Oweruza 16 – CCL & TNCV

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Oweruza 16:1-31

Samsoni ndi Delila

1Tsiku lina Samsoni anapita ku Gaza. Kumeneko anaonako mkazi wachiwerewere, ndipo analowa mu nyumba yake. 2Anthu a ku Gaza anawuzidwa kuti, “Samsoni ali kuno!” Choncho anthuwo anazungulira malowo, kumubisalira usiku wonse ku chipata cha mzindawo. Iwo anakhala chete usiku wonse namanena kuti, “Tidzamupha mmamawa.”

3Koma Samsoni anangogonako mpaka pakati pa usiku. Kenaka pakati pa usiku anadzuka nagwira zitseko za chipata cha mzinda ndi maferemu ake awiri, ndipo anazizula zonse pamodzi ndi mpiringidzo womwe. Anazisenza pa mapewa pake napita nazo pamwamba pa phiri loyangʼanana ndi Hebroni.

4Pambuyo pake, Samsoni anayamba kukonda mtsikana wina wa ku chigwa cha Soreki dzina lake Delila. 5Olamulira Afilisti anapita kwa mkaziyo ndipo anati, “Umunyengerere Samsoni kuti udziwe chinsinsi cha mphamvu zake zoopsazi, komanso ndi mmene ife tingamupambanire kuti timumange ndi kumugonjetsa. Ukatero aliyense wa ife adzakupatsa ndalama zasiliva 1,100.”

6Choncho Delila anati kwa Samsoni, “Inu tandiwuzani pamene pagona mphamvu zanu zoopsazi ndi mmene anthu akhoza kukumangirani kuti akugonjetseni.”

7Samsoni anamuyankha kuti, “Ngati wina atandimanga ndi zingwe zisanu ndi ziwiri zatsopano zosawuma, ndidzafowoka ndi kusanduka ngati munthu wina aliyense.”

8Tsono atsogoleri a Afilisti aja anapita kwa mkazi uja namupatsa zingwe zisanu ndi ziwiri zatsopano zosawuma, ndipo mkaziyo anamanga nazo Samsoni. 9Nthawi imeneyo nʼkuti mkazi uja atayika anthu omubisalira mʼchipinda. Tsono anati kwa mwamuna wake, “Amuna anga, Afilisti aja afika!” Koma iye anangodula zingwe zija ngati mmene imadukira nkhosi ya chingwe ikamapsa. Choncho chinsinsi cha mphamvu zake sichinadziwike.

10Kenaka Delila anati kwa Samsoni, “Inu mwandipusitsa ndi kundiwuza zabodza. Chonde tandiwuzani mmene munthu angakumangireni.”

11Iye anati, “Ngati aliyense atandimanga ine ndi zingwe zatsopano zimene sanazigwiritseko ntchito, ndidzasanduka wofowoka ndi kukhala monga munthu wina aliyense.”

12Choncho Delila anatenga zingwe zatsopano namumanga nazo. Kenaka anati “Amuna anga, Afilisti aja afikanso!” Nthawi iyi nʼkuti anthu omubisalira aja ali mʼchipinda chamʼkati. Koma iye anadulanso zingwe mʼmanja ake ngati akudula ulusi wa thonje.

13Ndipo Delila anati kwa Samsoni, “Mpaka tsopano mwakhala mukundipusitsa ndi kumandiwuza zabodza. Chonde, tandiwuzani mmene munthu angakumangireni.”

Iye anayankha kuti, “Ngati njombi zisanu ndi ziwiri za kumutu kwanga utazilukira mu cholukira nsalu ndi kuchimanga molimbika ndi chikhomo, ndidzasanduka wofowoka ndi kukhala wofanana ndi munthu wina aliyense.” 14Choncho iye akugona, Delila analukira njombi za ku mutu kwa Samsoni mu cholukira nsalu nachimanga molimba ndi chikhomo.

