Yesaya 1 – CCL & NVI-PT

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yesaya 1:1-31

1Masomphenya wonena za Yuda ndi Yerusalemu, amene Yesaya mwana wa Amozi, anaona pa nthawi ya ulamuliro wa Uziya, Yotamu, Ahazi ndi Hezekiya, mafumu a Yuda.

Anthu Owukira

2Tamverani, miyamba inu! Tchera khutu, iwe dziko lapansi!

Pakuti Yehova wanena kuti,

“Ndinabala ana ndi kuwalera,

koma anawo andiwukira Ine.

3Ngʼombe imadziwa mwini wake,

bulu amadziwa kumene kuli gome la mbuye wake,

koma Israeli sadziwa,

anthu anga samvetsa konse.”

4Haa, mtundu wochimwa,

anthu olemedwa ndi machimo,

obadwa kwa anthu ochita zoyipa,

ana odzipereka ku zoyipa!

Iwo asiya Yehova;

anyoza Woyerayo wa Israeli

ndipo afulatira Iyeyo.

5Chifukwa chiyani mukufuna kuti muzingolangidwabe?

Chifukwa chiyani mukupitirira kukhala mʼmoyo wowukira?

Mutu wanu wonse uli ndi mabala,

mtima wanu wonse wafowokeratu.

6Kuchokera ku phazi mpaka ku mutu

palibe pabwino,

paliponse pali mikwingwirima ndi zilonda,

mabala ali magazi chuchuchu,

mabala ake ngosatsuka, ngosamanga

ndiponso ngosapaka mafuta ofewetsa.

7Dziko lanu lasanduka bwinja,

mizinda yanu yatenthedwa ndi moto;

minda yanu ikukololedwa ndi alendo

inu muli pomwepo,

dziko lanu lasanduka bwinja monga ngati lagonjetsedwa ndi alendo.

8Mwana wamkazi wa Ziyoni watsala yekha

ngati nsanja mʼmunda wampesa,

ngati chisimba mʼmunda wa minkhaka,

ngati mzinda wozingidwa ndi nkhondo.

9Yehova Wamphamvuzonse akanapanda

kutisiyira opulumuka,

tikanawonongeka ngati Sodomu,

tikanakhala ngati anthu a ku Gomora.

10Imvani mawu a Yehova,

inu olamulira Sodomu;

mverani lamulo la Mulungu wathu,

inu anthu a ku Gomora!

11Yehova akuti, “Kodi ndili nazo chiyani

nsembe zanu zochuluka?”

“Zandikola nsembe zanu zopsereza

za nkhosa zazimuna ndiponso mafuta a nyama zonenepa;

sindikusangalatsidwanso

ndi magazi angʼombe zamphongo ndi a ana ankhosa ndi ambuzi zazimuna.

12Ndani anakulamulirani kuti

mubwere nazo pamaso panga?

Ndani anakuwuzani kuti muzipondaponda mʼmabwalo a nyumba yanga?

13Siyani kubweretsa nsembe zachabechabezo!

Nsembe zanu zofukiza zimandinyansa Ine.

Sindingapirire misonkhano yanu yoyipa,

kapenanso zikondwerero za Mwezi Watsopano ndi Masabata.

14Zikondwerero zanu za Mwezi Watsopano ndi masiku anu opatulika

ndimadana nazo.

Zasanduka katundu wondilemera;

ndatopa kuzinyamula.

15Mukamatambasula manja anu popemphera,

Ine sindidzakuyangʼanani;

ngakhale muchulukitse mapemphero anu,

sindidzakumverani.

Manja anu ndi odzaza ndi magazi;

16sambani, dziyeretseni.

Chotsani pamaso panu

ntchito zanu zoyipa!

Lekani kuchita zoyipa,

17phunzirani kuchita zabwino!

Funafunani chilungamo,

thandizani oponderezedwa.

Tetezani ana amasiye,

muwayimirire akazi amasiye pa milandu yawo.”

18Yehova akuti,

“Tiyeni tsono tikambe mlandu wanu.

Ngakhale machimo anu ali ofiira,

adzayera ngati thonje.

Ngakhale ali ofiira ngati kapezi,

adzayera ngati ubweya wankhosa.

19Ngati muli okonzeka kundimvera

mudzadya zinthu zabwino za mʼdziko;

20koma mukakana ndi kuwukira

mudzaphedwa ndi lupanga.”

Pakuti Yehova wayankhula.

21Taonani momwe mzinda wokhulupirika

wasandukira wadama!

Mzinda umene kale unali wodzaza ndi chiweruzo cholungama;

mu mzindamo munali chilungamo,

koma tsopano muli anthu opha anzawo!

22Siliva wako wasanduka wachabechabe,

vinyo wako wabwino wasungunulidwa ndi madzi.

23Atsogoleri ako ndi owukira,

anthu ogwirizana ndi mbala;

onse amakonda ziphuphu

ndipo amathamangira mphatso.

Iwo sateteza ana amasiye;

ndipo samvera madandawulo a akazi amasiye.

24Nʼchifukwa chake Ambuye Yehova Wamphamvu,

Wamphamvuyo wa Israeli, akunena kuti,

“Haa, odana nane ndidzawatha,

ndipo ndidzawabwezera ndekha adani anga.

25Ndidzatambasula dzanja langa kuti ndilimbane nawe;

ndidzasungunula machimo ako nʼkuwachotsa,

monga mmene amachotsera dzimbiri ndi mankhwala.

26Ndidzabwezeretsa oweruza ako ngati masiku amakedzana,

aphungu ako ndidzawabwezeretsa ngati poyamba paja.

Kenaka iweyo udzatchedwa

mzinda wolungama,

mzinda wokhulupirika.”

