Yeremiya 15 – CCL & NVI-PT

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yeremiya 15:1-21

1Kenaka Yehova anandiwuza kuti, “Ngakhale Mose ndi Samueli akanayima pamaso panga kupempherera anthu awa, Ine sindikanawachitira chisoni. Achotseni ndipo ndisawaonenso! Aleke apite! 2Ndipo ngati akufunsa iwe kuti, ‘Kodi tipite kuti?’ uwawuze kuti, ‘Yehova akuti,

“ ‘Oyenera kufa adzafa;

oyenera kufa ndi lupanga adzafa ndi lupanga;

oyenera kufa ndi njala adzafa ndi njala;

oyenera kupita ku ukapolo adzapita ku ukapolo.’

3“Ine ndidzawatumizira mitundu inayi ya zinthu zowononga,” akutero Yehova, “lupanga lowapha, agalu owaluma, mbalame zamumlengalenga ndiponso zirombo zoti ziwadye ndi kuwawononga. 4Ndidzawasandutsa kukhala chinthu chonyansa kwa anthu a maufumu onse a dziko lapansi chifukwa cha zimene Manase mwana wa Hezekiya mfumu ya Yuda anachita mu Yerusalemu.

5“Kodi adzakumvera chisoni ndani, Yerusalemu?

Kodi adzakulira ndani?

Kodi ndani amene adzapatuka kufunsa za moyo wako?

6Inu mwandikana Ine,” akutero Yehova.

“Inu mukubwererabe mʼmbuyo.

Choncho Ine ndidzakukanthani.

Ndatopa ndi kukuchitirani chifundo.

7Ine ndidzakubalalitsani kukuchotsani mʼmizinda ya mʼdzikomo

monga mmene amachitira ndi mankhusu popeta ndi lichero.

Anthu anga ndinawaliritsa ndi kuwawononga

chifukwa sanasinthe makhalidwe awo oyipa.

8Ndinachulukitsa amayi awo amasiye

kupambana mchenga wa kunyanja.

Amayiwo ndinawawonongera ana awo aamuna

dzuwa lili pamutu.

Mwadzidzidzi ndinawagwetsera

kuwawa mtima ndi mantha.

9Mayi wa ana asanu ndi awiri wakomoka

ndipo akupuma wefuwefu.

Dzuwa lake lalowa ukanali usana;

anamuchititsa manyazi ndipo wathedwa nzeru.

Otsala ndidzawapereka mʼmanja mwa adani awo

kuti awaphe ndi lupanga,”

akutero Yehova.

10Kalanga ine, amayi pakuti munandibereka ine,

munthu amene ndikutsutsana ndi kulimbana ndi anthu pa dziko lonse!

Ine sindinakongoze kapena kukongola kanthu,

komatu aliyense akunditemberera.

11Yehova anati,

“Ndithudi, Ine ndidzakulanditsa kuti upeze bwino.

Ndithudi, adani ako adzakupempha pa nthawi ya tsoka

ndi ya mavuto awo.

12“Palibe munthu amene angathe kudula chitsulo,

makamaka chitsulo chochokera kumpoto chosakaniza ndi mkuwa.

13Anthu ako ndi chuma chako

ndidzazipereka kwa ofunkha popanda malipiro,

chifukwa cha machimo anu onse

a mʼdziko lanu lonse.

14Ndidzakusandutsani akapolo a adani anu

mʼdziko limene inu simulidziwa,

chifukwa mkwiyo wanga wayaka ngati moto

umene udzakutenthani.”

15Ine ndinati, “Inu Yehova, mumadziwa zonse;

kumbukireni ndi kundisamalira.

Ndilipsireni anthu ondizunza.

Ndilezereni mtima musandilande moyo wanga.

Onani momwe ndi kuvutikira chifukwa cha Inu.

16Munandiyankhula ndipo mawu anu ndinawalandira bwino.

Mawu anu anandipatsa chimwemwe ndipo mtima wanga unasangalala.

Paja ine, Yehova Mulungu Wamphamvuzonse,

ndimadziwika ndi dzina lanu.

17Sindinakhale nawo mʼgulu la anthu amadyera,

sindinasangalale nawo anthu amenewo.

Ndinakhala ndekha chifukwa choti dzanja lanu linali pa ine

ndipo munadzaza mu mtima mwanga ndi mkwiyo.

18Nanga nʼchifukwa chiyani mavuto anga sakutha?

Bwanji chilonda changa sichikupola?

Kodi inu mudzakhala ngati mtsinje wowuma nthawi yachilimwe,

kapena ngati kasupe wopanda madzi?”

19Tsono Yehova anandiyankha kuti,

“Ukabwerera kwa Ine, ndidzakulandiranso

ndipo udzakhalanso mtumiki wanga.

Ngati udzayankhula mawu oyenera osati achabechabe,

udzakhalanso mneneri wanga.

