Yeremiya 3 – CCL & LCB

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yeremiya 3:1-25

1“Ngati munthu asudzula mkazi wake

ndipo mkaziyo nʼkuchoka nakakwatiwa ndi mwamuna wina,

kodi mwamuna woyambayo angathe kumutenganso mkaziyo?

Kodi atatero sindiye kuti dzikolo layipitsidwa kwambiri?

Koma iwe Israeli wachita zadama ndi zibwenzi zambiri.

Komabe bwerera kwa ine,”

akutero Yehova.

2“Tayangʼana ku zitunda zowuma.

Kodi aliponso malo ena amene iwe sunachitepo zadama?

Iwe unkakhala mʼmbali mwa njira kumadikira zibwenzi zako,

ngati Mluya wobisalira anthu mʼchipululu.

Inu mwayipitsa dziko ndi zadama zanu

ndi ntchito zanu zoyipa.

3Nʼchifukwa chake Yehova wayimitsa mvula,

ndipo mvula ya nthawi ya masika sinagwe.

Komabe uli ndi maonekedwe a mkazi wachiwerewere;

ndipo sukuchita manyazi ndi pangʼono pomwe.

4Kodi iwe siposachedwa pomwepa pamene wanena

kuti, ‘Abambo anga, Inu bwenzi langa la unyamata wanga,

5kodi mudzandikwiyira nthawi zonse?

Kodi ukali wanu udzakhalabe mpaka muyaya?’

Umu ndimo mmene umayankhulira,

koma umapitirizabe kuchita zoyipa monga momwe umathera.”

Kusakhulupirika kwa Israeli

6Pa nthawi ya Mfumu Yosiya Yehova anandiwuza kuti, “Kodi waona zomwe Israeli wosakhulupirika uja wachita? Anakwera pa phiri lililonse lalitali ndi kupita pa tsinde pa mtengo uliwonse wogudira kukapembedza. Choncho anachita za chiwerewere kumeneko. 7Ndinaganiza kuti atachita zonsezi, adzabwerera kwa Ine, koma sanabwerere, ndipo mlongo wake wosakhulupirika uja, Yuda, anaziona zimenezi. 8Anaona kuti ndinasudzula Israeli wosakhulupirikayo ndi kumupirikitsa chifukwa cha zigololo zake. Komabe Yuda mʼbale wake wosakhulupirika uja sanaope, nayenso anapita kukachita chigololo. 9Chiwerewere cha Israeli chinali chochititsa manyazi kotero kuti chinayipitsa dziko lonse. Anachita chigololo popembedza mafano a miyala ndi mitengo. 10Israeli atachita zonsezi, Yuda mʼbale wake wosakhulupirika uja sanabwerere kwa Ine ndi mtima wake wonse, koma mwachiphamaso chabe,” akutero Yehova.

11Yehova anandiwuza kuti, “Kusakhulupirika kwa Israeli nʼkochepa kuyerekeza ndi kusakhulupirika kwa Yuda. 12Pita ukalalikire kumpoto uthenga wakuti,

“ ‘Israeli wosakhulupirikawe, bwerera,’ akutero Yehova.

‘Sindidzakukalipira mpaka kalekale,

pakuti ndine wachifundo,’ akutero Yehova.

‘Sindidzakukwiyira mpaka kalekale.

13Ungovomera kulakwa kwako

kuti unawukira Yehova Mulungu wako.

Vomera kuti unayendayenda kukapembedza milungu yachilendo

pansi pa mtengo uliwonse wogudira,

ndiponso kuti sunandimvere,’ ”

akutero Yehova.

14“Bwererani, ana osakhulupirika, pakuti ndine mbuye wanu,” akutero Yehova. “Ndinakusankhani, mmodzimmodzi kuchokera ku mudzi uliwonse ndiponso awiriawiri kuchokera ku banja lililonse. 15Ndipo ndidzakupatsani abusa a pamtima panga amene adzakutsogolerani mwanzeru ndi mwaluntha. 16Masiku amenewo mukadzachulukana kwambiri mʼdzikomo, anthu sadzanenanso za ‘Bokosi la Chipangano la Yehova’ kapena kuliganizira. Sadzalikumbukiranso kapena kulifuna, ndipo sadzapanganso lina,”

akutero Yehova.

17Nthawi imeneyo adzatcha Yerusalemu Mpando Waufumu wa Yehova, ndipo mitundu yonse ya anthu idzasonkhana mu Yerusalemu pamaso pa Yehova. Sadzawumiriranso kutsata mitima yawo yoyipa. 18Masiku amenewo fuko la Yuda lidzaphatikizana ndi fuko la Israeli, onse pamodzi adzachokera ku dziko la kumpoto kupita ku dziko limene ndinapatsa makolo awo, kuti likhale cholowa.

