Oweruza 21 – CCL & NRT

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Oweruza 21:1-25

Akazi a Abenjamini

1Aisraeli anali atalumbira ku Mizipa kuti, “Palibe mmodzi wa ife adzapereke mwana wake wamkazi kuti akwatiwe ndi mwamuna wa fuko la Benjamini.”

2Anthu anapita ku Beteli kumene anakakhala pansi pamaso pa Mulungu mpaka madzulo. Iwo anakweza mawu nalira kwambiri. 3Iwo ankanena kuti, “Yehova Mulungu wa Israeli, nʼchifukwa chiyani izi zachitika mʼdziko la Israeli kuti lero fuko limodzi lisowe mu Israeli?”

4Mmawa mwake anthu anadzuka namanga guwa lansembe ndi kupereka nsembe zopsereza ndi nsembe zachiyanjano.

5Kenaka Aisraeli anafunsa kuti, “Kodi ndani pakati pa mafuko a Israeli sanafike ku msonkhano wa Yehova?” Anatero chifukwa anachita malumbiro aakulu okhudza munthu amene alephere kupita ku Mizipa ndi kuti woteroyo ayenera kuphedwa.

6Tsono Aisraeli anamva chisoni chifukwa cha abale awo, Abenjamini. Iwo anati, “Lero fuko limodzi lachotsedwa mu Israeli. 7Kodi tingawapezere bwanji anthu otsalawa akazi woti awakwatire? Paja ife tinalumbira kwa Yehova kuti sitidzapereka ana anthu aakazi kuti awakwatire. 8Kenaka anafunsa kuti, ‘Kodi mu fuko la Israeli ndani amene sanabwere pamaso pa Yehova ku Mizipa?’ ” Tsono panapezeka kuti panalibe ndi mmodzi yemwe wochokera ku Yabesi Giliyadi amene anapita ku msonkhano ku misasa kuja. 9Pamene anthu anawerengana anangoona kuti anthu a ku Yabesi Giliyadi palibe.

10Choncho msonkhano unatumiza anthu ankhondo 12,000 ndi kuwalamula kuti, “Mukaphe anthu onse okhala ku Yabesi Giliyadi, kuphatikizapo akazi ndi ana.” 11Izi ndi zimene mukachite. “Mukaphe mwamuna aliyense ndi mkazi aliyense amene anadziwapo mwamuna.” 12Iwo anapeza atsikana 400 pakati pa anthu okhala mu Yabesi Giliyadi amene anali asanadziwepo mwamuna ndipo anabwera nawo ku misasa ku Silo mʼdziko la Kanaani.

13Kenaka msonkhano wonse unatumiza uthenga kwa Abenjamini amene ankakhala ku thanthwe la Rimoni kuwawuza kuti nkhondo yatha. 14Choncho Abenjamini anabwera nthawi imeneyo ndipo Aisraeli anawapatsa akazi a ku Yabesi Giliyadi amene sanaphedwe. Koma sanapezeke owakwanira.

15Aisraeli anamvera chisoni Abenjamini, chifukwa Yehova anachita ngati waligwerula dzino fuko la Israeli. 16Choncho akuluakulu a msonkhano anati, “Kodi tikawapezera kuti akazi anthu otsalirawa kuti awakwatire popeza kuti akazi a fuko la Benjamini anaphedwa?” 17Iwo anati, “Abenjamini amene anapulumukawa ayenera kukhala ndi zidzukulu, kuti mtundu wa Israeli usafafanizike. 18Ife sitingathe kuwapatsa ana anthu aakazi kuti akwatire. Paja tinalumbira kuti, ‘Akhale wotembereredwa aliyense amene adzapereka mwana wake wamkazi kwa mwamuna wa fuko la Benjamini kuti akwatire.’ 19Ndipo anati, ‘Paja ku Silo kuli chikondwerero cha chaka ndi chaka cholemekeza Yehova. Tsono Silo ali kumpoto kwa Beteli, kummawa kwa msewu wochokera ku Beteli kupita ku Sekemu, ndiponso kummwera kwa Lebona.’ ”

20Choncho anawalamulira Abenjamini aja kuti, “Pitani mukabisale mʼminda ya mpesa 21ndipo mukakhale tcheru. Ana aakazi a ku Silo akadzatulukira kudzavina nawo magule, pomwepo inu mutuluke minda ya mpesa ndi kukawagwira aliyense wake ndi kupita nawo ku dziko la Benjamini. 22Ngati abambo awo kapena alongo awo adzabwera kudzadandaula kwa ife, tidzawawuza kuti, ‘Chonde, tikomereni mtima powalola kuti atenga ana anu aakaziwo popeza kuti ife sitinawapezere akazi pomenya nkhondo. Inunso simunachite kuwapatsa. Mukanatero ndiye mukanapalamula.’ ”

23Abenjamini anachitadi zimenezi. Mwa akazi amene ankavina aja anagwirapo ena, malingana ndi chiwerengero chawo, nawatenga kuti akhale akazi awo. Kenaka ananyamuka kubwerera ku dziko la kwawo, nakamanganso mizinda yawo ndi kumakhalamo.

