Yeremiya 48 – CCL & HOF

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yeremiya 48:1-47

Uthenga Wonena za Mowabu

1Ponena za Mowabu:

Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli akuti,

“Tsoka kwa mzinda wa Nebo, chifukwa wawonongedwa.

Mzinda wa Kiriyataimu wachititsidwa manyazi ndipo wagonjetsedwa;

linga lichititsidwa manyazi ndipo lagumulidwa.

2Palibenso amene akutamanda Mowabu;

ku Hesiboni anthu anamupanganira zoyipa:

‘Bwerani, tiyeni timuwonongeretu kuti asakhalenso mtundu wa anthu.’

Inunso anthu a ku Madimena, adzakukhalitsani chete;

ankhondo adzakupirikitsani.

3Tamvani mfuwu wa anthu a ku Horonaimu.

Iwo akulira kuti, ‘Kusakazika ndi kuwonongeka kwakukulu.’

4Mowabu wawonongeka;

ana ake angʼonoangʼono akulira kwambiri.

5Anthu akukwera chikweza cha ku Luhiti,

akulira kwambiri pamene akupita.

Kulira chifukwa cha chiwonongeko kukumveka

pa njira yotsikira ku Horonaimu.

6Thawani! Dzipulumutseni;

khalani ngati mbidzi ya mʼchipululu.

7Popeza inu munkadalira ntchito zanu ndi chuma chanu,

nanunso mudzatengedwa ukapolo,

ndipo Kemosi adzapita ku ukapolo,

pamodzi ndi ansembe ake ndi akuluakulu ake.

8Wowononga adzabwera ndi kusakaza mzinda uliwonse,

ndipo palibe mzinda umene udzapulumuke.

Chigwa chidzasanduka bwinja

ndipo malo athyathyathya a pamwamba pa phiri adzawonongedwa

monga Yehova wayankhulira.

9Mtsineni khutu Mowabu

chifukwa adzasakazika;

mizinda yake idzasanduka mabwinja,

wopanda munthu wokhalamo.

10“Wotembereredwa munthu amene amagwira ntchito ya Yehova monyinyirika!

Wotembereredwa munthu amene amaletsa lupanga lake kupha anthu!

11“Mowabu wakhala pa mtendere kuyambira ubwana wake,

ngati vinyo wokhazikika pa masese ake,

osapungulidwa kuchoka mu mtsuko wina kuthira mu mtsuko wina;

iye sanatengedwepo ukapolo.

Nʼchifukwa chake kukoma kwake nʼkomwe kuja

ndipo fungo lake silinasinthe.

12Nʼchifukwa chake masiku akubwera,”

akutero Yehova,

“pamene ndidzatuma anthu amene amakhuthula vinyo mʼmitsuko

ndipo adzamukhutula;

adzakhuthula vinyo yense mitsuko yake

pambuyo pake nʼkuphwanya mitsukoyo.

13Pamenepo Mowabu adzachita manyazi ndi Kemosi,

monga momwe Aisraeli anachitira manyazi

ndi Beteli amene ankamukhutulira.

14“Kodi munganene bwanji kuti, ‘Ife ndife asilikali.

Ife ndife ngwazi, anthu amphamvu pa nkhondo?’

15Owononga Mowabu ndi mizinda yake abwera ndipo ankhondo adzalowa mʼmidzi yake;

anyamata ake okongola apita kukaphedwa,”

ikutero Mfumu, imene dzina lake ndi Yehova Wamphamvuzonse.

16Kugwa kwa Mowabu kuli pafupi;

masautso ake akubwera posachedwa.

17Mulireni kwambiri, inu nonse amene mwamuzungulira,

inu nonse amene mumadziwa za kutchuka kwake;

nenani kuti, “Taonani momwe yathyokera ndodo yamphamvu yaufumu ija,

taonani momwe ndodo yaulemu yathyokera!”

