Yeremiya 18 – CCL & CCBT

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yeremiya 18:1-23

Ku Nyumba ya Wowumba Mbiya

1Yehova anawuza Yeremiya kuti, 2“Pita ku nyumba ya munthu wowumba mbiya, ndipo kumeneko ndikakuwuza mawu anga.” 3Choncho ndinatsikira ku nyumba ya wowumba mbiya, ndipo ndinamuona akuwumba mbiya pa mkombero. 4Tsono amati ngati mbiya imene waumba ikhala yosawumbika bwino ankayiphwanya nʼkuwumbanso ina monga mmene afunira ndi dothi lake lomwe lija.

5Kenaka Yehova anandiwuza kuti, 6“Inu Aisraeli, kodi Ine sindingathe kuchita nanu monga amachitira wowumba mbiya?” akutero Yehova. “Inu muli mʼmanja mwanga ngati mtapo mʼmanja mwa wowumba mbiya. 7Ngati nditalengeza kuti mtundu wina wa anthu kapena ufumu wina ndiwuzula, kuwugwetsa ndi kuwuwononga, 8ndipo ngati mtundu wa anthu umene ndawuchenjezawo ulapa zoyipa zawo, ndiye kuti Ine ndidzaleka ndipo sindidzabweretsa pa anthuwo mavuto amene ndinakonzekera kuwachitira. 9Ndipo ngati ndilengeza kuti ndikufuna kumanga ndi kukhazikitsa mtundu wa anthu kapena ufumu. 10Koma mtunduwo ukachita choyipa pamaso panga nʼkusandimvera, ndiye kuti sindidzawuchitiranso zabwino zimene ndimafuna ndiwuchitire.

11“Ndipo tsopano kawawuze anthu a ku Yuda ndi amene akukhala mu Yerusalemu kuti, ‘Yehova akuti, Taonani! Ndikukukonzerani mavuto, ndi kuganizira zoti ndikulangeni. Kotero siyani makhalidwe anu oyipa aliyense wa inu, ndipo mukonzenso makhalidwe anu ndi zochita zanu.’ 12Koma iwo adzayankha kuti, ‘Zimenezo nʼzosathandiza. Ife tidzapitiriza kuchita zomwe takonzekera; aliyense wa ife adzatsatira zoyipa za mtima wake wokanika.’ ”

13Yehova akuti,

“Uwafunse anthu a mitundu ina kuti:

Kodi ndani anamvapo zinthu zofanana ndi zimenezi?

Israeli amene anali ngati namwali wanga wachita

chinthu choopsa kwambiri.

14Kodi chisanu chimatha pa matanthwe

otsetsereka a phiri la Lebanoni?

Kodi madzi ozizira amitsinje ochokera

ku phiri la Lebanoni adzamphwa?

15Komatu anthu anga andiyiwala;

akufukiza lubani kwa mafano achabechabe.

Amapunthwa mʼnjira

zawo zakale.

Amayenda mʼnjira zachidule

ndi kusiya njira zabwino.

16Dziko lawo amalisandutsa chipululu,

chinthu chochititsa manyazi nthawi zonse;

onse odutsapo adzadabwa kwambiri

ndipo adzapukusa mitu yawo.

17Ngati mphepo yochokera kummawa,

ndidzawabalalitsa pamaso pa adani awo;

ndidzawafulatira osawathandiza

pa tsiku la mavuto awo.”

18Anthuwo anati, “Tiyeni, tipangane zoti timuchitire Yeremiya; pakuti ansembe otiphunzitsa malamulo tidzakhala nawobe. Anthu anzeru otilangiza tidzakhala nawo, ndiponso aneneri otilalikira mawu. Choncho tiyeni timupezere chifukwa ndipo tisamvere chilichonse chimene akunena.”

19Ndipo ndinapemphera kwa Yehova kuti, “Inu Yehova, ndimvereni;

imvani zimene adani anga akunena za ine!