Pambuyo pake anati kwa Samsoni, “Amuna anga, Afilisti aja abwera!” Tsono iye anadzuka ku tulo, nazula chikhomo chija ndipo njombi zinachoka mu cholukira chija.

15Tsono mkaziyo ananenanso kwa iye kuti, “Munganene bwanji kuti mumandikonda pamene mtima wanu suli pa ine? Aka ndi kachitatu mukundipusitsa ndipo simunandiwuze pamene pagona mphamvu zanu zoopsazi.” 16Tsono popeza anamupanikiza ndi mawu ake tsiku ndi tsiku ndi kumukakamiza, mtima wa Samsoni unatopa pafupi kufa.

17Choncho anamuwuza mkaziyo zonse za mu mtima mwake nati “Lumo silinapitepo pa mutu wanga chifukwa ndakhala ndili Mnaziri wopatulikira Mulungu chibadwire. Ngati nditametedwa mphamvu zanga zidzandichokera, ndidzasanduka wofowoka ndipo ndidzafanana ndi munthu wina aliyense.”

18Delila ataona kuti wamuwuza zonse za mu mtima mwake anatumiza uthenga kukayitana akuluakulu a Afilisti nati, “Bweraninso kamodzi kano kokha popeza wandiwululira zonse za mu mtima mwake.” Choncho akuluakulu a Afilisti aja anabwera ndi ndalama za siliva mʼmanja mwawo. 19Mkazi uja anagoneka Samsoni pa miyendo yake. Kenaka anayitana munthu wina ndipo anadzameta Samsoni njombi zisanu ndi ziwiri zija kumutu kwake. Pamenepo anayamba kufowoka, ndipo mphamvu zake zinamuchokera.

20Pambuyo pake mkaziyo anamuyitana kuti, “Amuna anga, Afilisti aja abwera!”

Iye anadzuka kutuloko, naganiza kuti, “Ndituluka monga ndimachitira nthawi zonse ndi kudzimasula.” Koma sanadziwe kuti Yehova wamuchokera.

21Afilisti anamugwira ndipo anamukolowola maso. Kenaka anapita naye ku Gaza atamumanga ndi maunyolo achitsulo. Kumeneko anakhala wa pamphero mu ndende. 22Pambuyo pake tsitsi la pa mutu wake, monga linametedwa, linayambanso kumera.

Imfa ya Samsoni

23Tsono atsogoleri a Afilisti anasonkhana kuti adzapereke nsembe yayikulu kwa Dagoni mulungu wawo ndi kukondwerera popeza ankanena kuti, “Mulungu wathu wapereka Samsoni mdani wathu mʼmanja mwathu.”

24Anthuwo atamuona Samsoni, anayamba kutamanda mulungu wawo popeza ankanena kuti,

“Mulungu wathu wapereka mdani wathu

mʼmanja mwathu,

ndiye amene anawononga dziko lathu,

napha anthu athu ambirimbiri.”

25Ali mʼkati mosangalala, anthu aja amafuwula kuti, “Mutulutseni Samsoniyo kuti adzatisangalatse.” Choncho anamutulutsadi Samsoni mʼndende, ndipo anawasangalatsadi.

Ndipo anamuyimiritsa pakati pa mizati. 26Pambuyo pake Samsoni anawuza mnyamata amene anamugwira dzanja kuti, “Ndilole kuti ndikhudze mizati imene yachirikiza nyumba yonseyi kuti ndiyitsamire.” 27Nthawi imeneyi nʼkuti nyumbayo ili yodzaza ndi anthu aamuna ndi aakazi. Olamulira onse a Afilisti anali momwemo, ndipo pamwamba pa nyumbayo panali anthu 3,000 aamuna ndi aakazi amene amaonerera Samsoni akusewera. 28Tsono Samsoni anapemphera kwa Yehova kuti, “Inu Yehova Ambuye anga, ndikumbukireni. Chonde ndilimbitseni nthawi yokha ino, inu Yehova, kuti ndiwabwezere Afilistiwa chifukwa cha maso anga awiri.” 29Choncho Samsoni anagwira mizati iwiri yapakati imene inkachirikiza nyumbayo. Anayitsamira ndi mphamvu zake zonse, dzanja lake lamanja ku mzati wina ndi dzanja lamanzere ku mzati winanso, 30ndipo Samsoni anati, “Ndife nawo pamodzi!” Nthawi yomweyo anakankha ndi mphamvu zake zonse ndipo mizati inagwera atsogoleri a Afilisti ndi anthu onse anali mʼmenemo. Tsono chiwerengero cha anthu amene Samsoni anapha pa nthawi ya imfa yake chinaposa cha iwo amene anawapha akanali ndi moyo.

