Yeremiya 24 – CCL & CARST

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yeremiya 24:1-10

Madengu Awiri a Nkhuyu

1Nebukadinezara, mfumu ya ku Babuloni anatenga ukapolo Yekoniya mwana wa Yehoyakimu mfumu ya ku Yuda pamodzi ndi nduna zake, anthu aluso ndi akatswiri a ku Yuda ndi kupita nawo ku Babuloni. Pambuyo pake Yehova anandionetsa madengu awiri a nkhuyu atayikidwa pa khomo pa Nyumba ya Yehova. 2Mʼdengu limodzi munali nkhuyu zabwino kwambiri, ngati nkhuyu zoyambirira kucha. Mʼdengu linalo munali nkhuyu zoyipa kwambiri zosati nʼkudya.

3Yehova anandifunsa kuti, “Yeremiya, kodi ukuona chiyani?”

Ndinayankha kuti, “Ndikuona nkhuyu zabwino kwambiri ndi nkhuyu zoyipa zosati nʼkudya.”

4Tsono Yehova anandiwuza kuti, 5“Ine Yehova, Mulungu wa Israeli ndikuti, ‘Anthu a ku Yuda amene ndinawachotsa ku malo ano nʼkupita nawo ku ukapolo ku dziko la Ababuloni ndikuwafanizira ndi nkhuyu zabwinozi. 6Ndidzaonetsesa kuti ndiwachitire zabwino ndipo ndidzabwera nawonso ku dziko lino. Ndidzawamanga osati kuwapasula; ndidzawadzala osati kuwazula. 7Ndidzawapatsa mtima woti andidziwe kuti ndine Yehova. Adzakhala anthu anga ndipo Ine ndidzakhala Mulungu wawo, chifukwa adzabwerera kwa Ine ndi mtima wawo wonse.

8“ ‘Koma monga nkhuyu zoyipa zija, zomwe ndi zoyipa kwambiri zosati nʼkudya,’ Yehova akuti, ‘ndi mmene ndidzalangire Zedekiya mfumu ya ku Yuda, nduna zake pamodzi ndi otsala a mu Yerusalemu, kaya adzakhala ali mʼdziko muno kapena mʼdziko la Igupto. 9Ndidzawasandutsa chinthu chonyansa kwa maufumu onse a dziko lapansi, chinthu chonyozeka ndi chopandapake, chinthu chochitidwa chipongwe ndi chotembereredwa kulikonse kumene ndidzawabalalitsira. 10Ndidzawatumizira nkhondo, njala ndi mliri mpaka atawonongedwa mʼdziko limene ndinawapatsa iwo ndi makolo awo.’ ”

Священное Писание (Восточный перевод), версия для Таджикистана

Иеремия 24:1-10

Две корзины с инжиром

1После того как Навуходоносор, царь Вавилона, увёл в плен из Иерусалима в Вавилон иудейского царя Иехонию, сына Иоакима, с сановниками Иудеи, и с мастеровыми, и с кузнецами Иерусалима24:1 Это событие произошло в 597 г. до н. э. (см. 4 Цар. 24:10-17)., Вечный показал мне две корзины инжира, поставленные перед входом в храм Вечного. 2В одной корзине был отличный инжир раннего урожая; в другой корзине инжир был самый скверный, настолько плохой, что его нельзя было есть.

3И сказал мне Вечный:

– Что ты видишь, Иеремия?

Я ответил:

– Инжир. Хорошие плоды очень хороши, а плохие настолько испорчены, что их нельзя есть.

4И сказал мне Вечный:

5– Так говорит Вечный, Бог Исроила: Этим хорошим инжиром Я считаю изгнанников из Иудеи, высланных Мной из этой земли в землю вавилонян. 6Мои глаза будут обращены на них ради их же блага, и Я верну их на эту землю. Я утвержу их, а не разрушу; насажу, а не искореню. 7Я дам им сердце, способное познать Меня, познать, что Я – Вечный. Они будут Моим народом, а Я буду их Богом, потому что они вернутся ко Мне от чистого сердца.

8А этому скверному инжиру, который так плох, что его нельзя есть, – говорит Вечный, – Я уподоблю Цедекию, царя Иудеи, его приближённых и уцелевших горожан Иерусалима, независимо от того, останутся ли они в этой стране или поселятся в Египте. 9Я сделаю их ужасом и отвращением для всех царств на земле, позором и притчей, предметом издевательств и проклятий, повсюду, куда бы ни изгнал их. 10Я буду поражать их мечом, посылать на них голод и мор, пока они не исчезнут с земли, которую Я дал им и их предкам.