Numeri 18 – CCL & CARS

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Numeri 18:1-32

Ntchito za Ansembe ndi Alevi

1Yehova anawuza Aaroni kuti, “Iwe, ana ako aamuna ndi banja la abambo ako mudzasenza tchimo la malo wopatulika, koma iwe ndi ana ako aamuna okha mudzasenza tchimo lokhudza unsembe wanu. 2Ubweretse Alevi, abale ako, kuchokera ku fuko la abambo ako kuti azikhala ndi iwe ndi kumakuthandiza pamodzi ndi ana ako amuna pamene mukutumikira mu tenti ya umboni. 3Iwowo azikutumikirani ndipo azichita ntchito zonse za ku tenti, koma asamafike pafupi ndi zipangizo za ku malo opatulika kapena guwa lansembe, kuopa kuti iwo ndi inu mungafe. 4Azikhala ndi inu ndipo azisamalira ntchito yonse ya mu tenti ya msonkhano koma munthu wina aliyense wapadera sayenera kufika pafupi nanu.

5“Inuyo muzisamalira malo wopatulika ndi guwa lansembe, kuti ukali wa Yehova usawagwerenso Aisraeli. 6Ine mwini ndasankha Alevi, abale ako, pakati pa Aisraeli ngati mphatso yako ndipo aperekedwa kwa Yehova kuti azigwira ntchito ku tenti ya msonkhano. 7Koma iwe wekha ndi ana ako aamuna muzitumikira ngati ansembe ndi zina zonse zokhudza pa guwa lansembe ndi za mʼkati mwa malo wopatulika kwambiri. Ndikukupatsani mphatso ya utumiki wa unsembe. Aliyense woyandikira malo wopatulika ayenera kuphedwa.

Zopereka za Ansembe ndi Alevi

8“Kenaka Yehova anati kwa Aaroni, ona, Ine mwini ndikukuyika kuti ukhale woyangʼanira zopereka zobwera kwa Ine; zopereka zonse zopatulika za Aisraeli zimene amapereka kwa ine ndi kuzipereka kwa iwe ndi ana ako aamuna ngati gawo lanu la nthawi zonse. 9Uzilandiranso gawo la zopereka zopatulika kwambiri zomwe sizinawotchedwe pa moto. Kuchokera pa mphatso zonse zimene amabweretsa kwa Ine ngati zopatulika kwambiri, nsembe zachakudya kapena nsembe zopepesera machimo, gawo limenelo ndi lako ndi ana ako aamuna. 10Muzidya zimenezo ngati zinthu zopatulika kwambiri; mwamuna aliyense adyeko. Uzitenge kukhala zopatulika.

11“Izinso ndi zako: chilichonse chopatulidwa kuchokera ku mphatso zoweyula za Aisraeli ndapereka kwa iwe ndi ana ako aamuna ndi aakazi ngati gawo lako la nthawi zonse. Aliyense wa mʼnyumba mwako amene ali woyeretsedwa monga mwa mwambo angathe kudyako.

12“Ndikukupatsani mafuta onse abwino kwambiri a olivi ndi vinyo yense watsopano wabwino kwambiri ndi tirigu yense zomwe Aisraeli amapereka kwa Yehova ngati zipatso zoyamba pa zokolola zawo. 13Zipatso zonse zoyamba kucha za mʼdziko lawo zomwe amapereka kwa Yehova zidzakhala zako. Aliyense mʼnyumba mwako amene ali woyeretsedwa angathe kudyako.

14“Chilichonse mu Israeli chomwe chapatulidwira Yehova ndi chako. 15Chilichonse choyamba kubadwa kwa munthu kaya nyama, chomwe chaperekedwa kwa Yehova ndi chako. Koma uyenera kuwombola mwana aliyense wamwamuna ndi mwana aliyense woyamba wa nyama zodetsedwa. 16Pamene zili ndi mwezi umodzi wa kubadwa, uziwombole pa mtengo wowombolera wa ndalama zisanu zasiliva, monga mwa ndalama za ku malo wopatulika.

