Yeremiya 47 – CCL & HOF

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yeremiya 47:1-7

Uthenga Wonena za Afilisti

1Uthenga umene Yehova anamupatsa mneneri Yeremiya wonena za Afilisti, Farao asanathire nkhondo Gaza ndi uwu:

2Yehova akuti,

“Taonani mmene madzi akubwerera kuchokera kumpoto;

adzasanduka mtsinje wosefukira ndi a mkokomo.

Adzasefukira mʼdziko monse ndi kumiza chilichonse mʼmenemo,

mizinda ndi onse okhala mʼmenemo.

Anthu adzafuwula;

anthu onse okhala mʼdzikomo adzalira

3akadzamva mgugu wa ngʼombe zazimuna zothamanga,

phokoso la magaleta ake

ndi kulira kwa mikombero yake.

Makolo sadzatembenuka kuti athandize ana awo;

manja awo adzangoti khoba.

4Pakuti tsiku lafika

lowononga Afilisti onse

ndi kupha onse otsala,

onse amene akanatha kuthandiza Turo ndi Sidoni.

Yehova ali pafupi kuwononga Afilisti,

otsala ochokera ku zilumba za ku Kafitori.

5Anthu a ku Gaza ameta mipala;

anthu a ku Asikeloni akhala chete.

Inu otsala a ku chigwa,

mudzakhala mukudzichekacheka mpaka liti?

6“Mukulira kuti, ‘Aa, lupanga la Yehova,

kodi udzapumula liti?

Bwerera mʼmalo ako;

ukhale momwemo ndipo ukhale chete.’

7Koma lupangalo lidzapumula bwanji

pamene Yehova walilamulira

kuti lithire nkhondo

Asikeloni ndi anthu a mʼmbali mwa nyanja?”

Hoffnung für Alle

Jeremia 47:1-7

Die Philister werden ausgerottet

1Ehe der Pharao die Stadt Gaza eroberte, empfing der Prophet Jeremia vom Herrn eine Botschaft für die Philister:

2»So spricht der Herr: Seht, aus dem Norden droht eine Flut; das Wasser wird zum reißenden Strom, der über die Ufer tritt. Er überschwemmt das Land und die Felder, er reißt Städte und Menschen mit fort. Die Bewohner rufen um Hilfe, im ganzen Land schreien sie laut! 3Denn sie hören Pferde galoppieren, Räder rasseln, Streitwagen herandonnern. Die Väter fliehen und sehen sich nicht mehr nach ihren Kindern um, die Angst hat sie gepackt! 4Der Tag ist gekommen, an dem das Land der Philister verwüstet wird; die letzten Verbündeten von Tyrus und Sidon werden ausgerottet. Ja, ich, der Herr, lösche die restlichen Philister aus, die einst von der Insel Kreta gekommen sind.

5Die Einwohner von Gaza sind verzweifelt und scheren sich den Kopf kahl, die Menschen in Aschkelon wurden alle umgebracht. Wie lange ritzt ihr euch vor Trauer die Haut blutig, ihr Nachkommen der Enakiter47,5 So nach der griechischen Übersetzung. Der hebräische Text lautet: ihr restlichen Bewohner der Talebene.? 6Ihr schreit: ›Ach, du Schwert des Herrn, wie lange willst du noch zustechen? Hör auf damit, kehr zurück in deine Scheide und lass uns endlich in Ruhe!‹ 7Doch wie kann das Schwert ruhen, wenn ich, der Herr, ihm einen Auftrag gegeben habe? Ich selbst habe ihm befohlen, Aschkelon und das Gebiet an der Küste zu zerstören!«