Nyimbo ya Solomoni 1 – CCL & NASV

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Nyimbo ya Solomoni 1:1-17

1Nyimbo ya Solomoni, nyimbo yoposa nyimbo zonse.

Mkazi

2Undipsompsone ndi milomo yako

chifukwa chikondi chako nʼchokoma kuposa vinyo.

3Mafuta ako odzola ndi onunkhira bwino;

dzina lako lili ngati mafuta onunkhira otsanulidwa.

Nʼchifukwa chake atsikana amakukonda!

4Nditenge ndipo ndizikutsata, tiye tifulumire!

Mfumu indilowetse mʼchipinda chake.

Abwenzi

Ife timasangalala ndi kukondwera nawe,

tidzatamanda chikondi chako kupambana vinyo.

Mkazi

Amachita bwinotu potamanda iwe!

5Ndine wakuda, komatu ndine wokongola,

inu akazi a ku Yerusalemu,

ine ndine wakuda ngati tenti ya ku Kedara,

ngati makatani a tenti ya Solomoni.

6Musandiyangʼane monyoza chifukwa ndine wakuda,

ndine wakuda chifukwa cha dzuwa.

Alongo anga anandikwiyira

ndipo anandigwiritsa ntchito mʼminda ya mpesa;

munda wangawanga sindinawusamalire.

7Ndiwuze iwe, amene ndimakukonda, kumene umadyetsa ziweto zako

ndi kumene umagoneka nkhosa zako nthawi yamasana.

Ndikhalirenji ngati mkazi wachiwerewere

pambali pa ziweto za abwenzi ako?

Abwenzi

8Ngati sukudziwa iwe wokongola kwambiri kuposa akazi ena,

ngati sukudziwa, tsatira makwalala a nkhosa

ndipo udyetse ana ambuzi

pambali pa matenti a abusa.

Mwamuna

9Iwe bwenzi langa,

uli ngati kavalo wamkazi ku magaleta a Farao.

10Masaya ako ndi okongola ndi ndolo zamʼmakutuzo,

khosi lako likukongola ndi mikanda yamiyala yamtengowapatali.

11Tidzakupangira ndolo zagolide

zokongoletsedwa ndi mikanda yasiliva.

Mkazi

12Pamene mfumu inali pa malo ake odyera,

mafuta anga onunkhira anamveka fungo lake.

13Wokondedwa wanga ali ngati kathumba ka mure kwa ine,

kamene kamakhala pakati pa mawere angawa.

14Wokondedwa wanga ali ngati mpukutu wa maluwa ofiira,

ochokera ku minda ya mpesa ya ku Eni-Gedi.

Mwamuna

15Iwe wokondedwa wanga, ndiwe wokongoladi!

Ndithu, ndiwe chiphadzuwa,

maso ako ali ngati nkhunda.

Mkazi

16Iwe bwenzi langa, ndiwe wokongoladi!

Ndithu, ndiwe wokongoladi kwambiri!

Ndipo malo athu ogonapo ndi msipu wobiriwira.

Mwamuna

17Mitanda ya nyumba yathu ndi ya mkungudza,

phaso lake ndi la mtengo wa payini.

New Amharic Standard Version

ማሕልየ መሓልይ 1:1-17

1ከመዝሙር ሁሉ የሚበልጥ የሰሎሞን መዝሙር።

ሙሽራዪቱ

2በከንፈሩ መሳም ይሳመኝ

ፍቅርህ ከወይን ጠጅ ይልቅ ደስ ያሰኛልና።

3የሽቱህ መዐዛ ደስ ያሰኛል፤

ስምህ እንደሚፈስስ ሽቱ ነው፤

ታዲያ ቈነጃጅት ቢወድዱህ ምን ያስደንቃል!

4ይዘኸኝ ሂድ፤ እንፍጠን፤

ንጉሡ ወደ ዕልፍኞቹ አምጥቶኛል።

ባልንጀሮቿ

በአንተ1፥4 በዕብራይስጥ ነጠላ ተባዕታይ ነው። ደስ ይለናል፤ ሐሤትም እናደርጋለን፤

ከወይን ጠጅ ይልቅ ፍቅርህን እንወድሳለን።

ሙሽራዪቱ

አንተን እንደዚህ ማፍቀራቸው ትክክል ነው።

5እናንት የኢየሩሳሌም ቈነጃጅት ሆይ፤

እኔ ጥቍር ነኝ፤ ይሁን እንጂ ውብ ነኝ፤

ጥቍረቴ እንደ ቄዳር ድንኳኖች፣

እንደ ሰሎሞን1፥5 ወይም ሳልማ ቤተ መንግሥት መጋረጃዎችም ነው።

6ጥቍር ስለሆንሁ ትኵር ብላችሁ አትዩኝ፤

መልኬን ያጠቈረው ፀሓይ ነውና፤

የእናቴ ልጆች ወንድሞቼ ተቈጡኝ፤

የወይን ተክል ቦታዎችም ጠባቂ አደረጉኝ፤

የራሴን የወይን ተክል ቦታ ተውሁት።

7ውዴ ሆይ፤ መንጋህን የት እንደምታሰማራ፣

በቀትርም የት እንደምትመስጋቸው

እባክህ ንገረኝ፤

በወዳጆችህ መንጎች ኋላ፣

ፊቷን ሸፍና እንደምትቅበዘበዝ ሴት ለምን ልሁን?

ባልንጀሮቿ

8አንቺ ከሴቶች ሁሉ ይበልጥ የተዋብሽ ሆይ፤ የማታውቂ ከሆነ፣

የበጎቹን ዱካ ተከተዪ፤

የፍየል ግልገሎችሽንም፣

በእረኞቹ ድንኳን አጠገብ አሰማሪ።

ሙሽራው

9ውዴ ሆይ፤ የፈርዖንን ሠረገሎች ከሚስቡ ፈረሶች መካከል፣

በአንዲቱ ባዝራ መሰልሁሽ።

10ጕንጮችሽ በጕትቻ፣

ዐንገትሽም በዕንቍ ሐብል አጊጠዋል።

11እኛም ባለ ብር ፈርጥ፣

የወርቅ ጕትቻ እናሠራልሻለን።

ሙሽራዪቱ

12ንጉሡ ማእዱ ላይ ሳለ፣

ሽቱዬ መዐዛውን ናኘው።

13ውዴ ለእኔ በጡቶቼ መካከል እንዳረፈ፣

በመቋጠሪያ እንዳለ ከርቤ ነው።

14ውዴ ለእኔ ከዓይንጋዲ የወይን ተክል ቦታ

እንደ መጣ የሄና አበባ ዕቅፍ ነው።

ሙሽራው

15ውዴ ሆይ፤ እንዴት ውብ ነሽ!

እንዴትስ ያለሽ ቈንጆ ነሽ!

ዐይኖችሽም እንደ ርግብ ዐይኖች ናቸው።

ሙሽራዪቱ

16አንተ ውዴ ሆይ፤ እንዴት ውብ ነህ!

እንዴትስ ታምራለህ!

ዐልጋችንም እንደ ለምለም ሣር ነው።

ሙሽራው

17የቤታችን ተሸካሚዎች ዝግባዎች፣

የጣራችን ማዋቀሪያዎችም ጥዶች ናቸው።