19“Ine mwini ndinati,

“ ‘Ndikanakonda bwanji kukukhazikani pakati pa ana anga

ndikukupatsani dziko labwino kwambiri,

cholowa chokongola kwambiri kuposa cha mitundu ina ya anthu.’

Ndinaganiza kuti mudzanditcha Ine ‘Atate’

ndi kuti simudzaleka kunditsata.

20Koma monga mkazi wosakhulupirika amasiya mwamuna wake,

momwemonso inu mwakhala osakhulupirika kwa Ine, inu fuko la Israeli,”

akutero Yehova.

21Mawu akumveka pa magomo,

Aisraeli akulira ndi kupempha chifundo

chifukwa anatsata njira zoyipa

ndi kuyiwala Yehova Mulungu wawo.

22Inu mukuti, “Bwererani, anthu osakhulupirika;

ndidzachiritsa kubwerera mʼmbuyo kwanu.”

“Inde, tidzabwerera kwa Inu

pakuti ndinu Yehova Mulungu wathu.

23Ndithu kupembedza pa magomo

komanso kuchita maphwando pa mapiri zilibe phindu.

Zoonadi chipulumutso cha Israeli

chili mwa Yehova Mulungu wathu basi.

24Kuyambira pa ubwana wathu milungu yochititsa manyazi ija yakhala ikutiwonongetsa phindu

la ntchito za makolo athu,

nkhosa ndi ngʼombe zawo,

ana awo aamuna ndi aakazi.

25Tilekeni tigone pansi mwa manyazi,

ndipo kunyozeka kwathu kutiphimbe.

Paja tachimwira Yehova Mulungu wathu,

ife pamodzi ndi makolo athu

kuyambira nthawi ya ubwana wathu mpaka lero lino

sitinamvere Yehova Mulungu wathu.”

Luganda Contemporary Bible

Yeremiya 3:1-25

Yuda Omukazi Atali Mwesigwa

13:1 a Ma 24:1-4 b Yer 2:20, 25; Ez 16:26, 29“Omusajja bw’agoba mukazi we,

omukazi oyo n’agenda n’afuuka ow’omusajja omulala,

omusajja we alimukomyawo nate?

Ensi eba teyonoonekedde ddala nnyo?

Naye obadde nga malaaya, ng’olina abasajja bangi;

naye kaakano oyagala okukomawo gye ndi?”

bw’ayogera Mukama.

23:2 a Lub 38:14; Ez 16:25 b Yer 2:7Yimusa amaaso go olabe ku ntikko y’obusozi.

Waliwo ekifo we bateebakira naawe?

Ku mabbali g’ekkubo we watulanga

n’olinda abasajja ng’oli nga Omuwalabu mu ddungu;

n’olyoka oyonoona ensi

n’obwenzi bwo n’ekibi kyo.

33:3 a Lv 26:19 b Yer 14:4 c Yer 6:15; 8:12; Zef 3:5Noolwekyo enkuba kyevudde eziyizibwa,

n’enkuba eya ttoggo n’etetonnya.

Naye era otemya nga malaaya

tokwatibwa nsonyi.

43:4 a nny 19 b Yer 2:2Tewakaŋŋamba nti Kitange ggwe mukwano gwange

okuva mu buto bwange,

53:5 Zab 103:9; Is 57:16onoonyiigira ddala emirembe gyonna,

olisunguwala emirembe gyonna?

Bw’otyo bw’oyogera,

naye okoze ebibi byonna ebisoboka.

Isirayiri, Atali Mwesigwa

63:6 a Yer 17:2 b Yer 2:20Mu nnaku z’obufuzi bwa kabaka Yosiya Mukama yayogera nange n’aŋŋamba nti, “Olabye Isirayiri etali neesigwa ky’ekoze? Agenze ku buli kasozi na buli wansi w’omuti oguyimiridde ne yeeyisa ng’omukazi omwenzi. 73:7 Ez 16:46Nalowooza nti, Bw’alimala okukola bino byonna agenda kudda gye ndi naye teyadda, era muganda we atali mwesigwa Yuda n’akiraba. 83:8 Ez 16:47; 23:11Yalaba nti bwe namala okugoba Isirayiri eyanvaako, ne muwa n’ebbaluwa ey’okumugoba olw’obwenzi bwe. Naye ate ne ndaba muganda we atali mwesigwa Yuda nga taliimu kutya, naye n’agenda n’akola obwenzi. 93:9 a nny 2 b Is 57:6 c Yer 2:27Awo obwenzi bwe bwatuuka ne bumwanguyira nnyo n’ayenda n’asinza amayinja n’ebikonge. 103:10 Yer 12:2Naye wadde nga byonna bimaze okubaawo, muganda we Yuda atali mwesigwa, teyakomawo gye ndi na mutima gwe gwonna, naye yali alimbalimba,” bw’ayogera Mukama.

