Numeri 17 – CCL & NIRV

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Numeri 17:1-13

Kuphukira kwa Ndodo ya Aaroni

1Yehova anawuza Mose kuti, 2“Yankhula ndi Aisraeli ndipo akupatse ndodo khumi ndi ziwiri, imodzi kuchokera kwa mtsogoleri wa fuko lililonse. Ulembe dzina la munthu aliyense pa ndodo yake. 3Pa ndodo ya Levi ulembepo dzina la Aaroni, chifukwa pafunika ndodo imodzi ya mtsogoleri pa fuko lililonse. 4Uyike ndodozo mu tenti ya msonkhano, kutsogolo kwa Bokosi la Umboni, kumene ndimakumana nawe. 5Ndodo ya munthu amene ndamusankha idzachita maluwa potero ndidzaletsa madandawulo osatha a Aisraeli otsutsana nawe.”

6Choncho Mose anayankhula ndi Aisraeli, ndipo atsogoleri awo anapereka ndodo khumi ndi ziwiri, imodzi kuchokera kwa mtsogoleri wa fuko lililonse ndipo ndodo ya Aaroni inali pakati pa ndodo zawozo. 7Mose anayika ndodozo pamaso pa Yehova mu tenti ya msonkhano.

8Pa tsiku lotsatira Mose analowa mu tenti ya msonkhanoyo ndipo anaona kuti ndodo ya Aaroni, yomwe inkayimira fuko la Levi, sinangophuka masamba chabe, komanso inachita maluwa nʼkubala zipatso za alimondi. 9Choncho Mose anatulutsa ndodo zonse pamaso pa Yehova napita nazo kwa Aisraeli onse. Iwowo anaziona ndipo munthu aliyense anatenga ndodo yake.

10Yehova anawuza Mose kuti, “Bwezera ndodo ya Aaroni patsogolo pa Bokosi la Umboni, kuti chikhale chizindikiro cha kuwukira kwawo. Zimenezi zidzathetsa kudandaula kwawo kotsutsana nane, kuopa kuti angafe.” 11Mose anachita monga Yehova anamulamulira.

12Aisraeli anati kwa Mose, “Tikufa! Tatayika, tonse tatayika! 13Aliyense woyandikira chihema adzafa. Kodi ndiye kuti tonse tikufa?”

New International Reader’s Version

Numbers 17:1-13

Aaron’s Walking Stick Produces Buds

1The Lord said to Moses, 2“Speak to the Israelites. Get 12 walking sticks from them. Get one from the leader of each of Israel’s tribes. Write the name of each man on his walking stick. 3Write Aaron’s name on Levi’s walking stick. There must be one stick for the head of each of Israel’s tribes. 4Put the walking sticks in the tent of meeting. Place them in front of the ark where the tablets of the covenant law are kept. That is where I meet with you. 5The walking stick that belongs to the man I choose will begin to grow new shoots. The Israelites are never happy with what you do. I will put an end to what they are saying.”

6So Moses spoke to the Israelites. Their leaders gave him 12 walking sticks. They gave one for the leader of each of Israel’s tribes. Aaron’s walking stick was among them. 7Moses put the sticks in front of the Lord in the tent where the tablets of the covenant law were kept.

8The next day Moses entered the tent. He looked at Aaron’s walking stick. It stood for the tribe of Levi. Moses saw that it had begun to grow new shoots. It had also produced buds and flowers and almonds. 9Then Moses brought out all the walking sticks from in front of the Lord. He brought them to all the Israelites. They looked at them. And each man took his own walking stick.

10The Lord said to Moses, “Put Aaron’s walking stick back in front of the ark where the tablets of the covenant law are kept. The stick will be kept there as a warning to those who refuse to obey. They are never happy with what I do. Aaron’s walking stick will put an end to what they are saying. Then they will not die.” 11Moses did just as the Lord commanded him.

12The Israelites said to Moses, “We’ll die! We are lost! All of us are lost! 13Anyone who even comes near the Lord’s holy tent will die. Are all of us going to die?”