Nyimbo ya Solomoni 2 – CCL & NASV

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Nyimbo ya Solomoni 2:1-17

Mkazi

1Ine ndine duwa la ku Saroni,

duwa lokongola la ku zigwa.

Mwamuna

2Monga duwa lokongola pakati pa minga

ndi momwe alili wokondedwa wanga pakati pa atsikana.

Mkazi

3Monga mtengo wa apulosi pakati pa mitengo ya mʼnkhalango

ndi momwe alili bwenzi langa pakati pa anyamata.

Ndimakondwera kukhala pansi pa mthunzi wako,

ndipo chipatso chake ndi chokoma mʼkamwa mwanga.

4Iye wanditengera ku nyumba yaphwando,

ndipo mbendera yake yozika pa ine ndi chikondi.

5Undidyetse keke ya mphesa zowuma,

unditsitsimutse ndi ma apulosi,

pakuti chikondi chandifowoketsa.

6Mutu wanga watsamira dzanja lake lamanzere,

ndipo dzanja lake lamanja landikumbatira.

7Inu akazi a ku Yerusalemu, ndithu ndikukupemphani

pali gwape ndi mbawala yayikazi zakuthengo:

Musachigwedeze chikondi kapena kuchiutsa

mpaka pamene chifunire ichocho.

8Tamverani bwenzi langa!

Taonani! Uyu akubwera apayu,

akulumphalumpha pa mapiri,

akujowajowa pa zitunda.

9Bwenzi langa ali ngati gwape kapena mwana wa mbawala.

Taonani! Uyo wayima kuseri kwa khoma lathulo,

akusuzumira mʼmazenera,

akuyangʼana pa mpata wa zenera.

10Bwenzi langa anayankha ndipo anati kwa ine,

“Dzuka bwenzi langa,

wokongola wanga, ndipo tiye tizipita.

11Ona, nyengo yozizira yatha;

mvula yatha ndipo yapitiratu.

12Maluwa ayamba kuoneka pa dziko lapansi;

nthawi yoyimba yafika,

kulira kwa njiwa kukumveka

mʼdziko lathu.

13Mtengo wankhuyu ukubereka zipatso zake zoyambirira;

mitengo ya mpesa ya maluwa ikutulutsa fungo lake.

Dzuka bwenzi langa, wokongola wanga

tiye tizipita.”

Mwamuna

14Nkhunda yanga yokhala mʼmingʼalu ya thanthwe,

mʼmalo obisala a mʼmbali mwa phiri,

onetsa nkhope yako,

nʼtamvako liwu lako;

pakuti liwu lako ndi lokoma,

ndipo nkhope yako ndi yokongola.

15Mutigwirire nkhandwe,

nkhandwe zingʼonozingʼono

zimene zikuwononga minda ya mpesa,

minda yathu ya mpesa imene yayamba maluwa.

Mkazi

16Bwenzi langa ndi wangadi ndipo ine ndine wake;

amadyetsa gulu lake la ziweto pakati pa maluwa okongola.

17Kamphepo kamadzulo kakayamba kuwuzira

ndipo mithunzi ikayamba kuthawa,

unyamuke bwenzi langa,

ndipo ukhale ngati gwape

kapena ngati mwana wa mbawala

pakati pa mapiri azigwembezigwembe.

New Amharic Standard Version

ማሕልየ መሓልይ 2:1-17

ሙሽራዪቱ

1እኔ የሳሮን ጽጌረዳ፣

የሸለቆም አበባ2፥1 ጸደይ ከመሆኑ ቀደም ብሎ የሚበቅል ቢጫ፣ ሐምራዊና ነጭ ቀለም ያሉት የአበባ ተክል ዝርያ ሊሆን ይችላል። ነኝ።

ሙሽራው

2በእሾኽ መካከል እንዳለ ውብ አበባ፣

ውዴም በቈነጃጅት መካከል እንዲሁ ናት።

ሙሽራዪቱ

3በዱር ዛፎች መካከል እንዳለ እንኮይ፣

ውዴም በጕልማሶች መካከል እንዲሁ ነው፤

በጥላው ሥር መቀመጥ ደስ ያሰኛል፤

የፍሬውም ጣፋጭነት ያረካኛል።

4ወደ ግብዣው አዳራሽ ወሰደኝ፤

በእኔ ላይ ያለው ዐላማው ፍቅር ነው።

5በዘቢብ አበረታቱኝ፤

በእንኮይም አስደስቱኝ፤

በፍቅሩ ተይዤ ታምሜአለሁና።

6ግራ እጁን ተንተርሻለሁ፤

ቀኝ እጁም ዐቅፎኛል።

7እናንት የኢየሩሳሌም ቈነጃጅት፣

ራሱ እስኪፈልግ ድረስ፣

ፍቅርን እንዳታስነሡት ወይም እንዳትቀሰቅሱት፣

በሚዳቋና በሜዳ ዋሊያ አማጥናችኋለሁ።

8እነሆ፤ የውዴ ድምፅ

በተራሮች ላይ እየዘለለ፣

በኰረብቶችም ላይ እየተወረወረ፣

ሲመጣ ይሰማኛል።

9ውዴ ሚዳቋ ወይም የዋሊያ ግልገል ይመስላል፤

እነሆ፤ ከቤታችን ግድግዳ ኋላ ቆሟል፤

በመስኮት ትክ ብሎ ወደ ውስጥ ያያል፤

በፍርግርጉም እያሾለከ ይመለከታል።

10ውዴም እንዲህ አለኝ፤

“ፍቅሬ ሆይ፤ ተነሺ፤

አንቺ የእኔ ቈንጆ፤ ከእኔ ጋር ነዪ።

11እነሆ! ክረምቱ ዐለፈ፤

ዝናቡም አባርቶ አበቃ፤

12አበቦች በምድር ላይ ታዩ፤

የዝማሬ ወቅት መጥቷል፤

የርግቦችም ድምፅ፣

በምድራችን ተሰማ።

13በለስ ፍሬዋን አፈራች፤

ያበቡ ወይኖችም መዐዛቸውን ሰጡ፤

ፍቅሬ ሆይ፤ ተነሺና ነዪ፤

አንቺ የእኔ ቈንጆ፤ ከእኔ ጋር ነዪ።”

ሙሽራው

14አንቺ በገደል ዐለት ንቃቃት፣

በተራሮችም ባሉ መደበቂያ ስፍራዎች ውስጥ ያለሽ ርግቤ ሆይ!

ፊትሽን አሳዪኝ፤

ድምፅሽንም አሰሚኝ፤

ድምፅሽ ጣፋጭ፣

መልክሽም ውብ ነውና።

15የወይን ተክሉን ቦታ፣

በማበብ ላይ ያለውን የወይን ተክል ቦታችንን፣

የሚያጠፉትን ቀበሮዎች፣

እነዚያን ትንንሽ ቀበሮዎች አጥምዳችሁ ያዙልን።

ሙሽራዪቱ

16ውዴ የእኔ ነው፤ እኔም የእርሱ ነኝ፣

እርሱ መንጋውን በውብ አበቦች መካከል ያሰማራል።

17ጎሕ ከመቅደዱ በፊት፣

ጥላውም ሳይሸሽ፣

ውዴ ሆይ፤ ተመለስ፤

ሚዳቋን ምሰል፤

ወይም በወጣ ገባ ኰረብቶች2፥17 ወይም የቤጠር ኰረብቶች

እንዳለው የዋሊያ ግልገል ሁን።