113:11 a Ez 16:52; 23:11 b nny 7Mukama n’aŋŋamba nti, Isirayiri asudde obwesigwa, mutukuvu okusinga Yuda atali mwesigwa. 123:12 a 2Bk 17:3-6 b nny 14; Yer 31:21, 22; Ez 33:11 c Zab 86:15Genda obuulire abantu b’omu bukiikakkono obubaka buno, obagambe nti,

“ ‘Komawo ggwe Isirayiri,

eyanvaako,’ bw’ayogera Mukama.

‘Siribatunuuliza busungu kubanga ndi waakisa,’ bw’ayogera Mukama;

‘Sirisiba busungu ku mwoyo emirembe gyonna.

133:13 a Ma 30:1-3; Yer 14:20; 1Yk 1:9 b Yer 2:25 c Ma 12:2 d nny 25Mukkirize bukkiriza ekibi kyammwe,

mwajeemera Mukama Katonda wammwe,

mwasinza bakatonda abalala,

wansi wa buli muti oguyimiridde,

era ne mutaŋŋondera,’ ”

bw’ayogera Mukama.

143:14 Kos 2:19“Mukomeewo mmwe abaana abanvaako,” bw’ayogera Mukama; “kubanga nze bbammwe, era ndibalondamu omu ku omu okuva mu buli kibuga, babiri babiri okuva mu buli kika mbaleete ku lusozi Sayuuni. 153:15 Bik 20:28Era ndibawa abasumba abakola ng’omutima gwange bwe gwagala, abalibakulembera mu kumanya era ne mu kutegeera. 163:16 Is 65:17Ennaku bwe zirituuka nga mwaze era nga muli bangi nnyo mu nsi,” bw’ayogera Mukama, “abantu baliba tebakyayogera ku Ssanduuko y’Endagaano. Baliba tebakyagirowooza nako, okugijjukira; oba okulumwa emitima olw’obutaba nayo wadde okukola endala. 173:17 a Yer 17:12; Ez 43:7 b Is 60:9 c Yer 11:8Ebbanga lyonna Yerusaalemi kiriyitibwa Entebe ya Mukama ey’Obwakabaka, amawanga gonna mwe ganaakuŋŋaaniranga okumugulumiza Mukama mu Yerusaalemi era tebaliddayo kugoberera mitima gyabwe minyoomi. 183:18 a Kos 1:11 b Is 11:13; Yer 50:4 c Yer 16:15; 31:8 d Am 9:15Mu nnaku ezo ennyumba ya Yuda eryegatta ku nnyumba ya Isirayiri, era bombi awamu baliva mu nsi ey’omu bukiikakkono ne bajja mu nsi gye ndiwa bakitammwe okuba omugabo.

193:19 nny 4; Is 63:16“Nze kennyini nalowooza

“nga nayagala okubayisanga nga batabani bange,

era mbawe ensi eyeegombebwa,

nga gwe mugabo ogusinga obulungi mu mawanga gonna.

Nalowooza nti mulimpita ‘Kitammwe,’

ne mutanvaako ne mwongera okungoberera.

20Naye ng’omukazi atali mwesigwa eri bba bw’abeera,

bwe mutyo bwe mutabadde beesigwa gye ndi, mmwe ennyumba ya Isirayiri,”

bw’ayogera Mukama.

Okuyitibwa Okwenenya

213:21 nny 2Okukaaba kw’Abaana ba Isirayiri

kuwuliddwa ku ntikko z’ensozi ezitaliiko kantu,

nga bakaaba n’okwegayirira, kubanga baatambulira mu kukola ebibi,

ne beerabira Mukama Katonda waabwe.

223:22 a Kos 14:4 b Yer 33:6; Kos 6:1“Mukomeewo mmwe abantu abatali beesigwa,

nnaabawonya ne mbafuula abeesigwa.”

Ne mugamba nti, “Weewaawo tujja kudda gy’oli,

kubanga ggwe Mukama Katonda waffe.

233:23 Zab 3:8; Yer 17:14Ddala okusuubira obuyambi okuva mu nsozi gye twasinzizanga bakatonda abalala

temuli kantu.

Ddala mu Mukama Katonda waffe

mwe muli obulokozi bwa Isirayiri.

243:24 Kos 9:10Naye okuva mu buto bwaffe

bakatonda abo abalala abatagasa balidde ne bamalawo ebibala

bakitaffe bye baamalirako amaanyi gaabwe, embuzi zaabwe, n’ente zaabwe,

batabani baabwe ne bawala baabwe.

253:25 a Ezr 9:6 b Yer 22:21Leka tugalamire, ng’ensonyi zitutta, n’obuswavu bwaffe butuyitiridde

kubanga twonoonye eri Mukama Katonda waffe, ffe ne bakadde baffe,

okuva mu buto bwaffe n’okutuusa ku lunaku luno;

kubanga tetugondedde ddoboozi lya Mukama Katonda waffe.”