Yeremiya 12 – CCL & CCBT

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yeremiya 12:1-17

Madandawulo a Yeremiya

1Yehova, Inu mumakhala wokhoza nthawi zonse

ndikati nditsutsane nanu.

Komabe ndikufuna kuyankhula nanu za mlandu wanga.

Chifukwa chiyani anthu oyipa zinthu zimawayendera bwino?

Chifukwa chiyani anthu achinyengo amakhala pabwino?

2Inu munawadzala ndipo anamera mizu;

amakula ndi kubereka zipatso.

Dzina lanu limakhala pakamwa pawo nthawi zonse,

koma mitima yawo imakhala kutali ndi Inu.

3Koma Inu Yehova, ine mumandidziwa;

mumandiona ndipo mumayesa zolingalira zanga.

Akokeni anthu oyipawo ngati nkhosa zokaphedwa!

Ayikeni padera mpaka tsiku loti akaphedwe!

4Kodi dziko lidzakhala likulirabe mpaka liti

ndipo udzu mʼmunda uliwonse udzakhalabe ofota mpaka liti?

Nyama ndi mbalame kulibiretu

chifukwa anthu amene amakhalamo ndi oyipa.

Iwo amati:

“Yehova sangathe kuona ntchito zathu.”

Yankho la Mulungu

5Yehova anayankha kuti, “Ngati kukutopetsa kuthamanga pamodzi ndi anthu

nanga ungapikisane bwanji ndi akavalo?

Ngati ukupunthwa ndi kugwa pa malo abwino,

udzatha bwanji kuthamanga mʼnkhalango

za ku Yorodani?

6Ngakhale abale ako

ndi anansi akuwukira,

onsewo amvana zokuyimba mlandu.

Usawakhulupirire,

ngakhale ayankhule zabwino ndi iwe.

7“Ine ndawasiya anthu anga;

anthu amene ndinawasankha ndawataya.

Ndapereka okondedwa anga

mʼmanja mwa adani awo.

8Anthu amene ndinawasankha

asanduka ngati mkango wa mʼnkhalango.

Akundibangulira mwaukali;

nʼchifukwa chake Ine ndikudana nawo.

9Anthu anga amene ndinawasankha

asanduka ngati mbalame yolusa yamawangamawanga

imene akabawi ayizinga.

Pitani, kasonkhanitseni nyama zakuthengo.

Mubwere nazo kuti zidzadye mbalameyo.

10Abusa ambiri anawononga munda wanga wa mpesa,

anapondereza munda wanga;

munda wanga wabwino uja

anawusandutsa chipululu.

11Unawusandutsadi chipululu.

Ukanali wokhawokha chomwecho ukundilirira Ine.

Dziko lonse lasanduka chipululu

chifukwa palibe wolisamalira.

12Anthu onse owononga abalalikira

ku zitunda zonse za mʼchipululu.

Yehova watuma ankhondo ake

kudzawatha kuyambira kumalire ena a dziko mpaka ku malire enanso a dziko,

ndipo palibe amene adzakhale pa mtendere.

13Anthu anafesa tirigu koma anatuta minga;

anadzitopetsa kugwira ntchito koma osapeza phindu lililonse.

Choncho mudzachita manyazi ndi zokolola zanu

chifukwa cha mkwiyo wa Yehova.”

14“Anthu oyipa oyandikana ndi anthu anga Aisraeli, akuwalanda Aisraeliwo dziko, cholowa chimene ndinawapatsa. Nʼchifukwa chake ndidzawachotsa mʼdziko limenelo, ndipo ndidzachotsa banja la Yuda pakati pawo. 15Komabe nditawachotsa, ndidzawachitiranso chifundo, ndipo ndidzabwezera aliyense cholowa chake ndi dziko lake. 16Ndipo ngati iwo adzaphunzira bwino njira za anthu anga ndi kulumbira mʼdzina langa, namanena kuti, ‘Pali Yehova wamoyo,’ monga iwo anaphunzitsira anthu anga kulumbira mʼdzina la Baala, Ine ndidzawakhazikitsa pakati pa anthu anga. 17Koma ngati mtundu wina uliwonse sudzamvera, Ine ndidzawuchotsa ndi kuwuwonongeratu,” akutero Yehova.

Chinese Contemporary Bible (Traditional)

耶利米書 12:1-17

耶利米的抱怨

1耶和華啊,每次我與你爭論,

都顯明你是對的。

然而,我還是對你的公正有所不解:

為什麼惡人總是得勢?

為什麼詭詐之人反而生活安逸?

2你栽培他們,讓他們生根長大,

結出果實。

他們嘴上尊崇你,

心卻遠離你。

3但耶和華啊,你認識我,瞭解我,

察驗我的內心。

求你拖走他們,

就像拖走待宰的羊,

留到宰殺之日。

4大地哀慟、

田野的植物枯槁要到何時呢?

由於這地方居民的罪惡,

野獸和飛鳥都滅絕了。

他們說:「上帝看不見我們的行為12·4 上帝看不見我們的行為」參照《七十士譯本》,希伯來文也可譯作「他(指耶利米)看不見我們的結局」。。」

5耶和華說:「如果你與步行的人競走,

尚且感到疲乏,

又怎能與馬賽跑呢?

如果你在寬闊之地尚且跌倒,

約旦河邊的叢林中又會怎樣呢?

6你的弟兄和家人都背叛了你,

與你作對。

任他們甜言蜜語,你不要相信。

7「我已離開我的殿,

撇棄我的產業,

把我愛的子民交給他們的敵人。

8我的子民像林中的獅子一樣向我吼叫,

因此我憎惡他們;

9我的子民就像一隻帶斑點的鷙鳥,

被其他鷙鳥圍攻。

招聚野獸來吞吃牠吧!

10列國的首領毀壞我的葡萄園,

踐踏我美好的土地,

使它荒涼;

11他們使這片土地荒涼,

以致它在我面前哀哭。

遍地如此荒涼,卻無人在意。

12殺戮者已來到曠野中光禿的山嶺,

耶和華使刀劍橫掃全境,

無人倖免。

13我的子民播種麥子,

卻收割荊棘;

辛勤耕耘,卻一無所獲。

他們必因耶和華的烈怒而收穫羞辱。」

14耶和華說:「邪惡的鄰國侵佔了我賜給我以色列子民的土地,我要把這些惡鄰逐出他們的本土,正如我要逐出猶大一樣。 15我逐出他們以後,還要再憐憫他們,把他們帶回各自的家園和故土。 16如果他們真心接受我子民的信仰,憑永活的耶和華之名起誓,正如他們教導我子民向巴力起誓一樣,他們便能成為我的子民。 17如果哪一國不聽我的話,我必把它連根拔起,徹底毀滅。這是耶和華說的。」