Yeremiya 45 – CCL & CCB

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yeremiya 45:1-5

Uthenga kwa Baruki

1Uwu ndi uthenga umene mneneri Yeremiya anawuza Baruki mwana wa Neriya mʼchaka cha chinayi cha Yehoyakimu mwana wa mwana ya Yosiya kuti alembe mʼbuku. 2“Yehova Mulungu wa Israeli, akunena kwa iwe Baruki kuti: 3Iwe unati, ‘Kalanga ine! Yehova wawonjezera chisoni pa mavuto anga. Ine ndatopa ndi kubuwula ndipo sindikupeza mpumulo.’ ”

4Koma Yehova akukuwuza kuti, “Ndidzagwetsa chimene ndinamanga ndipo ndidzazula chimene ndinadzala. Ndidzachita zimenezi mʼdziko lonse. 5Kodi tsono ukudzifunira wekha zinthu zazikulu? Usadzifunire. Pakuti ndidzagwetsa mavuto pa anthu onse, koma ndidzasunga moyo wako kulikonse kumene ungadzapite.”

Chinese Contemporary Bible (Simplified)

耶利米书 45:1-5

耶和华给巴录的信息

1犹大约西亚的儿子约雅敬执政第四年,尼利亚的儿子巴录耶利米口述的话写在书卷上。耶利米说: 2巴录啊,以色列的上帝耶和华说, 3‘你曾说,我真悲惨!因为耶和华使我痛上加痛,呻吟不止,身心疲惫,不得安宁。’ 4我要告诉你,耶和华说,‘我必在整个大地上拆毁我所建立的,铲除我所栽培的。 5你想为自己谋求大事吗?不要谋求,因为我要给世人降下灾祸。但不论你到哪里,我必使你保住性命。这是耶和华说的。’”