Nyimbo ya Solomoni 8 – CCL & NIV

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Nyimbo ya Solomoni 8:1-14

1Ukanakhala kuti ndiwe mlongo wanga,

amene anayamwa mawere a amayi anga!

Ndikanakumana nawe pa njira,

ndikanakupsompsona,

ndipo palibe wina aliyense akanandinyoza.

2Ndikanakutenga

ndi kukulowetsa mʼnyumba ya amayi anga,

amayi amene anandiphunzitsa,

ndikanakupatsa vinyo wotsekemera kuti umwe,

zotsekemera za makangadza.

3Mutu wanga watsamira dzanja lake lamanzere

ndipo dzanja lake lamanja landikumbatira.

4Inu akazi a ku Yerusalemu, ndithu ndikukupemphani:

musachigwedeze chikondi kapena kuchiutsa

mpaka pamene chifunire ichocho.

Abwenzi

5Kodi ndani uyo akutuluka ku chipululuyo,

atatsamira wokondedwa wakeyo?

Mkazi

Ndinakudzutsa pa tsinde pa mtengo wa apulosi,

pamenepo ndi pamene amayi anachirira,

pamenepo ndi pamene wokubereka anamva ululu pokubala iweyo.

6Undiyike pamtima pako ngati chidindo,

ngati chidindo cha pa dzanja lako;

pakuti chikondi nʼchamphamvu ngati imfa,

nsanje ndiyaliwuma ngati manda.

Chikondi chimachita kuti lawilawi

ngati malawi a moto wamphamvu.

7Madzi ochuluka sangachizimitse chikondi,

mitsinje singachikokolole chikondicho.

Ngati wina apereka chuma chonse

cha mʼnyumba mwake chifukwa cha chikondi,

adzangonyozeka nazo kotheratu.

Abwenzi

8Ife tili naye mlongo wathu wamngʼono,

koma alibe mawere,

kodi tidzamuchitira chiyani mlongo wathuyu

pa tsiku limene adzamufunsire?

9Ngati iye ndi khoma,

tidzamumangira nsanja ya siliva.

Ngati iye ndi chitseko,

tidzamutchinga ndi matabwa a mkungudza.

Mkazi

10Ine ndili ngati khoma,

ndipo mawere anga ndi nsanja zake.

Tsono mʼmaso mwa bwenzi langa

ndine wobweretsa mtendere.

11Solomoni anali ndi munda wampesa ku Baala-Hamoni;

iyeyo anabwereketsa munda wamphesawo kwa alimi,

aliyense mwa iwo ankayenera kupereka

ndalama zasiliva 1,000 mʼmalo mwa zipatso zake.

12Koma munda wanga wampesa ndi wangawanga ndiponso wa ine ndekha.

Iwe Solomoni, khala nazo ndalama zasiliva 1,000

ndipo ndalama zasiliva 200 ndi za amene akusamalira mundawo.

Mwamuna

13Iwe amene umakhala mʼminda

uli pamodzi ndi anzako,

ndilole kuti ndimve liwu lako!

Mkazi

14Fulumira wokondedwa wanga,

ndipo ukhale ngati gwape

kapena mwana wa mbawala

wothamanga mʼmapiri mʼmene mumamera mbewu zokometsera chakudya.

New International Version

Song of Songs 8:1-14

1If only you were to me like a brother,

who was nursed at my mother’s breasts!

Then, if I found you outside,

I would kiss you,

and no one would despise me.

2I would lead you

and bring you to my mother’s house—

she who has taught me.

I would give you spiced wine to drink,

the nectar of my pomegranates.

3His left arm is under my head

and his right arm embraces me.

4Daughters of Jerusalem, I charge you:

Do not arouse or awaken love

until it so desires.

Friends

5Who is this coming up from the wilderness

leaning on her beloved?

She

Under the apple tree I roused you;

there your mother conceived you,

there she who was in labor gave you birth.

6Place me like a seal over your heart,

like a seal on your arm;

for love is as strong as death,

its jealousy8:6 Or ardor unyielding as the grave.

It burns like blazing fire,

like a mighty flame.8:6 Or fire, / like the very flame of the Lord

7Many waters cannot quench love;

rivers cannot sweep it away.

If one were to give

all the wealth of one’s house for love,

it8:7 Or he would be utterly scorned.

Friends

8We have a little sister,

and her breasts are not yet grown.

What shall we do for our sister

on the day she is spoken for?

9If she is a wall,

we will build towers of silver on her.

If she is a door,

we will enclose her with panels of cedar.

She

10I am a wall,

and my breasts are like towers.

Thus I have become in his eyes

like one bringing contentment.

11Solomon had a vineyard in Baal Hamon;

he let out his vineyard to tenants.

Each was to bring for its fruit

a thousand shekels8:11 That is, about 25 pounds or about 12 kilograms; also in verse 12 of silver.

12But my own vineyard is mine to give;

the thousand shekels are for you, Solomon,

and two hundred8:12 That is, about 5 pounds or about 2.3 kilograms are for those who tend its fruit.

He

13You who dwell in the gardens

with friends in attendance,

let me hear your voice!

She

14Come away, my beloved,

and be like a gazelle

or like a young stag

on the spice-laden mountains.