17“Koma usawombole ana oyamba kubadwa a ngʼombe, nkhosa kapena mbuzi. Iwo ndi opatulika. Uwaze magazi a nyamazi pa guwa lansembe ndi kutentha mafuta ake ngati nsembe yotentha ndi moto kuti likhale fungo lokoma kwa Yehova. 18Nyama yake ikhale yanu monga momwe chimakhalira chidale cha nsembe yoweyula ndi ntchafu za miyendo ya kumanja, zonsezi ndi zako. 19Zonse zimene mwazichotsa ku zopereka zoyera zomwe Aisraeli anapereka kwa Yehova ndazipereka kwa iwe ndi ana ako aamuna ndi aakazi ngati gawo lanu nthawi zonse. Ili ndi pangano losatha la mchere pamaso pa Yehova kwa iwe ndi ana ako.”

20Ndipo Yehova anati kwa Aaroni, “Iweyo sudzakhala ndi cholowa mʼdziko lawo, ndiponso sudzalandira gawo lililonse pakati pawo. Ine ndine gawo lako ndi cholowa chako pakati pa Aisraeli.

21“Taonani, ndawapatsa Alevi chakhumi chonse mu Israeli ngati cholowa chawo chifukwa cha ntchito ya ku tenti ya msonkhano. 22Kuyambira tsopano mpaka mʼtsogolo Aisraeli asamapite pafupi ndi tenti ya msonkhano. Ngati atero adzasenza zotsatira za tchimo lawo ndipo adzafa. 23Alevi ndi amene azidzagwira ntchito ya ku tenti ya msonkhano ndipo adzalangidwa chilichonse chikalakwika. Ili ndi lamulo losatha kwa mibado yawo yonse. Iwowo sadzalandira cholowa pakati pa Aisraeli. 24Mʼmalo mwake, ndikuwapatsa Aleviwo chakhumi ngati cholowa chawo chimene Aisraeli amapereka kwa Yehova. Nʼchifukwa chake zokhudza iwo ndinati: ‘Sadzakhala ndi cholowa pakati pa Aisraeli.’ ”

25Yehova anati kwa Mose, 26“Yankhula ndi Alevi ndi kunena nawo kuti, ‘Pamene mulandira chakhumi kuchoka kwa Aisraeli chimene ndimakupatsani ngati cholowa chanu, muyenera kupereka chakhumi cha choperekacho kwa Yehova. 27Chopereka chanucho chidzawerengedwa kwa inu ngati tirigu wochokera kopunthira kapena ngati mphesa zopsinya kuchokera kopsinyira mphesa. 28Mwa njira imeneyi inunso muzipereka chopereka kwa Yehova kuchokera ku chakhumi chanu chilichonse chimene mumalandira kuchokera kwa Aisraeli. Kuchokera ku chakhumicho muziperekako gawo la Yehova kwa Aaroni, wansembe. 29Muyenera kupereka monga gawo la Yehova magawo abwino kwambiri ndi opatulika a chilichonse chimene chapatsidwa kwa inu.’

30“Nena kwa Alevi: ‘Pamene mupereka gawo labwino lopambana zonse, gawo limenelo lidzawerengedwa kwa inu ngati lochokera popunthira tirigu kapenanso kopsinyira mphesa. 31Inu ndi a pa banja panu mungathe kudyera zimenezi paliponse chifukwa ndi malipiro a ntchito yanu ya ku tenti ya msonkhano. 32Popereka gawo labwino kwambirilo simudzapezeka olakwa. Mukatero simudzadetsa zopereka zoyera za Aisraeli, ndipo simudzafa.’ ”

Священное Писание

Числа 18:1-32

Обязанности священнослужителей и левитов

1Вечный сказал Харуну:

– Ты, твои сыновья и все остальные члены рода Леви будете в ответе за осквернение святилища, но только ты и твои сыновья будете в ответе за осквернение священства. 2Возьми к себе своих собратьев левитов из рода твоего предка, чтобы они были с тобой и помогали тебе, когда ты и твои сыновья будете служить перед шатром соглашения. 3Пусть они будут в ответе перед тобой и исполняют при шатре все обязанности, но не приближаются ни к утвари святилища, ни к жертвеннику, иначе умрут и они, и вы. 4Пусть они будут при тебе, чтобы заботиться о шатре встречи, исполняя при нём всю положенную работу, и пусть никого больше с вами не будет.

5Вашей заботе вверены святилище и жертвенник, чтобы Мой гнев впредь не падал на исраильтян. 6Я Сам избрал ваших собратьев левитов среди исраильтян и дарю их вам в помощники. Они посвящены Мне, чтобы работать при шатре встречи. 7Но только тебе и твоим сыновьям можно исполнять священнические обязанности во всём, что связано с жертвенником, и с тем, что за завесой. Я даю вам священство как дар. Всякий посторонний, кто приблизится к святилищу, должен быть предан смерти.