18“Tsikani pa ulemerero wanu

ndipo khalani pansi powuma,

inu anthu okhala ku Diboni,

pakuti wowononga Mowabu

wabwera kudzamenyana nanu,

wasakaza mizinda yanu yotetezedwa.

19Inu amene mumakhala ku Aroeri,

imani mʼmbali mwa msewu ndi kumaonerera.

Funsani mwamuna amene akuthawa ndiponso mkazi amene wapulumuka,

afunseni kuti, ‘Kodi chachitika nʼchiyani?’ ”

20Iwo adzayankha kuti, “Mowabu wachititsidwa manyazi, pakuti wasakazika.

Lirani mwachisoni ndipo fuwulani!

Lengezani ku mtsinje wa Arinoni

kuti Mowabu wawonongedwa.

21Chiweruzo chabwera ku mizinda ya ku mapiri,

ndiyo Holoni, Yaza, Mefaati,

22Diboni, Nebo, Beti-Dibilataimu,

23Kiriyataimu, Beti-Gamuli, Beti-Meoni,

24Keriyoti ndi Bozira

ndi mizinda yonse ya Mowabu, yakutali ndi yapafupi yomwe.

25Mphamvu za Mowabu zawonongeka;

mkono wake wathyoka,”

akutero Yehova.

26“Muledzeretseni Mowabu,

chifukwa anadzikuza powukira Yehova.

Mulekeni Mowabu avivinizike mʼmasanzi ake;

mulekeni akhale chinthu chomachiseka.

27Kodi suja Israeli anali kwa iwe ngati chinthu chomachiseka?

Kodi Israeli anapezeka pakati pa akuba

kuti nthawi zonse poyankhula za iye,

iwe uzimupukusira mutu momunyoza?

28Inu amene mumakhala ku Mowabu,

siyani mizinda yanu ndi kukakhala pakati pa matanthwe.

Khalani ngati nkhunda imene imamanga chisa chake

pa khomo la phanga.

29“Tamva za kunyada kwa Mowabu,

kunyada kwake nʼkwakukulu.

Ndi wodzitama, wonyada ndi wodzitukumula.

Ali ndi mtima wodzikweza.

30Ine ndikuzidziwa ntchito zake,

akutero Yehova.

Ntchitozo ndi nʼzosapindulitsa kanthu.

31Nʼchifukwa chake ndidzamulira Mowabu,

ine ndikulira chifukwa cha anthu onse a ku Mowabu,

ndikubuwula chifukwa cha anthu a ku Kiri Heresi.

32Ndikukhetsa misozi chifukwa cha inu, kupambana momwe ndinalirira Yazeri.

Inu anthu a ku Sibina muli ngati mipesa

imene nthambi zake zatambalala mpaka ku Nyanja;

zafika mpaka ku nyanja ya Yazeri.

Wowononga wasakaza

zipatso zake zachilimwe ndi mpesa.

33Chimwemwe ndi chisangalalo zatha

ku minda ya zipatso ya ku Mowabu.

Ndaletsa kuchucha kwa vinyo mopsinyira mphesa;

palibe amene akufuwula mokondwa akamapsinya mphesa.

Ngakhale kufuwula kulipo,

koma sikufuwula kwa chimwemwe.

34“A ku Hesiboni ndi Eleali akulira

ndipo mfuwu wawo ukumveka mpaka ku Yahazi,

kuchokera ku Zowari mpaka ku Horonaimu ndi ku Egilati Selisiya.

Ngakhale madzi a ku Nimurimu aphwa.

35Ndidzawaletsa anthu a ku Mowabu

kupereka nsembe mʼmalo awo opembedzera

ndi kufukiza lubani kwa milungu yawo,”

akutero Yehova.

36“Nʼchifukwa chake mtima wanga ukulirira Mowabu ngati chitoliro.

Mtima wanga ukulirira anthu a ku Kiri Heresi ngati chitoliro

chifukwa chuma chimene anachipata chatha.