31Kenaka abale ake ndi onse a pa banja la abambo ake anapita kukamutenga. Ndipo anakamuyika pakati pa Zora ndi Esitaoli mʼmanda a abambo ake, Manowa. Iye anatsogolera Israeli kwa zaka makumi awiri.

Thai New Contemporary Bible

ผู้วินิจฉัย 16:1-31

แซมสันกับเดลิลาห์

1วันหนึ่งแซมสันไปที่กาซาและพบหญิงโสเภณีคนหนึ่งที่นั่น เขาจึงไปนอนกับนาง 2เมื่อชาวเมืองกาซาได้ยินว่า “แซมสันอยู่ที่นี่!” พวกเขาจึงล้อมที่แห่งนั้นไว้และซุ่มอยู่ที่ประตูเมืองตลอดคืน พวกเขาคบคิดกันเงียบๆ ว่า “พอฟ้าสาง เราจะฆ่าเขา”

3แต่แซมสันนอนอยู่ที่นั่นจนถึงเที่ยงคืน แล้วลุกขึ้นออกไปที่ประตูเมือง ยกประตูเมืองขึ้นมา ดึงเสาประตูทั้งสองข้างพร้อมทั้งดาลประตูหลุดลอยจากพื้น แล้วแบกประตูไปจนถึงยอดเนินเขาที่หันหน้าไปทางเฮโบรน

4ต่อมาแซมสันหลงรักสาวคนหนึ่งชื่อเดลิลาห์ ซึ่งอาศัยอยู่ที่หุบเขาโสเรก 5เหล่าเจ้านายฟีลิสเตียไปพบหญิงนั้นและบอกนางว่า “เจ้าจงล้วงความลับของแซมสันว่ากำลังอันมหาศาลของเขามาจากไหน และทำอย่างไรพวกเราจึงจะสามารถปราบและจับกุมตัวเขาไว้ได้ แล้วพวกเราแต่ละคนจะให้เงินหนัก 1,100 เชเขล16:5 1 เชเขล คือเงินหนักประมาณ 11.5 กรัม มีค่าเท่ากับค่าแรงสองเดือนแก่เจ้า”

6ดังนั้นเดลิลาห์จึงกล่าวกับแซมสันว่า “โปรดบอกความลับที่ทำให้ท่านมีพลังมหาศาลอย่างนี้ ทำอย่างไรจึงจะมัดและคุมตัวท่านไว้ได้”

7แซมสันตอบว่า “ถ้าใช้สายธนูที่หนังยังไม่แห้งเจ็ดเส้นมัดตัวข้า ข้าก็จะอ่อนแอเหมือนคนอื่น”

8ฉะนั้นเจ้านายฟีลิสเตียจึงเอาสายธนูที่หนังยังไม่แห้งเจ็ดเส้นมาให้เดลิลาห์ นางก็เอาสายธนูมัดแซมสัน 9เดลิลาห์ให้คนซุ่มอยู่ในอีกห้องหนึ่ง แล้วนางก็ร้องว่า “แซมสัน พวกฟีลิสเตียมาจับท่านแล้ว!” แซมสันก็สะบัดสายธนูขาดอย่างง่ายดายเหมือนเชือกที่ถูกไฟลน ดังนั้นความลับของเขาเรื่องพละกำลังจึงยังไม่ถูกเปิดเผย