27Ziyoni adzawomboledwa mwa chiweruzo cholungama,

anthu ake olapadi adzapulumutsidwa mwachilungamo.

28Koma owukira ndi ochimwa adzawawonongera pamodzi,

ndipo amene asiya Yehova adzatheratu.

29“Mudzachita nayo manyazi mitengo ya thundu

imene inkakusangalatsani;

mudzagwetsa nkhope chifukwa cha minda

imene munayipatula.

30Mudzakhala ngati mtengo wa thundu umene masamba ake akufota,

mudzakhala ngati munda wopanda madzi.

31Munthu wamphamvu adzasanduka ngati udzu wowuma,

ndipo ntchito zake zidzakhala ngati mbaliwali;

motero zonse zidzayakira limodzi,

popanda woti azimitse motowo.”

Nova Versão Internacional

Isaías 1:1-31

1Visão que Isaías, filho de Amoz, teve a respeito de Judá e Jerusalém durante os reinados de Uzias, Jotão, Acaz e Ezequias, reis de Judá.

Uma Nação Rebelde

2Ouçam, ó céus! Escute, ó terra!

Pois o Senhor falou:

“Criei filhos e os fiz crescer,

mas eles se revoltaram contra mim.

3O boi reconhece o seu dono,

e o jumento conhece a manjedoura do seu proprietário,

mas Israel nada sabe,

o meu povo nada compreende”.

4Ah, nação pecadora,

povo carregado de iniquidade!

Raça de malfeitores,

filhos dados à corrupção!

Abandonaram o Senhor,

desprezaram o Santo de Israel e o rejeitaram.

5Por que haveriam de continuar a ser castigados?

Por que insistem na revolta?

A cabeça toda está ferida,

todo o coração está sofrendo.

6Da sola do pé ao alto da cabeça não há nada são;

somente machucados,

vergões e ferimentos abertos,

que não foram limpos nem enfaixados

nem tratados com azeite.

7A terra de vocês está devastada,

suas cidades foram destruídas a fogo;

os seus campos estão sendo tomados

por estrangeiros diante de vocês

e devastados como a ruína

que eles costumam causar.

8Só restou a cidade1.8 Hebraico: filha. de Sião

como tenda numa vinha,

como abrigo numa plantação de melões,

como uma cidade sitiada.

9Se o Senhor dos Exércitos

não tivesse poupado alguns de nós,

já estaríamos como Sodoma

e semelhantes a Gomorra.

10Governantes de Sodoma,

ouçam a palavra do Senhor!

Vocês, povo de Gomorra,

escutem a instrução de nosso Deus!

11“Para que me oferecem tantos sacrifícios?”,

pergunta o Senhor.

“Para mim, chega de holocaustos1.11 Isto é, sacrifícios totalmente queimados. de carneiros

e da gordura de novilhos gordos.

Não tenho nenhum prazer

no sangue de novilhos, de cordeiros e de bodes!

12Quando vocês vêm à minha presença,

quem pediu que pusessem os pés em meus átrios?

13Parem de trazer ofertas inúteis!

O incenso de vocês é repugnante para mim.

Luas novas, sábados e reuniões!

Não consigo suportar suas assembleias

cheias de iniquidade.

14Suas festas da lua nova

e suas festas fixas, eu as odeio.

Tornaram-se um fardo para mim;

não as suporto mais!

15Quando vocês estenderem as mãos em oração,

esconderei de vocês os meus olhos;

mesmo que multipliquem as suas orações,

não as escutarei!

“As suas mãos estão cheias de sangue!

16Lavem-se! Limpem-se!

Removam suas más obras para longe da minha vista!

Parem de fazer o mal,

17aprendam a fazer o bem!

Busquem a justiça,

acabem com a opressão.1.17 Ou repreendam o opressor.

Lutem pelos direitos do órfão,

defendam a causa da viúva.

18“Venham, vamos refletir juntos”,

diz o Senhor.

“Embora os seus pecados

sejam vermelhos como escarlate,

eles se tornarão brancos como a neve;

embora sejam rubros como púrpura,

como a lã se tornarão.

19Se vocês estiverem dispostos a obedecer,

comerão os melhores frutos desta terra;

20mas, se resistirem e se rebelarem,

serão devorados pela espada.”

Pois o Senhor é quem fala!

21Vejam como a cidade fiel

se tornou prostituta!

Antes cheia de justiça e habitada pela retidão,

agora está cheia de assassinos!

22Sua prata tornou-se escória,

seu licor ficou aguado.

23Seus líderes são rebeldes,

amigos de ladrões;

todos eles amam o suborno

e andam atrás de presentes.

Eles não defendem os direitos do órfão,

e não tomam conhecimento da causa da viúva.

24Por isso o Soberano, o Senhor dos Exércitos,

o Poderoso de Israel, anuncia:

“Ah! Derramarei minha ira sobre os meus adversários

e me vingarei dos meus inimigos.

25Voltarei minha mão contra você;

tirarei toda a sua escória

e removerei todas as suas impurezas.

26Restaurarei os seus juízes como no passado;

os seus conselheiros, como no princípio.

Depois disso você será chamada

cidade de retidão, cidade fiel”.

27Sião será redimida com justiça,

com retidão os que se arrependerem.

28Mas os rebeldes e os pecadores serão destruídos,

e os que abandonam o Senhor perecerão.

29“Vocês se envergonharão dos carvalhos sagrados

que tanto apreciam;

ficarão decepcionados

com os jardins sagrados que escolheram.

30Vocês serão como um terebinto

cujas folhas estão caindo,

como um jardim sem água.

31O poderoso se tornará como estopa,

e sua obra como fagulha;

ambos serão queimados juntos

sem que ninguém apague o fogo”.