37Aliyense wameta mutu wake

ndi ndevu zake;

manja a munthu aliyense ndi ochekacheka,

ndipo munthu aliyense wavala chiguduli mʼchiwuno mwake.

38Pa madenga onse a ku Mowabu

ndiponso mʼmisewu yake

anthu akungolira,

pakuti ndaphwanya Mowabu

ngati mtsuko wopanda ntchito,”

akutero Yehova.

39“Taonani mmene waphwanyikira! Tamvani momwe akulirira!

Taonani momwe Mowabu wachititsidwira manyazi.

Mowabu wasanduka chinthu chonyozeka,

chinthu chochititsa mantha kwa onse amene amuzungulira.”

40Yehova akuti,

“Mtundu wina udzachita kuwuluka nʼkugwera pa Mowabu ngati chiwombankhanga

chimene chatambalitsa mapiko ake.

41Mizinda idzagwidwa

ndipo malinga adzalandidwa.

Pa tsiku limenelo mitima ya ankhondo a ku Mowabu

idzakhala ngati mtima wa mayi pa nthawi yake yochira.

42Mowabu sudzakhala mtundu wa anthu

chifukwa unadzikuza powukira Yehova.

43Zoopsa, dzenje ndi msampha zikudikira

inu anthu a ku Mowabu,”

akutero Yehova.

44“Aliyense wothawa zoopsa

adzagwera mʼdzenje,

aliyense wotuluka mʼdzenje

adzakodwa mu msampha.

Ndigwetsa zimenezi pa Mowabu

pa nthawi ya chilango chake,”

akutero Yehova.

45“Anthu othawa nkhondo ayima pa mthunzi wa Hesiboni

chifukwa chotopa.

Koma moto wayaka kuchokera ku Hesiboni,

malawi a moto abuka kuchokera ku nyumba ya mfumu Sihoni.

Motowo ukuwononga mapiri a ku Mowabu,

dziko la anthu onyada.

46Tsoka kwa iwe Mowabu!

Anthu opembedza Kemosi awonongeka.

Ana ako aamuna ndi aakazi

atengedwa ukapolo.

47“Komabe masiku akutsogolo

ndidzabwezeranso Mowabu chuma chake,”

akutero Yehova.

Chiweruzo cha Mowabu chathera pamenepa.

Hoffnung für Alle

Jeremia 48:1-47

Moabs Untergang

1»So spricht der Herr, der allmächtige Gott Israels, über Moab:

Verloren ist die Stadt Nebo, sie liegt in Trümmern! Kirjatajim ist erobert worden, seine Bergfestung wurde niedergerissen. Nun hat man nur noch Verachtung für sie übrig. 2Moabs Ruhm ist dahin! In Heschbon haben die Feinde seinen Untergang geplant. ›Kommt und lasst uns die Moabiter ausrotten!‹, sagen sie. Auch du, Stadt Madmen, wirst vom Erdboden verschwinden! Der Feind wird dich überrollen.

3In Horonajim rufen sie schon: ›Unser Land ist verwüstet, alles liegt in Trümmern!‹ 4Ja, die Moabiter sind geschlagen. Hört ihr, wie ihre kleinen Kinder schreien? 5Weinend schleppen sich die Menschen den steilen Weg nach Luhit hinauf. Sie klagen laut über ihren Untergang, auf der Flucht nach Horonajim rufen sie: 6›Flieht! Lauft, so schnell ihr könnt! Kämpft in der Wüste ums Überleben!48,6 Wörtlich: Werdet wie ein Dornstrauch in der Wüste!