Приношения для священнослужителей и левитов

8Вечный сказал Харуну:

– Я Сам поручил тебе наблюдать за всеми приношениями, которые Мне приносят. Все священные приношения, которые приносят Мне исраильтяне, Я отдаю тебе и твоим сыновьям как вашу часть и постоянную долю. 9Тебе будет доставаться та часть самых священных жертвоприношений, которую не предают огню. Во всех самых священных приношениях, которые приносят Мне в дар, будь то хлебное приношение, жертва за грех или жертва повинности, эта часть принадлежит тебе и твоим сыновьям. 10Ешьте её как великую святыню; её может есть любой мужчина. Она будет святыней для вас.

11Вот что ещё принадлежит тебе: все жертвы потрясания, которые исраильтяне приносят в дар. Я даю это тебе и твоим сыновьям и дочерям как постоянную долю. Всякий в твоём доме, кто чист, может это есть.

12Я отдаю тебе всё лучшее оливковое масло, молодое вино и зерно, которые приносят Мне как первые плоды урожая. 13Все первые плоды земли, которые приносят Мне, будут твоими. Всякий в твоём доме, кто чист, может это есть.

14Всё в Исраиле, что посвящено Вечному, твоё. 15Первый ребёнок в семье и первородное животное, которое приносят Вечному, твоё. Но выкупай любого сына-первенца и любого первородного самца из нечистых животных. 16Когда им исполнится месяц, выкупи их, заплатив шестьдесят граммов серебра18:16 Букв.: «пять шекелей серебра, шекелей святилища, в одном шекеле двадцать гер». Шекель святилища – стандартная мера, которой пользовались священнослужители шатра и храма..

17Но не выкупай первородных волов, овец или коз; они священны. Окропи жертвенник их кровью и сожги их жир как огненную жертву, благоухание, приятное Вечному. 18Их мясо отойдёт тебе, подобно грудине из приношения потрясания и правому бедру. 19Все священные приношения, которые исраильтяне приносят Вечному, Я отдаю тебе и твоим сыновьям и дочерям как вашу постоянную долю. Это вечное, нерасторжимое соглашение18:19 Букв.: «вечное соглашение соли». На Востоке совместно съеденная соль служила символом нерасторжимости договора между людьми. Кроме того, соль говорила о долговечности договора, так как она сохраняет продукты, не давая им испортиться (см. Лев. 2:13; 2 Лет. 13:5). между Вечным, тобой и твоим потомством.

20Вечный сказал Харуну:

– У тебя не будет ни надела на их земле, ни доли среди них; Я – твоя доля и твой надел среди исраильтян. 21Я отдаю левитам в удел все десятины в Исраиле за их службу при шатре встречи. 22Пусть исраильтяне впредь не приближаются к шатру встречи, иначе они навлекут на себя кару и умрут. 23Пусть одни левиты исполняют работу при шатре встречи и будут нести ответственность за его осквернение. Это установление для грядущих поколений будет вечным. Они не получат надел среди исраильтян. 24Вместо этого Я даю левитам в удел десятины, которые исраильтяне приносят Мне в дар. Поэтому Я и сказал о них: «У них не будет надела среди исраильтян».

25Вечный сказал Мусе:

26– Поговори с левитами и скажи им: «Когда вы получаете от исраильтян десятину, которую Я даю вам в удел, то приносите её десятую часть в дар Мне. 27Ваше приношение будет зачтено вам, как зерно с гумна или сок из давильни. 28Точно так же отделяйте Мне в дар часть всех десятин, которые получаете от исраильтян. Отдавайте Мою часть из этих десятин священнослужителю Харуну. 29Приносите Мне в дар самую лучшую и священную часть всего, что вам дают».

30Скажи левитам: «Когда вы приносите в дар лучшую часть, она будет зачтена вам, как взятая с вашего гумна или давильни. 31Вы и ваши домочадцы можете есть остаток где угодно – это вознаграждение за вашу службу при шатре встречи. 32Вы не навлечёте на себя наказание, делая это, если будете приносить в дар лучшую часть. Тогда вы не оскверните священных приношений исраильтян и не умрёте».