Anthu adzabwera kwa iwe

ndipo sipadzafunika kuti iwe upite kwa iwo.

20Ndidzakusandutsa ngati khoma lolimba

ngati mkuwa kwa anthu awa.

Adzalimbana nawe

koma sadzakugonjetsa,

pakuti Ine ndili nawe

kukulanditsa ndi kukupulumutsa,”

akutero Yehova.

21“Ndidzakupulumutsa mʼdzanja la anthu oyipa

ndipo ndidzakuwombola kwa anthu ankhanza.”

Nova Versão Internacional

Jeremias 15:1-21

1Então o Senhor me disse: “Ainda que Moisés e Samuel estivessem diante de mim, intercedendo por este povo, eu não lhes mostraria favor. Expulse-os da minha presença! Que saiam! 2E, se perguntarem a você: ‘Para onde iremos?’, diga-lhes: Assim diz o Senhor:

“Os destinados à morte, para a morte;

os destinados à espada, para a espada;

os destinados à fome, para a fome;

os destinados ao cativeiro, para o cativeiro.

3“Enviarei quatro tipos de destruidores contra eles”, declara o Senhor: “a espada para matar, os cães para dilacerar, as aves do céu e os animais selvagens para devorar e destruir. 4Eu farei deles uma causa de terror para todas as nações da terra, por tudo o que Manassés, filho de Ezequias, rei de Judá, fez em Jerusalém.

5“Quem terá compaixão de você, ó Jerusalém?

Quem se lamentará por você?

Quem vai parar e perguntar como você está?

6Você me rejeitou”, diz o Senhor.

“Você vive se desviando.

Por isso, porei as mãos em você e a destruirei;

cansei-me de mostrar compaixão.

7Eu os espalhei ao vento

como palha nas cidades desta terra.

Deixei-os sem filhos; destruí o meu povo,

pois não se converteram de seus caminhos.

8Fiz com que as suas viúvas se tornassem mais numerosas

do que a areia do mar.

Ao meio-dia, trouxe um destruidor

contra as mães dos jovens guerreiros;

fiz cair sobre elas

repentina angústia e pavor.

9A mãe de sete filhos desmaiou

e está ofegante.

Para ela o sol se pôs enquanto ainda era dia;

ela foi envergonhada e humilhada.

Entregarei os sobreviventes à espada

diante dos seus inimigos”,

declara o Senhor.

10Ai de mim, minha mãe, por me haver dado à luz!

Pois sou um homem em luta e em contenda com a terra toda!

Nunca emprestei nem tomei emprestado,

e assim mesmo todos me amaldiçoam.

11O Senhor disse:

“Eu certamente o fortaleci para o bem e intervim por você,

na época da desgraça e da adversidade,

por causa do inimigo.15.11 A Septuaginta diz Certamente, Senhor, eu te servi fielmente e te busquei na época da desgraça e da adversidade, para o bem de meu inimigo.

12“Será alguém capaz de quebrar o ferro,

o ferro que vem do norte, ou o bronze?

13“Diga a esse povo:

Darei de graça a sua riqueza

e os seus tesouros como despojo,

por causa de todos os seus pecados

em toda a sua terra.

14Eu os tornarei escravos de seus inimigos,

numa terra15.14 Conforme alguns manuscritos do Texto Massorético, a Septuaginta e a Versão Siríaca. A maioria dos manuscritos do Texto Massorético diz Eu farei com que os seus inimigos o levem a uma terra. Veja Jr 17.4. que vocês não conhecem,

pois a minha ira acenderá um fogo

que arderá contra vocês”.

15Tu me conheces, Senhor;

lembra-te de mim, vem em meu auxílio

e vinga-me dos meus perseguidores.

Que, pela tua paciência para com eles,

eu não seja eliminado.

Sabes que sofro afronta por tua causa.

16Quando as tuas palavras foram encontradas, eu as comi;

elas são a minha alegria e o meu júbilo,

pois pertenço a ti15.16 Hebraico: pois teu nome foi invocado sobre mim., Senhor Deus dos Exércitos.

17Jamais me sentei na companhia dos que se divertem,

nunca festejei com eles.

Sentei-me sozinho,

porque a tua mão estava sobre mim

e me encheste de indignação.

18Por que é permanente a minha dor,

e a minha ferida é grave e incurável?

Por que te tornaste para mim como um riacho seco,

cujos mananciais falham?

19Assim respondeu o Senhor:

“Se você se arrepender, eu o restaurarei

para que possa me servir;

se você disser palavras de valor, e não indignas,

será o meu porta-voz.

Deixe este povo voltar-se para você,

mas não se volte para eles.

20Eu farei de você uma muralha de bronze fortificada diante deste povo;

lutarão contra você, mas não o vencerão,

pois estou com você para resgatá-lo e salvá-lo”,

declara o Senhor.

21“Eu o livrarei das mãos dos ímpios

e o resgatarei das garras dos violentos”.