24Pambuyo pake Aisraeli anachoka kumeneko ndi kubwerera kwawo, ku mafuko ndi ku mabanja awo, aliyense ku dera la cholowa chake.

25Masiku amenewo kunalibe mfumu ku Israeli. Aliyense ankangochita zimene zomukomera yekha.

New Russian Translation

Судей 21:1-25

Жены для вениамитян

1Израильтяне поклялись в Мицпе:

– Никто из нас не отдаст свою дочь замуж за вениамитянина.

2Народ пошел в Вефиль, где и сидели перед Богом до вечера, громко и горько плача.

3– О Господь, Бог Израиля, – говорили они, – почему это случилось с Израилем? Почему сегодня у Израиля недостает одного рода?

4На следующее утро, встав рано, народ построил там жертвенник и принес на нем всесожжения и жертвы примирения.

5И израильтяне спросили:

– Какой из всех родов Израиля не пришел на собрание перед Господом?

Они дали великую клятву, что всякий, кто не придет на собрание перед Господом в Мицпу, непременно будет предан смерти.

6Израильтяне горевали о своих братьях вениамитянах.

– Сегодня от Израиля отсечен один род, – говорили они. – 7Где нам взять жен для тех, кто уцелел, раз мы поклялись Господом не отдавать им в жены наших дочерей?

8Затем они спросили:

– Какой из израильских родов не пришел на собрание перед Господом в Мицпу?

Выяснилось, что в лагерь на собрание не пришел никто из Иавеша, что в Галааде; 9и когда они пересчитали народ, там не оказалось ни одного из жителей Иавеша, что в Галааде.

10И тогда общество отправило туда двенадцать тысяч воинов, велев им:

– Идите, предайте мечу всех жителей Иавеша, что в Галааде, вместе с женщинами и детьми. 11Сделайте вот что: полностью истребите21:11 На языке оригинала стоит слово, которое говорит о полном посвящении предметов или людей Господу, часто осуществлявшемся через их уничтожение. всех мужчин и всех женщин, кроме девственниц.

12Среди жителей Иавеша Галаадского они нашли четыреста девушек, которые еще не спали с мужчиной, и увели их в лагерь в Шило, что в земле Ханаана.

13Все общество послало вениамитянам к скале Риммон предложение заключить мир. 14Тогда вениамитяне вернулись, и им дали женщин Иавеша, что в Галааде, которых оставили в живых. Но на всех не хватило.

15Народ горевал о Вениамине, потому что Господь не сохранил целостности родов Израиля. 16И старейшины общества сказали:

– Женщины Вениамина истреблены. Как нам добыть жен для мужчин, которые уцелели? 17У уцелевших вениамитян должны быть наследники, – сказали они, – чтобы Израиль не потерял один из своих родов. 18Мы не можем дать им в жены своих дочерей, ведь мы, израильтяне, поклялись: «Проклят всякий, кто даст жену вениамитянину». 19Но смотрите, праздник Господу21:19 Возможно, здесь говорится об одном из праздников, установленных в Законе (см. Исх. 23:14-17), или же о каком-то местном празднике урожая винограда. ежегодно празднуется в Шило, что на севере от Вефиля и на востоке от дороги, что ведет от Вефиля в Шехем и на юг от Левоны.

20И они научили вениамитян, говоря:

– Идите, спрячьтесь в виноградниках 21и наблюдайте. Когда девушки Шило выйдут, чтобы кружиться в плясках, выбегайте из виноградников, хватайте каждый себе в жены одну из девушек Шило и ступайте в землю Вениамина. 22Когда их отцы или братья станут жаловаться нам, мы им скажем: «Будьте великодушны и оставьте их нам, потому что мы не взяли для них жен на войне, а раз не вы сами отдали их нам, то и вы не виновны».

23Так вениамитяне и поступили. Когда девушки плясали, каждый мужчина схватил по одной и унес, чтобы она стала его женой. После этого они вернулись в свой удел, отстроили города и поселились в них.

24А израильтяне тогда же покинули то место и пошли домой к своим родам и кланам, каждый – в свой удел.

25В те дни у Израиля не было царя, и каждый делал то, что считал правильным.