20Kodi chinthu choyipa nʼkukhala dipo la chinthu chabwino?

Komabe iwo andikumbira dzenje.

Kumbukirani kuti ndinadzayima pamaso panu

kudzawapempherera

kuti muwachotsere mkwiyo wanu.

21Choncho langani ana awo ndi njala;

aperekeni kuti aphedwe ndi lupanga.

Akazi awo asanduke opanda ana ndi amasiye;

amuna awo aphedwe ndi mliri,

anyamata awo aphedwe ndi lupanga ku nkhondo.

22Kulira kumveke kuchokera mʼnyumba zawo

mutawatumizira gulu lankhondo mwadzidzidzi kuti liwakanthe.

Iwo andikumbira dzenje kuti ndigweremo

ndipo atchera msampha mapazi anga.

23Koma Inu Yehova, mukudziwa

ziwembu zawo zonse zofuna kundipha.

Musawakhululukire zolakwa zawo

kapena kufafaniza machimo awo pamaso panu.

Agonjetsedwe pamaso panu;

muwalange muli wokwiya.”

Chinese Contemporary Bible (Traditional)

耶利米書 18:1-23

陶器的比喻

1耶和華對耶利米說: 2「你去陶匠家,在那裡我有話告訴你。」 3我便到陶匠家,見他正用輪盤做器皿。 4每當他手中的器皿做壞了,他就用那塊泥重做,想怎麼做就怎麼做。 5這時,耶和華對我說: 6以色列人啊,難道我不能像陶匠對待陶泥一樣對待你們嗎?以色列人啊,你們在我手中就像陶泥在陶匠手中一樣。這是耶和華說的。 7當我宣佈要剷除、推翻、毀滅哪一邦或哪一國的時候, 8如果他們悔過自新,我必施憐憫,取消我原本要降給他們的災禍。 9當我宣佈要建造、栽培哪一邦或哪一國的時候, 10如果他們做我視為惡的事,不聽從我的話,我必改變心意,取消我原本要賜給他們的福氣。 11因此,你去告訴猶大人和耶路撒冷的居民,『耶和華說,我正計劃降災禍懲罰你們。你們要離開罪惡,改邪歸正。』 12他們卻說,『不!我們喜歡隨心所欲,為所欲為。』」

13因此耶和華說:

「你們問問列國,

看看誰曾聽過這樣的事?

少女般的以色列竟做了一件極可怕的事。

14黎巴嫩山嶺上的積雪會融化嗎?

從遠方流來的冰涼溪水會停止嗎?

15然而,我的子民卻把我拋諸腦後,

向虛無的神明燒香,

偏離古道,在歧途上絆絆跌跌。

16因此,他們的土地必荒涼,

永遠遭人嗤笑,

經過此地的人無不驚懼,

搖頭歎息。

17我要在敵人面前驅散他們,

就像東風吹散塵土一樣。

在他們遭難的時候,

我必以背相向,

不理睬他們。」

18他們說:「來!我們設計對付耶利米吧,反正我們有祭司教導律法,有智者出謀劃策,有先知傳講預言。來吧!我們抨擊他,不要理會他的話。」

19耶和華啊,求你眷顧我,

聽聽敵人對我的指控。

20人豈能以惡報善?

他們竟設陷阱謀害我,

求你回想我怎樣站在你面前為他們求情,

怎樣求你不要向他們發烈怒。

21因此,願他們喪身刀下,

兒女餓死,

妻子喪夫亡子,

年長的被殺,

年少的死於戰場!

22當你使敵軍突襲他們時,

願他們家中傳出哭喊聲,

因為他們挖陷阱要捕捉我,

設圈套要絆我的腳。

23耶和華啊,你知道他們害我的各種詭計,

求你不要赦免他們的罪過,

不要饒恕他們的惡行。

求你使他們倒在你面前,

求你在烈怒中懲罰他們。