10แล้วเดลิลาห์กล่าวกับแซมสันว่า “ท่านโกหกหลอกลวงฉัน โปรดบอกฉันมาเดี๋ยวนี้ว่าจะจับท่านมัดไว้ได้อย่างไร”

11แซมสันกล่าวว่า “ถ้าใช้เชือกใหม่ที่ไม่เคยใช้งานมาก่อนมัดข้าอย่างแน่นหนา ข้าก็จะอ่อนแอเหมือนชายอื่น”

12ฉะนั้นเดลิลาห์จึงเอาเชือกใหม่มามัดเขาไว้ แล้วให้คนซุ่มอยู่ในอีกห้องหนึ่งเหมือนครั้งก่อน เดลิลาห์ร้องว่า “แซมสัน พวกฟีลิสเตียมาจับท่านแล้ว!” แต่แซมสันก็สะบัดเชือกออกจากแขนอย่างง่ายดายเหมือนเส้นด้าย

13เดลิลาห์กล่าวว่า “จนถึงเดี๋ยวนี้ท่านยังโกหกหลอกลวงฉัน จงบอกมาว่าจะมัดท่านไว้ได้อย่างไร”

แซมสันตอบว่า “หากทอเส้นผมทั้งเจ็ดปอยของข้าเข้าไปในหูกทอผ้า แล้วกระทกด้วยฟืม ข้าก็จะอ่อนแอเหมือนชายอื่น” ฉะนั้นเมื่อแซมสันนอนหลับ เดลิลาห์ก็ทอผมทั้งเจ็ดปอยของเขาเข้าในหูก 14แล้วกระทกด้วยฟืม

นางร้องบอกเขาอีกครั้งว่า “แซมสัน พวกฟีลิสเตียมาจับท่านแล้ว!” แซมสันก็ลุกขึ้นดึงผมออก ทำให้หูกทอผ้าเสียหาย

15แล้วเดลิลาห์ตัดพ้อว่า “ท่านพูดได้อย่างไรว่า ‘ข้ารักเจ้า’ ในเมื่อท่านไม่ไว้ใจฉันเลย? ท่านหลอกลวงฉันถึงสามครั้งแล้ว ยังไม่บอกความลับกับฉันเสียทีว่าอะไรทำให้ท่านมีเรี่ยวแรงมากถึงขนาดนี้” 16นางพิรี้พิไรกับแซมสันทุกวันจนเขาเหนื่อยหน่ายเหลือทน

17เขาจึงบอกนางทุกอย่างว่า “ข้าไม่เคยตัดผมเลย เพราะข้าเป็นนาศีร์ถวายแด่พระเจ้าตั้งแต่เกิด ถ้าหากโกนผมทิ้ง เรี่ยวแรงกำลังของข้าก็จะหมดไป ข้าจะอ่อนแอเหมือนคนอื่นๆ”

18เมื่อเดลิลาห์เห็นว่าเขาได้บอกความลับทั้งหมดแก่นางแล้ว จึงส่งข่าวไปถึงเหล่าเจ้านายฟีลิสเตียว่า “โปรดมาอีกสักครั้ง เพราะเขาบอกทุกสิ่งทุกอย่างแก่ฉันแล้ว” ดังนั้นพวกเจ้านายฟีลิสเตียจึงกลับมา พร้อมนำเงินติดตัวมาด้วย 19เดลิลาห์ให้แซมสันนอนหลับหนุนตักนาง แล้วให้คนมาโกนผมแซมสันหมดทั้งเจ็ดปอย ทำให้เรี่ยวแรงของแซมสันถดถอยลง แล้วกำลังของเขาก็หมดไป

20แล้วนางร้องว่า “แซมสัน พวกฟีลิสเตียมาจับตัวท่านแล้ว!”

