Oweruza 17 – CCL & TNCV

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Oweruza 17:1-13

Mafuno a Mika

1Munthu wina dzina lake Mika wochokera ku dziko la mapiri la Efereimu anawuza amayi ake kuti 2“Ndinamva inu mukutemberera munthu amene anaba ndalama zanu zasiliva 1,100. Ndalamazo zili ndi ine, ndinatenga ndine.”

Pamenepo amayi akewo anati, “Yehova akudalitse mwana wanga!”

3Choncho Mika anabweza ndalama 1,100 za siliva kwa amayi ake, ndipo amayi akewo anati, “Ine ndapatulira Yehova ndalama za silivazi kuti mwana wanga aseme fano ndi kulikuta ndi siliva. Ndiye tsopano ndikubwezera ndalamazo.”

4Tsono Mika atabweza ndalama zija kwa amayi ake, iwo anatengapo ndalama za siliva 200 namupatsa mmisiri wosula siliva. Iye anakonza fano, nasungunula siliva uja ndi kulikutira fano lija. Ndipo Mika anayika fanolo mʼnyumba mwake.

5Mikayu anali ndi kachisi, ndipo anapanga efodi ndi mafano otchedwa terafimu. Anapatula mwana wake mmodzi kuti akhale wansembe. 6Masiku amenewo kunalibe mfumu ku Israeli. Aliyense amachita zomwe zinamukomera.

7Ku Betelehemu mʼdziko la Yuda kunali mnyamata wina amene anali wa fuko la Levi. 8Iyeyu anachoka mu mzinda wa Betelehemu uja ku Yuda kukafuna malo ena okhala. Akuyenda, anafika ku dziko la mapiri la Efereimu ku nyumba ya Mika.

9Tsono Mika anamufunsa kuti, “Mukuchokera kuti?”

Ndipo iye anayakha kuti, “Ndine Mlevi wochokera ku Betelehemu mʼdziko la Yuda. Ndikufunafuna malo okhala.”

10Tsono Mika anati kwa iye, “Khalani ndi ine. Mukhale ngati mlangizi wanga ndi wansembe, ndipo ine ndizikupatsani ndalama za siliva khumi pa chaka komanso zovala ndi zakudya.” 11Choncho Mleviyo anavomera kuti azikhala naye, ndipo mnyamatayo anakhala ngati mmodzi mwa ana ake aamuna. 12Pambuyo pake Mika anapatula Mleviyo ndipo mnyamatayu anakhala wansembe. Tsono ankakhala mʼnyumba ya Mika. 13Ndipo Mika anati, “Tsopano ndadziwa kuti Yehova adzandikomera mtima chifukwa Mleviyu ndiye wakhala wansembe wanga.”

Thai New Contemporary Bible

ผู้วินิจฉัย 17:1-13

เทวรูปของมีคาห์

1ในแดนเทือกเขาแห่งเอฟราอิม มีชายคนหนึ่งชื่อมีคาห์ 2เขากล่าวกับมารดาว่า “เงินหนัก 1,100 เชเขล17:2 1 เชเขล คือเงินหนักประมาณ 11.5 กรัม มีค่าเท่ากับค่าแรงสองเดือน เช่นเดียวกับข้อ 3,4 และ 10ที่แม่คิดว่าถูกขโมยไปและข้าพเจ้าได้ยินแม่สาปแช่งขโมยอยู่ ที่แท้ข้าพเจ้าเอาไปเอง”

มารดาก็ตอบว่า “ขอองค์พระผู้เป็นเจ้าทรงอวยพรลูกเถิด!”

3เมื่อเขาคืนเงินหนัก 1,100 เชเขลแก่มารดาของเขา นางกล่าวว่า “แม่จะเอาเงินนี้ไปถวายแด่องค์พระผู้เป็นเจ้าสำหรับลูก แม่จะทำรูปสลักและหล่อรูปเคารพให้ลูก”

4ดังนั้นเขาจึงคืนเงินให้แก่มารดาและนางนำเงินหนัก 200 เชเขล ไปให้ช่างเงินทำรูปเคารพขึ้นมาตั้งไว้ที่บ้านของมีคาห์

5มีคาห์คนนี้มีหิ้งบูชา เขาทำเอโฟดและรูปเคารพต่างๆ และตั้งบุตรชายคนหนึ่งของตนให้เป็นปุโรหิต 6ในสมัยนั้นอิสราเอลไม่มีกษัตริย์ปกครองทุกคนต่างทำตามที่ตนเองเห็นดีเห็นชอบ

7มีหนุ่มเลวีคนหนึ่งซึ่งอาศัยอยู่ในเขตของตระกูลยูดาห์ มาจากเบธเลเฮมในยูดาห์ 8เขาจากที่นั่นมาเพื่อหาที่พักอาศัยแห่งใหม่ ระหว่างทาง17:8 หรือเพื่อมาประกอบอาชีพของเขาต่อไปเขามาถึงบ้านของมีคาห์ในแดนเทือกเขาแห่งเอฟราอิม

9มีคาห์ถามเขาว่า “ท่านมาจากไหน?”

เขาตอบว่า “ข้าพเจ้าเป็นคนเลวีมาจากเบธเลเฮมในแผ่นดินยูดาห์ กำลังหาที่พักอาศัย”

10มีคาห์จึงกล่าวว่า “มาอยู่กับข้าพเจ้าเถิด มาเป็นบิดาและเป็นปุโรหิตของข้าพเจ้า ข้าพเจ้าจะให้เงินท่านปีละ 10 เชเขลพร้อมทั้งเสื้อผ้าและอาหาร” 11ดังนั้นหนุ่มเลวีจึงตกลงอยู่กับเขา เขาเป็นเหมือนบุตรชายคนหนึ่งของมีคาห์ 12จากนั้นมีคาห์แต่งตั้งชายหนุ่มเลวีผู้นั้นให้เป็นปุโรหิตอาศัยอยู่ในบ้านของเขา 13และมีคาห์กล่าวว่า “บัดนี้ข้าพเจ้ารู้แล้วว่าองค์พระผู้เป็นเจ้าจะทรงดีต่อข้าพเจ้า เพราะว่าชาวเลวีคนนี้มาเป็นปุโรหิตของข้าพเจ้า”