7Ihr Moabiter habt euch auf eure Stärke und euren Reichtum verlassen, und gerade darum wird euer Land jetzt erobert. Euren Gott Kemosch wird man in die Verbannung bringen, zusammen mit den Priestern und den führenden Männern. 8Der Feind zieht heran und verwüstet ganz Moab; keine Stadt bleibt verschont. Ob unten im Jordantal oder auf der Hochebene – alle trifft das gleiche Los, so wie ich, der Herr, es angekündigt habe. 9Gebt den Moabitern Flügel, denn sie werden Hals über Kopf fliehen müssen.48,9 Oder nach der griechischen Übersetzung: Setzt den Moabitern einen Grabstein, denn es ist aus mit ihnen. – Der hebräische Text ist nicht sicher zu deuten. Ihre Städte werden zu Ruinen, in denen keiner mehr wohnt.

10Verflucht sei, wer meinen Auftrag nachlässig ausführt! Verflucht sei, wer nicht zuschlägt und das Blut der Moabiter vergießt! 11Sie haben seit jeher in Sicherheit gelebt, nie mussten sie in Gefangenschaft ziehen. Sie gleichen einem Wein, der lange gelagert und nicht von einem Fass ins andere umgegossen wurde. So ist er in Ruhe ausgereift, sein Duft und sein Geschmack konnten sich voll entfalten. 12Doch hört: Es kommt die Zeit, in der ich, der Herr, den Moabitern Leute schicke, die den Wein ausschütten, die Fässer leeren und die Weinkrüge zerschlagen! 13Dann wird Moab von seinem Gott Kemosch bitter enttäuscht sein, so wie das Nordreich Israel enttäuscht wurde, als es auf seine Götzen in Bethel vertraute.

14Wie könnt ihr Moabiter nur prahlen: ›Wir sind Helden und kampferprobte Soldaten‹? 15Ich, der Herr, sage euch: Euer Land wird zur Wüste, bald sind eure Städte erobert! Eure Elitetruppen werden zur Schlachtbank geführt. Denn ich bin König der ganzen Welt; ›allmächtiger Gott‹ lautet mein Name.«

Moabs Macht ist gebrochen

16»Moabs Untergang steht kurz bevor, das Unheil lässt nicht mehr lange auf sich warten! 17Sprecht den Moabitern euer Beileid aus, ihr Nachbarvölker und alle, die ihr sie kennt! Klagt: ›Moabs Macht und Ruhm ist dahin! Sein Zepter ist zerbrochen!‹

18Ihr Einwohner von Dibon, steigt herab von eurem hohen Ross und setzt euch in den Staub! Denn der Feind, der Moab verwüstet, zieht auch gegen euch heran und zerstört eure Festungen! 19Stellt euch an die Straße und seht euch um, ihr Einwohner von Aroër! Fragt die Flüchtlinge und die Vertriebenen, was geschehen ist. 20›Moab ist erobert, Angst und Schrecken herrschen überall‹, klagen sie und fordern euch auf: ›Weint und schreit! Sagt den Leuten am Fluss Arnon, dass ihr Land verwüstet ist!‹

21Jetzt halte ich Gericht über die Städte auf der Hochebene: über Holon, Jahaz, Mefaat, 22Dibon, Nebo, Bet-Diblatajim, 23Kirjatajim, Bet-Gamul, Bet-Meon, 24Kerijot, Bozra und alle anderen moabitischen Städte nah und fern!

25Moab ist machtlos geworden, seine Kraft ist gebrochen!48,25 Wörtlich: Das Horn Moabs ist abgehauen, und sein Arm ist zerschmettert! – Das Horn und der Arm stehen sinnbildlich für Stärke und Kraft. 26Macht Moab betrunken, bis es sich in seinem Erbrochenen wälzt und selbst von allen verspottet wird, denn es hat mich, den Herrn, herausgefordert!