แซมสันก็ตื่นขึ้น และคิดว่า “เราจะสะบัดตัวหลุดรอดไปเหมือนครั้งก่อนๆ” แต่เขาไม่รู้ว่าองค์พระผู้เป็นเจ้าทรงทิ้งเขาไปเสียแล้ว

21จากนั้นชาวฟีลิสเตียจึงจับตัวแซมสัน ควักตาทั้งสองข้างของเขาออกและนำตัวเขาไปยังกาซา ล่ามเขาด้วยโซ่ทองสัมฤทธิ์และให้โม่ข้าวอยู่ในเรือนจำ 22แต่ไม่นานผมของแซมสันก็เริ่มยาวอีก

การตายของแซมสัน

23ฝ่ายเจ้านายชาวฟีลิสเตียชุมนุมกันเพื่อถวายเครื่องบูชาครั้งใหญ่แด่พระดาโกนเทพเจ้าของพวกเขา เพื่อเป็นการเฉลิมฉลองและกล่าวว่า “เทพเจ้าของเรามอบแซมสันศัตรูของเราไว้ในมือของเราแล้ว”

24เมื่อประชาชนเห็นแซมสัน ก็ร้องสรรเสริญเทพเจ้าของตนว่า

“เทพเจ้าของเรามอบศัตรู

ไว้ในมือของเราแล้ว

คนนี้แหละที่ล้างผลาญแผ่นดินของเรา

และฆ่าพวกเราตายมากมาย”

25ขณะที่พวกเขากำลังมึนเมา พวกเขาก็ตะโกนขึ้นว่า “เอาตัวแซมสันออกมาสร้างความบันเทิงให้พวกเราเถิด” แซมสันถูกนำตัวออกจากที่คุมขัง แล้วแสดงให้พวกเขาดู

ขณะที่แซมสันถูกนำมายืนอยู่ท่ามกลางหมู่เสา 26เขาบอกคนรับใช้ที่จูงมือตนมาว่า “พาเราไปตรงที่จะคลำพบเสารองรับวิหาร เพื่อเราจะได้พิงเสา” 27ขณะนั้นภายในวิหารคลาคล่ำไปด้วยฝูงชนทั้งชายและหญิง เจ้านายฟีลิสเตียทั้งปวงก็อยู่ที่นั่นด้วย และบนดาดฟ้ามีชายหญิงประมาณสามพันคนเฝ้าดูแซมสันแสดงอยู่ 28แซมสันจึงอธิษฐานต่อองค์พระผู้เป็นเจ้าว่า “ข้าแต่พระยาห์เวห์องค์เจ้าชีวิต ขอทรงระลึกถึงข้าพระองค์ ข้าแต่พระเจ้าโปรดให้พละกำลังแก่ข้าพระองค์อีกครั้งเดียว เพื่อข้าพระองค์จะได้แก้แค้นชาวฟีลิสเตียชดเชยกับที่ต้องสูญเสียดวงตาทั้งสองข้างไป” 29จากนั้นแซมสันก็ไปที่เสาสองต้นกลางวิหารซึ่งเป็นเสารองรับวิหาร มือขวายันเสาข้างหนึ่ง มือซ้ายยันเสาอีกข้างหนึ่ง แล้วรวบรวมกำลังดันเสา 30แซมสันกล่าวว่า “เราขอตายพร้อมพวกฟีลิสเตีย!” แล้วเขาก็ดันเสาสุดแรง วิหารพังครืนลงมาทับเจ้านายฟีลิสเตียและประชากรทั้งหมดในนั้น เป็นอันว่าขณะที่แซมสันกำลังจะตาย เขาได้ฆ่าชาวฟีลิสเตียมากยิ่งกว่าตอนที่เขายังมีชีวิตอยู่

31แล้วญาติพี่น้องและครอบครัวของบิดาแซมสันก็ลงมารับศพของเขากลับไป และฝังไว้ระหว่างโศราห์กับเอชทาโอลในอุโมงค์ฝังศพของมาโนอาห์ บิดาของแซมสัน แซมสันนำ16:31 หรือวินิจฉัยอิสราเอลอยู่ยี่สิบปี