola zanu ndi chakudya chanu,

adzapha ana anu aamuna ndi aakazi;

adzakupherani nkhosa zanu ndi ngʼombe zanu,

adzawononga mpesa wanu ndi mikuyu yanu.

Ndi malupanga awo adzagwetsa

mizinda yanu yotetezedwa imene mumayidalira.

18“Komabe pa masiku amenewo sindidzakuwonongani kotheratu,” akutero Yehova. 19Ndipo pamene anthu adzafunsa Yehova kuti, “Chifukwa chiyani Yehova Mulungu wathu wachita zimenezi?” Iwe udzawawuze kuti, “Monga momwe mwasiyira Ine ndi kutumikira milungu yachilendo mʼdziko mwanu, momwemonso mudzatumikira anthu a mʼdzikonso lachilendo.”

20“Lengeza izi kwa ana a Yakobo

ndipo mulalikire kwa anthu a ku Yuda kuti,

21Imvani izi, inu anthu opusa ndi opanda nzeru,

inu amene maso muli nawo koma simupenya,

amene makutu muli nawo koma simumva.

22Kodi simuyenera kuchita nane mantha?”

Akutero Yehova.

“Kodi simuyenera kunjenjemera pamaso panga?

Ine ndinayika mchenga kuti ukhale malire a nyanja,

malire a muyaya amene nyanjayo singadutsepo.

Mafunde angawombe motani, koma sangathe kupitirira malirewo;

mafunde angakokome motani, koma sangadutse malirewo.

23Koma anthu awa ndi nkhutukumve ndiponso a mitima yowukira;

andifulatira ndipo andisiyiratu.

24Sananenepo mʼmitima mwawo kuti,

‘Tiyeni tizipembedza Yehova Mulungu wathu.

Kodi suja amatipatsa pa nthawi yake mvula yachizimalupsa ndi yamasika.

Iye salephera konse kutipatsa nyengo ya kholola.’

25Koma zolakwa zanu zalepheretsa zonsezi;

ndipo machimo anu akumanitsani zabwino.

26“Pakati pa anthu anga pali anthu ena oyipa

amene amabisalira anzawo monga amachitira mlenje mbalame

ndiponso ngati amene amatchera misampha kuti akole anthu anzawo.

27Nyumba zawo zadzaza ndi chuma chochipeza mwa chinyengo

ngati zikwere zodzaza ndi mbalame.

Nʼchifukwa chake asanduka otchuka ndi olemera.

28Ndipo ananenepa ndi kukhala ndi matupi osalala.

Ntchito zawo zoyipa nʼzopanda malire;

saweruza mwachilungamo nkhani ya ana amasiye kuti iyende bwino,

sateteza ufulu wa anthu osauka.

29Kodi Ine ndingaleke kuwalanga chifukwa cha zimenezi?

Kodi ndisawulipsire

mtundu woterewu?

Akutero Yehova.

30“Chinthu chothetsa nzeru ndi choopsa kwambiri

chachitika mʼdzikomo:

31Aneneri akunenera zabodza,

ndipo ansembe akuvomerezana nawo,

ndipo anthu anga akukonda zimenezi.

Koma mudzatani potsiriza?

King James Version

Jeremiah 5:1-31

1Run ye to and fro through the streets of Jerusalem, and see now, and know, and seek in the broad places thereof, if ye can find a man, if there be any that executeth judgment, that seeketh the truth; and I will pardon it. 2And though they say, The LORD liveth; surely they swear falsely. 3O LORD, are not thine eyes upon the truth? thou hast stricken them, but they have not grieved; thou hast consumed them, but they have refused to receive correction: they have made their faces harder than a rock; they have refused to return. 4Therefore I said, Surely these are poor; they are foolish: for they know not the way of the LORD, nor the judgment of their God. 5I will get me unto the great men, and will speak unto them; for they have known the way of the LORD, and the judgment of their God: but these have altogether broken the yoke, and burst the bonds. 6Wherefore a lion out of the forest shall slay them, and a wolf of the evenings shall spoil them, a leopard shall watch over their cities: every one that goeth out thence shall be torn in pieces: because their transgressions are many, and their backslidings are increased.5.6 evenings: or, deserts5.6 are increased: Heb. are strong

7¶ How shall I pardon thee for this? thy children have forsaken me, and sworn by them that are no gods: when I had fed them to the full, they then committed adultery, and assembled themselves by troops in the harlots’ houses. 8They were as fed horses in the morning: every one neighed after his neighbour’s wife. 9Shall I not visit for these things? saith the LORD: and shall not my soul be avenged on such a nation as this?

10¶ Go ye up upon her walls, and destroy; but make not a full end: take away her battlements; for they are not the LORD’s. 11For the house of Israel and the house of Judah have dealt very treacherously against me, saith the LORD. 12They have belied the LORD, and said, It is not he; neither shall evil come upon us; neither shall we see sword nor famine: 13And the prophets shall become wind, and the word is not in them: thus shall it be done unto them. 14Wherefore thus saith the LORD God of hosts, Because ye speak this word, behold, I will make my words in thy mouth fire, and this people wood, and it shall devour them. 15Lo, I will bring a nation upon you from far, O house of Israel, saith the LORD: it is a mighty nation, it is an ancient nation, a nation whose language thou knowest not, neither understandest what they say. 16Their quiver is as an open sepulchre, they are all mighty men. 17And they shall eat up thine harvest, and thy bread, which thy sons and thy daughters should eat: they shall eat up thy flocks and thine herds: they shall eat up thy vines and thy fig trees: they shall impoverish thy fenced cities, wherein thou trustedst, with the sword. 18Nevertheless in those days, saith the LORD, I will not make a full end with you.

19¶ And it shall come to pass, when ye shall say, Wherefore doeth the LORD our God all these things unto us? then shalt thou answer them, Like as ye have forsaken me, and served strange gods in your land, so shall ye serve strangers in a land that is not yours.

20Declare this in the house of Jacob, and publish it in Judah, saying, 21Hear now this, O foolish people, and without understanding; which have eyes, and see not; which have ears, and hear not:5.21 understanding: Heb. heart 22Fear ye not me? saith the LORD: will ye not tremble at my presence, which have placed the sand for the bound of the sea by a perpetual decree, that it cannot pass it: and though the waves thereof toss themselves, yet can they not prevail; though they roar, yet can they not pass over it? 23But this people hath a revolting and a rebellious heart; they are revolted and gone. 24Neither say they in their heart, Let us now fear the LORD our God, that giveth rain, both the former and the latter, in his season: he reserveth unto us the appointed weeks of the harvest.

25¶ Your iniquities have turned away these things, and your sins have withholden good things from you. 26For among my people are found wicked men: they lay wait, as he that setteth snares; they set a trap, they catch men.5.26 they lay…: or, they pry as fowlers lie in wait 27As a cage is full of birds, so are their houses full of deceit: therefore they are become great, and waxen rich.5.27 cage: or, coop 28They are waxen fat, they shine: yea, they overpass the deeds of the wicked: they judge not the cause, the cause of the fatherless, yet they prosper; and the right of the needy do they not judge. 29Shall I not visit for these things? saith the LORD: shall not my soul be avenged on such a nation as this?

30¶ A wonderful and horrible thing is committed in the land;5.30 A wonderful…: or, Astonishment and filthiness 31The prophets prophesy falsely, and the priests bear rule by their means; and my people love to have it so: and what will ye do in the end thereof?5.31 bear…: or, take into their hands