27Ihr Moabiter, ständig habt ihr euch über die Israeliten lustig gemacht. Ihr habt auf sie herabgesehen, als seien sie Diebe, die auf frischer Tat ertappt wurden. 28Verlasst eure Städte und haust in Höhlen, lebt wie die Tauben, die ihr Nest am Felsabhang bauen!«

29»Wir haben gehört, wie stolz und hochmütig die Moabiter sind. Eingebildet und selbstherrlich benehmen sie sich, hochtrabend und überheblich!«

30»Doch ich, der Herr, durchschaue ihre Prahlerei – es ist nichts als Geschwätz! Sie gaukeln anderen nur etwas vor. 31Darum klage ich laut über die Moabiter und ihr Land, ich trauere um die Einwohner von Kir-Heres. 32Mehr als über die Einwohner von Jaser weine ich über die Stadt Sibma. Sie war berühmt für ihren Wein, ihre Ranken erstreckten sich bis zum Toten Meer, bis nach Jaser. Doch dann fiel der Feind über ihre Weintrauben und ihre ganze Ernte her. 33In den Obstgärten und auf den Feldern von Moab singt und jubelt man nicht mehr. Ich habe dafür gesorgt, dass niemand mehr die Trauben presst, kein Wein fließt aus der Kelter. Man hört zwar lautes Rufen – aber Freudenschreie sind es nicht!

34In Heschbon rufen die Menschen verzweifelt um Hilfe, sie sind noch in Elale und Jahaz zu hören, und die Schreie in Zoar dringen bis Horonajim und Eglat-Schelischija. Selbst der Bach von Nimrim ist ausgetrocknet. 35Ich, der Herr, lasse es nicht mehr zu, dass man in Moab zu den Opferstätten hinaufsteigt, um dort den Göttern Opfer zu bringen. Alle, die dies tun, rotte ich aus!«

36Darüber bin ich tief erschüttert. Ich trauere um Moab und die Einwohner von Kir-Heres wie jemand, der ein Klagelied auf der Flöte spielt. Denn sie haben alles verloren, was sie erspart haben. 37Vor Kummer und Sorgen haben sich die Männer allesamt den Kopf kahl geschoren und den Bart abrasiert. Sie ritzen sich die Hände blutig und tragen Trauergewänder. 38Auf den Dächern der Häuser und auf den Straßen hört man lautes Klagen.

So spricht der Herr: »Ich habe Moab zerschmettert wie ein Tongefäß, das niemand haben will. 39Ja, Moab ist zerschlagen! Es schreit verzweifelt, vor Scham wendet es sich ab. Bei allen Nachbarvölkern ist es zum Gespött geworden, zum Bild des Schreckens!«

Moab hat den Herrn herausgefordert

40»So spricht der Herr: Seht, der Feind greift schon an, wie ein Adler mit ausgebreiteten Flügeln kreist er über Moab, 41er erobert die Städte und Festungen. Dann zittern die mutigen Soldaten vor Angst wie eine Frau in den Wehen! 42Ja, Moab wird ausgelöscht, es wird kein Volk mehr sein, denn es hat mich herausgefordert.

43Ich, der Herr, sage: Angst und Schrecken werden euch packen, in Fallgruben und Schlingen werdet ihr geraten, ihr Moabiter! 44Wer dem Schrecken entfliehen will, stürzt in die Grube, und wer sich daraus noch befreien kann, der verfängt sich in der Schlinge. Ja, es kommt das Jahr, in dem ich Gericht halte über Moab. Mein Wort gilt!

45Erschöpft suchen die Flüchtlinge Schutz in der Stadt Heschbon, wo König Sihon früher regierte. Doch von Heschbon geht ein Feuer aus, mitten aus der Stadt lodern die Flammen hervor. Sie versengen den Moabitern, diesen vorlauten Angebern, den Kopf. 46Wehe euch, ihr Moabiter! Euer Volk, das Kemosch verehrte, ist zugrunde gegangen. Denn eure Söhne und Töchter wurden in die Gefangenschaft verschleppt.

47Doch es kommt die Zeit, da werde ich euer Schicksal wieder zum Guten wenden. Darauf gebe ich, der Herr, mein Wort!«

Hier endet die Gerichtsbotschaft über Moab.